< Salmos 97 >

1 ¡El Señor reina! ¡Qué la tierra se alegre, y que las costas distantes se llenen de alegría!
Yehova akulamulira, dziko lapansi lisangalale; magombe akutali akondwere.
2 Él está rodeado de nubes y densas tinieblas; su trono está fundado en la justicia y la verdad.
Mitambo ndi mdima waukulu zamuzungulira; chilungamo ndi kuweruza molungama ndiwo maziko a mpando wake waufumu.
3 Las llamas le proceden, quemando a sus enemigos de cada lado.
Moto umapita patsogolo pake ndi kunyeketsa amaliwongo kumbali zonse.
4 Sus rayos de luz iluminan el mundo; la tierra observa y tiembla.
Zingʼaningʼani zake zimawalitsa dziko lonse; dziko lapansi limaona ndipo limanjenjemera.
5 Las montañas se derriten como cera en la presencia del Señor, ante el Señor de toda la tierra.
Mapiri amasungunuka ngati phula pamaso pa Yehova, pamaso pa Ambuye a dziko lonse lapansi.
6 Los cielos proclaman su bondad; todos ven su gloria.
Mayiko akumwamba amalengeza za chilungamo chake, ndipo mitundu yonse ya anthu imaona ulemerero wake.
7 Todos aquellos que adoran ídolos son humillados, todos los que están orgullosos de sus ídolos, porque todos los “dioses” se postran ante él.
Onse amene amalambira mafano osema amachititsidwa manyazi, iwo amene amanyadira mafano; mulambireni, inu milungu yonse!
8 Jerusalén oye esto y celebra; todos los pueblos de Judá están felices por tus juicios, Señor.
Ziyoni akumva ndipo akukondwera, midzi ya Yuda ikusangalala chifukwa cha maweruzo anu Yehova.
9 Porque tú, eres el más grande de todos, que gobierna sobre toda la tierra; tu posición está muy por encima de cualquier otro dios.
Pakuti Inu Yehova ndi Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi; ndinu wokwezeka kupambana milungu yonse.
10 Tú, que amas al Señor, ¡Odia el mal! Porque él protege las vidas de todos los que le son leales, y los salva del poder de la gente mala.
Iwo amene amakonda Yehova adane ndi zoyipa pakuti Iye amayangʼanira miyoyo ya amene amamukhulupirira ndipo amawapulumutsa mʼdzanja la anthu oyipa
11 La luz brilla sobre aquellos que hicieron el bien, llevando alegría a aquellos que vivieron con rectitud.
Kuwala kumafika pa anthu olungama, ndi chimwemwe kwa olungama mtima.
12 ¡Alégrate en el Señor, tú, que haces el bien, y agradécele por su naturaleza santa!
Kondwerani mwa Yehova Inu olungama ndipo tamandani dzina lake loyera.

< Salmos 97 >