< Salmos 20 >
1 Para el director del coro. Un salmo de David. Que el señor te responda cuando estés en problemas; que el nombre del Dios de Jacob te proteja.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Yehova akuyankhe pamene uli pa msautso; dzina la Mulungu wa Yakobo likuteteze.
2 Que el Señor te envíe su ayuda desde el santuario, y que te sostenga desde Sión.
Iye atumize thandizo kuchokera ku malo ake opatulika; akugwirizize kuchokera ku Ziyoni.
3 Que el Señor recuerde todas tus ofrendas, y que acepte todos los holocaustos que elevaste desde tu altar. (Selah)
Iye akumbukire nsembe zako zonse ndipo alandire nsembe zako zopsereza. (Sela)
4 Que el Señor te conceda todos los deseos de tu corazón. Que haga que todos tus planes prosperen.
Akupatse chokhumba cha mtima wako ndipo akuthandize kuti zonse wakonza zichitike.
5 Que todos gritemos de alegría por tu victoria, y despleguemos estandartes en nombre de nuestro Dios. Que el Señor responda todas tus peticiones.
Ife tidzafuwula ndi chimwemwe pamene iwe wapambana ndipo tidzanyamula mbendera zathu mʼdzina la Mulungu wathu, Yehova ayankhe zopempha zako zonse.
6 Ahora sé que el Señor salvó a aquél que había ungido. Le responderá desde su santo cielo, y salvará a su ungido con su diestra poderosa.
Tsopano ndadziwa kuti Yehova amapulumutsa wodzozedwa wake; Iye amamuyankha kuchokera kumwamba ku malo ake opatulika ndi mphamvu yopulumutsa ya dzanja lake lamanja.
7 Algunos creen en carruajes y otros en caballos de guerra, pero nosotros confiamos en quien es el Señor.
Ena amadalira magaleta ndipo ena akavalo koma ife tidzadalira dzina la Yehova Mulungu wathu.
8 Ellos se desmoronan y caen, pero nosotros nos levantamos y nos ponemos en pie.
Iwo amagonjetsedwa ndi kugwa, koma ife timadzuka ndi kuyima chilili.
9 ¡Que el Señor salve al rey! ¡Por favor respóndenos cuando clamemos por ayuda!
Inu Yehova, pulumutsani mfumu! Tiyankheni pamene tikuyitanani!