< Salmos 13 >
1 Para el director del coro. Un salmo de David. ¿Por cuánto tiempo más, Señor, me vas a olvidar? ¿Para siempre? ¿Por cuánto tiempo más te vas a apartar de mí?
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Mpaka liti Yehova? Kodi mudzandiyiwala mpaka kalekale? Mpaka liti mudzandibisira nkhope yanu?
2 ¿Qué tan profundo debo caer en la confusión, sintiéndome triste todo el día? ¿Por cuánto tiempo más mi enemigo seguirá siendo victorioso sobre mí?
Ndidzalimbana ndi maganizo anga ndi kukhala ndi chisoni mu mtima mwanga tsiku lililonse mpaka liti? Mpaka liti adani anga adzandipambana?
3 Considera esto y respóndeme, Señor mi Dios. Regrésame mi fuerza porque de otro modo moriré.
Ndiyangʼaneni ndi kundiyankha, Inu Yehova Mulungu wanga. Walitsani maso anga kuti ndingafe;
4 Y mi enemigo dirá, “¡Lo derroté!” y mis oponentes celebrarán mi caída.
mdani wanga adzati, “Ndamugonjetsa,” ndipo adani anga adzakondwera pamene ine ndagwa.
5 Pero confío en tu amor inquebrantable, y sé que estaré feliz porque me salvaste.
Koma ndikudalira chikondi chanu chosasinthika; mtima wanga umakondwera ndi chipulumutso chanu.
6 ¡Cantaré al Señor, por cuanto Él me ha tratado con tanta generosidad!
Ine ndidzayimbira Yehova pakuti wandichitira zokoma.