< Salmos 120 >
1 Un cántico para los peregrinos que van a Jerusalén. Clamé al Señor en medio de todas mis tribulaciones, y Él me contestó.
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndimafuwulira kwa Yehova mʼmasautso anga, ndipo Iye amandiyankha.
2 ¡Señor, por favor sálvame de los mentirosos y de los engañadores!
Pulumutseni Yehova ku milomo yabodza, ndi kwa anthu achinyengo.
3 ¿Qué hará el Señor con ustedes, mentirosos? ¿Cómo los castigará?
Kodi adzakuchitani chiyani, ndipo adzawonjezerapo zotani, inu anthu achinyengo?
4 Con la espada afilada de un guerrero y carbones encendidos de un enebro.
Adzakulangani ndi mivi yakuthwa ya munthu wankhondo, ndi makala oyaka a mtengo wa tsanya.
5 ¡Ay de mí! Que soy extranjero en Meséc, que he acampado entre las tiendas de Cedar.
Tsoka ine kuti ndimakhala ku Mesaki, kuti ndimakhala pakati pa matenti a ku Kedara!
6 He vivido por mucho tiempo entre los pueblos que odian la paz.
Kwa nthawi yayitali ndakhala pakati pa iwo amene amadana ndi mtendere.
7 Quiero paz, pero cuando hablo de paz, ellos quieren guerra.
Ine ndine munthu wamtendere; koma ndikamayankhula, iwo amafuna nkhondo.