< Salmos 116 >
1 Yo amo al Señor porque Él me escucha, escucha mi clamor pidiendo ayuda.
Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga; Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.
2 Lo invocaré mientras viva porque Él atiende lo que digo.
Pakuti ananditchera khutu, ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.
3 Estuve atrapado por las trampas de la muerte; Estuve cautivo por los terrores de la tumba. Todo lo que experimenté fue dolor y sufrimiento. (Sheol )
Zingwe za imfa zinandizinga, zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera; ndinapeza mavuto ndi chisoni. (Sheol )
4 Entonces clamé al Señor, “¡Dios, por favor, sálvame!”
Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova: “Inu Yehova, pulumutseni!”
5 ¡El Señor es justo y bueno! ¡Nuestro Dios es un Dios compasivo!
Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.
6 El Señor cuida de los indefensos; cuando fui derribado Él me salvó.
Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima; pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.
7 Puedo estar en paz otra vez porque el Señor ha sido bueno conmigo.
Pumula iwe moyo wanga, pakuti Yehova wakuchitira zokoma.
8 Porque me has salvado de la muerte, has detenido mi llanto, y me has salvado de caer.
Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa, maso anga ku misozi, mapazi anga kuti angapunthwe,
9 Ahora puedo caminar con el Señor en la tierra de los vivos.
kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
10 Confié en ti, y clamé a ti diciendo, “¡Estoy sufriendo terriblemente!”
Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati, “Ndasautsidwa kwambiri.”
11 Estaba tan molesto que dije, “¡Todos son unos mentirosos!”
Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati, “Anthu onse ndi abodza.”
12 ¿Qué puedo darle al Señor en agradecimiento por todo lo que ha hecho por mí?
Ndingamubwezere chiyani Yehova, chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?
13 Levantaré la copa de la salvación y adoraré al Señor.
Ndidzakweza chikho cha chipulumutso ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.
14 Cumpliré mis promesas al Señor para que todos puedan ver.
Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse.
15 Le duele al Señor cuando mueren aquellos que ama.
Imfa ya anthu oyera mtima ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.
16 Señor, realmente soy tu siervo, te sirvo tal y como y mi madre lo hizo antes de mí, sin embargo, tú me has liberado.
Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu: ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; Inu mwamasula maunyolo anga.
17 Te ofreceré sacrificio en acción de gracias y te alabaré.
Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.
18 Cumpliré mis promesas en presencia de todo tu pueblo,
Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse,
19 en la casa del Señor, justo en Jerusalén. ¡Alabado sea el Señor!
mʼmabwalo a nyumba ya Yehova, mʼkati mwako iwe Yerusalemu. Tamandani Yehova.