< Salmos 105 >

1 ¡Denle gracias al Señor, alaben su maravillosa naturaleza! ¡Que todo el mundo sepa lo que Él ha hecho!
Yamikani Yehova, itanani dzina lake; lalikirani pakati pa anthu a mitundu ina zimene Iye wachita.
2 ¡Cántenle a él, canten alabanzas; cuéntenle a todos las grandes cosas que ha hecho!
Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo; fotokozani za machitidwe ake onse odabwitsa.
3 Siéntanse orgullosos de su santo nombre; alégrense, todos los que vienen al Señor!
Munyadire dzina lake loyera; mitima ya iwo amene amafunafuna Yehova ikondwere.
4 Busquen al Señor, y a su fuerza; busquen siempre estar en su presencia.
Dalirani Yehova ndi mphamvu zake; funafunani nkhope yake nthawi yonse.
5 Recuerden las maravillas que ha creado, los milagros que ha hecho, y los juicios que ha llevado a cabo,
Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita, zozizwitsa zake ndi maweruzo amene anapereka,
6 descendientes de Abraham, hijos de Israel, su pueblo escogido.
inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake, inu ana a Yakobo, osankhika ake.
7 Él es el Señor, Nuestro Dios, sus juicios cubren toda la tierra!
Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; maweruzo ake ali pa dziko lonse lapansi.
8 Él siempre recuerda su pacto, la promesa que ha hecho durará por mil generaciones;
Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya, mawu amene analamula kwa mibado yonse,
9 el pacto que hizo con Abraham, el voto que le dio a Isaac.
pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu, lumbiro limene analumbira kwa Isake.
10 El Señor lo confirmó a Jacob con un decreto, hizo este acuerdo de unión con Israel:
Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa, kwa Israeli monga pangano lamuyaya:
11 diciendo, “Te daré la tierra de Canaán”.
“Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani ngati gawo la cholowa chako.”
12 Él dijo esto cuando aún eran solo unos pocos, solo un pequeño grupo de extranjeros en la tierra.
Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero, ochepa ndithu, ndiponso alendo mʼdzikolo,
13 Vagaban de nación en nación, de un reino a otro.
ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina, kuchoka mu ufumu wina kupita ku wina.
14 Pero Él no permitió que nadie los tratara mal; advirtiendo a los reyes que los dejarán en paz:
Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza; anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo:
15 “No coloques mano sobre mi pueblo escogido, ni le hagas daño a mis profetas!”
“Musakhudze odzozedwa anga; musachitire choyipa aneneri anga.”
16 Causó una hambruna en la tierra de Canaán para que no hubiera comida.
Iye anabweretsa njala pa dziko ndipo anawononga chakudya chonse;
17 Pero, antes de eso envió a un hombre, José, quién había sido vendido como un esclavo.
Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo, Yosefe anagulitsidwa ngati kapolo.
18 Hirieron sus pies al ponerle cadenas, y pusieron un collar de hierro alrededor de su cuello,
Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza, khosi lake analiyika mʼzitsulo,
19 hasta que el tiempo predicho llegó cuando el Señor lo probó.
mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa, mpaka mawu a Yehova ataonetsa kuti Iye ananena zoona.
20 El rey envió por él y lo liberó; el rey del pueblo lo dejó en libertad.
Mfumu inatuma munthu kukamumasula, wolamulira wa mitundu ya anthu anamasula iyeyo.
21 Puso a José a cargo de la casa real, a cargo de todo lo que tenía,
Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake, wolamulira zonse zimene iye anali nazo,
22 para que le enseñara a los oficiales del rey todo lo que él quisiera, para hacer más sabios a los consejeros del rey.
kulangiza ana a mfumu monga ankafunira ndi kuphunzitsa nzeru akuluakulu.
23 Entonces Israel vino a Egipto, Jacob se estableció como extranjero en la tierra de Cam.
Tsono Israeli analowa mu Igupto; Yakobo anakhala monga mlendo mʼdziko la Hamu.
24 El Señor hizo a su pueblo más fuerte y más fértil que a sus enemigos.
Yehova anachulukitsa anthu ake; ndipo anachititsa kuti akhale ochuluka kwambiri kuposa adani awo;
25 Hizo que los egipcios cambiaran de opinión y odiarán a su gente.
amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake, kukonzera chiwembu atumiki ake.
26 Envió a su siervo Moisés, junto con Aarón, a quienes había escogido.
Yehova anatuma Mose mtumiki wake, ndi Aaroni amene Iye anamusankha.
27 Llevaron sus señales milagrosas a los egipcios, sus maravillas hasta la tierra de Cam.
Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo, zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.
28 Hundió la nación en densas tinieblas, porque ¿acaso no se habían opuesto a lo que el Señor había dicho?
Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima. Koma anthuwo anakaniratu mawu a Yehova.
29 Él convirtió su agua en sangre, matando a todos los peces.
Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi, kuchititsa kuti nsomba zawo zife.
30 Luego envió una plaga de ranas a todo el país que entraban hasta a los cuartos de los gobernadores.
Dziko lawo linadzaza ndi achule amene analowa mʼzipinda zogona za olamulira awo.
31 Dio la orden, y las moscas se esparcieron por toda la tierra; los mosquitos estaban por todas partes.
Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka ndi nsabwe mʼdziko lawo lonse.
32 Hizo llover granizo sobre ellos, y relámpagos sobre todo el país.
Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala, ndi zingʼaningʼani mʼdziko lawo lonse;
33 Destruyó sus cultivos de vino, y acabó con sus árboles.
Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu, nawononganso mitengo ina ya mʼdziko lawolo.
34 Dio la orden, y los enjambres de langostas vinieron, miles y miles de langostas:
Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera, ziwala zosawerengeka;
35 ellas se comieron toda la vegetación sobre la tierra; terminaron con todos los cultivos.
zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo, zinadya zonse zotuluka mʼnthaka yawo.
36 Dios mató a todos los primogénitos de Egipto, el primero en ser concebido en toda su fuerza y vigor.
Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo, zipatso zoyamba za umunthu wawo wonse.
37 Y entonces guió a su pueblo fuera de Egipto, llevando consigo plata y oro, y ninguna de las tribus tambaleó.
Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri, ndipo pakati pa mafuko awo palibe mmodzi amene anafowoka.
38 Los egipcios se alegraron de su partida, porque tenían miedo de los Israelitas.
Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka, pakuti kuopsa kwa Israeli kunawagwera iwo.
39 El Señor mandó una nube sobre ellos como cubierta, y en la noche, una columna de fuego para darles luz.
Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo, ndi moto owawunikira usiku.
40 Les dios codornices para comer cuando se lo pidieron; los alimentó con el pan del cielo hasta que estuvieron saciados.
Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri ndipo anawakhutitsa ndi chakudya chochokera kumwamba.
41 Abrió la roca, y el agua comenzó a fluir, un río en medio del desierto.
Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka; ngati mtsinje anayenda mʼchipululu.
42 Porque él recordó su pacto santo con su siervo Abraham.
Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene linaperekedwa kwa Abrahamu mtumiki wake.
43 Así que liberó a su pueblo, sus elegidos, mientras cantaban de alegría.
Iye anatulutsa anthu ake akukondwera, osankhika ake akufuwula mwachimwemwe;
44 Les dio las tierras de las naciones paganas, y heredaron todo aquello por cuanto los demás habían trabajado.
Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina ndipo anakhala olowamʼmalo a zimene ena anazivutikira,
45 El Señor hizo esto para que ellos lo siguieran y guardaran sus leyes. ¡Alaben al Señor!
kuti iwo asunge malangizo ake ndi kutsatira malamulo ake. Tamandani Yehova.

< Salmos 105 >