< Proverbios 7 >
1 Hijo mío, acepta lo que te digo y saca provecho de mis instrucciones.
Mwana wanga, mvera mawu anga; usunge bwino malamulo angawa.
2 Haz lo que te digo y vivirás. Observa mis enseñanzas, y estímalas como el objetivo principal de tu vida.
Utsate malamulo anga ndipo udzakhala ndi moyo; samala malangizo angawa monga uchitira ndi maso ako.
3 Átalas a tus dedos y escríbelas en tu mente.
Uchite ngati wawamangirira pa zala zako, ndiponso ngati kuti wawalemba pa mtima pako.
4 A la sabiduría, dile: “Eres mi hermana”, y considera la inteligencia como tu mejor amiga.
Nzeru uyiwuze kuti, “Iwe ndiwe mlongo wanga,” ndipo khalidwe lomvetsa bwino zinthu ulitchule kuti, “Bwenzi langa lapamtima.”
5 Ellas te protegerán de la mujer inmoral, y de la prostituta que viene a ti con palabras seductoras.
Zidzakuteteza kwa mkazi wachigololo ndiponso zidzakuthandiza kusamvera mawu oshashalika a mkazi wachilendo.
6 Una vez miré a través de la ventana de mi casa,
Tsiku lina pa zenera la nyumba yanga ndinasuzumira pa zenera.
7 y vi entre los jóvenes inmaduros a uno que era totalmente insensato.
Ndinaona pakati pa anthu opusa, pakati pa anyamata, mnyamata wina wopanda nzeru.
8 Este hombre caminaba por la calle cerca a la esquina de la casa de la prostituta, y tomó el sendero que pasaba por su casa.
Iye ankayenda njira yodutsa pafupi ndi nyumba ya mkaziyo, kuyenda molunjika nyumba ya mkaziyo.
9 Ya era la hora del crepúsculo, y la luz se desvanecía, mientras llegaba la oscuridad de la noche.
Inali nthawi yachisisira madzulo, nthawi ya usiku, kuli mdima.
10 Entonces salió esta mujer a su encuentro. Estaba vestida como una prostituta con intenciones engañosas.
Ndipo mkaziyo anadzakumana naye, atavala ngati munthu wachiwerewere wa mtima wonyenga.
11 (Era ruidosa y provocativa, sin deseo de quedarse en casa.
(Mkaziyo ndi wolongolola ndiponso nkhutukumve, iye ndi wosakhazikika pa khomo.
12 Por momentos caminaba por las calles, luego andaba por las plazas, vagabundeando en cada esquina).
Mwina umupeza pa msewu, mwina umupeza pa msika, ndipo amadikirira munthu pa mphambano iliyonse).
13 Lo agarró y lo besó, y con osadía en su rostro, le dijo:
Tsono amagwira mnyamatayo ndi kupsompsona ndi nkhope yake yopanda manyazi amamuwuza kuti,
14 “Ya presenté mi ofrenda de paz hoy, y pagué mis votos.
“Ndinayenera kupereka nsembe zachiyanjano. Lero ndakwaniritsa malumbiro anga.
15 Por eso vine a tu encuentro. ¡Te estaba buscando, y ahora te he encontrado!
Choncho ndinabwera kudzakumana nawe; ndinkakufunafuna ndipo ndakupeza!
16 Mi cama está lista, con sábanas de colores traídas desde Egipto.
Pa bedi panga ndayalapo nsalu zosalala zokongola zochokera ku Igupto.
17 En mi cama he rociado perfume, aromas de mirra, aloe y canela.
Pa bedi panga ndawazapo zonunkhira za mure, mafuta onunkhira a aloe ndi sinamoni.
18 Ven conmigo, y hagamos el amor hasta el amanecer. ¡Disfrutemos el uno del otro haciendo el amor!
Bwera, tiye tikhale malo amodzi kukondwerera chikondi mpaka mmawa; tiye tisangalatsane mwachikondi!
19 Mi esposo no está en casa, pues se ha ido a un largo viaje.
Mwamuna wanga kulibe ku nyumbako; wapita ulendo wautali:
20 Se llevó una bolsa de dinero, y no volverá hasta la luna nueva”.
Anatenga thumba la ndalama ndipo adzabwera ku nyumba mwezi ukakhwima.”
21 Así lo convenció con sus palabras, y lo sedujo con su hablar.
Ndi mawu ake onyengerera amamukakamiza mnyamatayo; amukopa ndi mawu ake oshashalika.
22 Él la siguió de inmediato, como buey llevado al matadero. Como ciervo atrapado en una trampa
Nthawi yomweyo chitsiru chimamutsatira mkaziyo ngati ngʼombe yopita kukaphedwa, monga momwe mbawala ikodwera mu msampha,
23 hasta que una lanza traspasa su hígado, como un ave que vuela y queda atrapada, y no sabe que pagará con su vida.
mpaka muvi utalasa chiwindi chake, chimakhala ngati mbalame yothamangira mʼkhwekhwe, osadziwa kuti moyo wake uwonongeka.
24 Así que escúchame ahora, hijo mío, y presta atención a lo que digo.
Tsono ana inu, ndimvereni; mvetsetsani zimene ndikunena.
25 No pienses ni siquiera en seguir a tal mujer. No camines por su casa.
Musatengeke mtima ndi njira za mkazi ameneyu; musasochere potsata njira zake.
26 Porque ella ha hecho caer a muchos hombres, y los ha destruido.
Paja iye anagwetsa anthu ambiri; wapha gulu lalikulu la anthu.
27 Su casa conduce a la muerte, y en su planta baja se encuentran las moradas de la muerte. (Sheol )
Nyumba yake ndi njira yopita ku manda, yotsikira ku malo a anthu akufa. (Sheol )