< Proverbios 4 >

1 Escuchen, hijos, la instrucción de un padre. Estén atentos al sano juicio,
Ananu, mverani malangizo a abambo anu; tcherani khutu kuti mupeze nzeru zodziwira zinthu.
2 porque lo que les diré es consejo fiel. No rechacen mis enseñanzas.
Zimene ndikukuphunzitsani ndi zabwino. Choncho musasiye malangizo anga.
3 Porque yo también fui hijo de mi padre, un joven tierno, e hijo único de mi madre
Paja ndinalinso mwana mʼnyumba mwa abambo anga; mwana mmodzi yekha wapamtima pa amayi anga.
4 y él fue quien me instruyó. Me dijo: “Presta atención a las palabras que te digo y no las olvides. Haz lo que te digo y vivirás.
Ndipo abambo anandiphunzitsa ndi mawu akuti, “Ugwiritse mawu anga pa mtima pako, usunge malamulo anga kuti ukhale ndi moyo.
5 Obtén sabiduría, busca el sano juicio. No olvides mis palabras, ni las desprecies.
Upeze nzeru, upeze nzeru zomvetsa zinthu; usayiwale mawu anga kapena kutayana nawo.
6 “No abandones la sabiduría porque ella te mantendrá a salvo. Ama la sabiduría y ella te protegerá.
Usasiye nzeru ndipo idzakusunga. Uziyikonda ndipo idzakuteteza.
7 Lo primero que debes hacer para ser sabio es obtener sabiduría. Junto a todo lo que obtengas, procura obtener inteligencia.
Fundo yayikulu pa za nzeru ndi iyi: upeze nzeru. Kaya pali china chilichonse chimene ungapeze, koma upeze nzeru yomvetsa bwino zinthu.
8 Atesora la sabiduría y ella te alabará. Abrázala y ella te honrará.
Uyilemekeze nzeruyo ndipo idzakukweza; ikumbatire nzeruyo ndipo idzakupatsa ulemu.
9 Colocará sobre tu cabeza una corona de gracia, y te ofrecerá una corona de gloria”.
Idzayika sangamutu yokongola yamaluwa pamutu pako; idzakupatsa chipewa chaufumu chaulemu.”
10 Escucha, hijo mío. Si aceptas lo que te digo, vivirás larga vida.
Mwana wanga, umvere ndi kuvomereza zimene ndikunena, ndipo zaka za moyo wako zidzakhala zochuluka.
11 Te he explicado el camino de la sabiduría. Te he guiado por los caminos de rectitud.
Ndakuphunzitsa njira yake ya nzeru. Ndakutsogolera mʼnjira zolungama.
12 No habrá obstáculos cuando camines, ni tropezarás al correr.
Pamene ukuyenda, mapazi ako sadzawombana; ukamadzathamanga, sudzapunthwa.
13 Aférrate a estas instrucciones, y no las dejes ir. Protégelas, porque son el cimiento de la vida.
Ugwiritse zimene ndikukuphunzitsazi osazitaya ayi. Uwasamale bwino pakuti moyo wako wagona pamenepa.
14 No andes por el camino de los malvados, ni sigas el ejemplo de los que hacen el mal.
Usayende mʼnjira za anthu oyipa kapena kuyenda mʼnjira ya anthu ochimwa.
15 Evítalos por completo y no vayas por allí. Da la vuelta y sigue tu camino.
Pewa njira zawo, usayende mʼmenemo; uzilambalala nʼkumangopita.
16 Los malvados no descansan hasta haber cometido maldad. No pueden dormir sin haber engañado a alguna persona.
Pakuti iwo sagona mpaka atachita zoyipa; tulo salipeza mpaka atapunthwitsa munthu wina.
17 Porque comen del pan de la maldad y beben del vino de la violencia.
Paja chakudya chawo ndicho kuchita zoyipa basi ndipo chakumwa chawo ndi chiwawa.
18 La vida de los que hacen el bien es como la luz de la aurora, que va en aumento hasta que su luz llega a plenitud del día.
Koma njira ya anthu olungama ili ngati kuwala kwa mʼbandakucha kumene kumanka kuwalirawalira mpaka dzuwa litafika pa mutu.
19 Pero la vida de los malvados es como la total oscuridad, en la que no pueden ver con qué tropiezan.
Koma njira ya anthu oyipa ili ngati mdima wandiweyani; iwo sadziwa chomwe chimawapunthwitsa.
20 Hijo mío, presta atención a lo que te digo y escucha mis palabras.
Mwana wanga, mvetsetsa zimene ndikunena; tchera khutu ku mawu anga.
21 No las pierdas de vista y reflexiona sobre ellas,
Usayiwale malangizo angawa, koma uwasunge mu mtima mwako.
22 porque son vida para quien las encuentra, y traen sanidad a todo el cuerpo.
Pakuti amapatsa moyo kwa aliyense amene awapeza ndipo amachiritsa thupi lake lonse.
23 Por encima de todas las cosas, protege tu mente, pues todo en la vida procede de ella.
Ndipotu mtima wako uziwuyangʼanira bwino ndithu pakuti ndiwo magwero a moyo.
24 Nunca mientas, ni hables con deshonestidad.
Usiyiretu kuyankhula zokhotakhota; ndipo ulekeretu kuyankhula zinthu zonyansa.
25 Enfócate en lo que está delante de ti, mira lo que tienes adelante.
Maso ako ayangʼane patsogolo; uziyangʼana kutsogolo molunjika.
26 Pon tu atención en el camino que te has propuesto, y estarás seguro donde vayas.
Uzilingalira bwino kumene kupita mapazi ako ndipo njira zako zonse zidzakhala zosakayikitsa.
27 No te apartes ni a la derecha, ni a la izquierda, y aléjate del mal.
Usapatukire kumanja kapena kumanzere; usapite kumene kuli zoyipa.

< Proverbios 4 >