< Proverbios 3 >
1 Hijo mío, no olvides mis instrucciones. Recuerda siempre mis mandamientos.
Mwana wanga, usayiwale malangizo anga, mtima wako usunge malamulo anga.
2 Así vivirás muchos años, y tu vida será plena.
Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka ndipo udzakhala pa mtendere.
3 Aférrate a la bondad y a la verdad. Átalas a tu cuello y escríbelas en tu mente.
Makhalidwe ochitira ena chifundo ndi owonetsa kukhulupirika asakuchokere. Uwamangirire mʼkhosi mwako ngati mkanda ndi kuwalemba pa mtima pako.
4 Así tendrás buena reputación y serás apreciado por Dios y la gente.
Ukatero udzapeza kuyanja ndi mbiri yabwino pamaso pa Mulungu ndi anthu.
5 Pon tu confianza totalmente en el Señor, y no te fíes de lo que crees saber.
Uzikhulupirira Yehova ndi mtima wako wonse ndipo usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.
6 Recuérdalo en todo lo que hagas, y él te mostrará el camino correcto.
Pa zochita zako zonse uvomereze kuti Mulungu alipo, ndipo Iye adzawongola njira zako.
7 No te creas sabio, respeta a Dios y evita el mal.
Usamadzione ngati wa nzeru. Uziopa Yehova ndi kupewa zoyipa.
8 Entonces serás sanado y fortalecido.
Ukatero thupi lako lidzakhala la moyo wabwino ndi mafupa ako adzakhala olimba.
9 Honra al Señor con tu riqueza y con los primeros frutos de tus cosechas.
Uzilemekeza Yehova ndi chuma chako chonse; zokolola zonse zoyamba kucha uzilemekeza nazonso Yehova.
10 Entonces tus graneros serán llenos de fruto, y tus estanques rebosarán de vino nuevo.
Ukatero nkhokwe zako zidzadzaza ndi zinthu zambiri, ndiponso mitsuko yako idzadzaza ndi vinyo.
11 Hijo mío, no rechaces la disciplina del Señor ni te enojes cuando te corrija,
Mwana wanga usanyoze malangizo a Yehova, ndipo usayipidwe ndi chidzudzulo chake.
12 porque el Señor corrige a los que ama, así como un padre corrige al hijo que más le agrada.
Paja Yehova amadzudzula amene amamukonda, monga abambo achitira mwana amene amakondwera naye.
13 Felices son los que encuentran la sabiduría y obtienen entendimiento,
Wodala munthu amene wapeza nzeru, munthu amene walandira nzeru zomvetsa zinthu,
14 porque la sabiduría vale más que la plata, y ofrece mejor recompensa que el oro.
pakuti phindu la nzeru ndi labwino kuposa la siliva, phindu lakelo ndi labwino kuposanso golide.
15 ¡La sabiduría vale más que muchos rubíes y no se compara con ninguna cosa que puedas imaginar!
Nzeru ndi yoposa miyala yamtengowapatali; ndipo zonse zimene umazikhumba sizingafanane ndi nzeru.
16 Por un lado ella te brinda larga vida, y por el otro riquezas y honra.
Mʼdzanja lake lamanja muli moyo wautali; mʼdzanja lake lamanzere muli chuma ndi ulemu.
17 Te dará verdadera felicidad, y te guiará a una prosperidad llena de paz.
Njira zake ndi njira zosangalatsa, ndipo mu njira zake zonse muli mtendere.
18 La sabiduría es un árbol de vida para todo el que se aferra a ella, y bendice a todos los que la aceptan.
Nzeru ili ngati mtengo wopatsa moyo kwa oyigwiritsitsa; wodala munthu amene amayigwiritsa kwambiri.
19 Fue gracias a la sabiduría el Señor creó la tierra, y gracias al conocimiento puso los cielos en su lugar.
Yehova anakhazikitsa dziko lapansi pogwiritsa ntchito nzeru. Anagwiritsanso ntchito nzeru zakudziwa bwino zinthu pamene ankakhazikitsa zakumwamba.
20 Fue gracias a su conocimiento que las aguas de las profundidades fueron liberadas, y las nubes enviadas como rocío.
Mwa nzeru zake Yehova anatumphutsa madzi kuchokera mʼnthaka ndiponso mitambo inagwetsa mvula.
21 Hijo mío, aférrate al buen juicio y a las decisiones sabias; no los pierdas de vista,
Mwana wanga usunge nzeru yeniyeni ndi khalidwe lomalingarira zinthu bwino. Zimenezi zisakuchokere.
22 porque serán vida para ti, y como un adorno en tu cuello.
Zimenezi zidzakupatsa moyo, moyo wake wosangalatsa ndi wabwino ngati mkanda wa mʼkhosi.
23 Caminarás con confianza y no tropezarás.
Choncho udzayenda pa njira yako mosaopa kanthu, ndipo phazi lako silidzapunthwa;
24 Cuando descanses, no tendrás temor, y cuando te acuestes tu sueño será placentero.
pamene ugona pansi, sudzachita mantha; ukadzagona pansi tulo tako tidzakhala tokoma.
25 No tendrás temor del pánico repentino, ni de los desastres que azotan al malvado,
Usaope tsoka lobwera mwadzidzidzi kapena chiwonongeko chimene chidzagwera anthu oyipa,
26 porque el Señor será tu confianza, y evitará que caigas en trampa alguna.
pakuti Yehova adzakulimbitsa mtima ndipo adzasunga phazi lako kuti lisakodwe mu msampha.
27 No le niegues el bien a quien lo merece cuando tengas el poder en tus manos.
Usaleke kuchitira zabwino amene ayenera kulandira zabwino, pamene uli nazo mphamvu zochitira zimenezi.
28 No le digas a tu prójimo: “Vete. Ven mañana, y yo te daré”, si ya tienes los recursos para darle.
Usanene kwa mnansi wako kuti, “Pita, uchite kubweranso. Ndidzakupatsa mawa” pamene uli nazo tsopano.
29 No hagas planes para perjudicar a tu prójimo que vive junto a ti, y que confía en ti.
Usamukonzere chiwembu mnansi wako, amene anakhala nawe pafupi mokudalira.
30 No discutas con nadie sin razón, si no han hecho nada para hacerte daño alguno.
Usakangane ndi munthu wopanda chifukwa pamene iye sanakuchitire zoyipa.
31 ¡No sientas celos de los violentos, ni sigas su ejemplo!
Usachite naye nsanje munthu wachiwawa kapena kutsanzira khalidwe lake lililonse.
32 Porque el Señor aborrece a los mentirosos, pero es amigo de los que hacen lo que es bueno.
Pakuti Yehova amanyansidwa ndi munthu woyipa koma amayanjana nawo anthu olungama.
33 Las casas de los malvados están malditas por el Señor, pero él bendice los hogares de los que viven en rectitud.
Yehova amatemberera nyumba ya munthu woyipa, koma amadalitsa nyumba ya anthu olungama.
34 Él se burla de los que se burlan, pero es bondadoso con los humildes.
Anthu onyoza, Iye amawanyoza, koma amakomera mtima anthu odzichepetsa.
35 Los sabios recibirán honra, pero los necios permanecerán en desgracia.
Anthu anzeru adzalandira ulemu, koma zitsiru adzazichititsa manyazi.