< Proverbios 23 >

1 Cuando te sientes a comer con un gobernante, ten cuidado con lo que te sirven,
Ngati ukhala pansi kuti udye pamodzi ndi wolamulira, uyangʼane bwino zimene zili pamaso pako,
2 y ponte límites si tienes mucha hambre.
ngati ndiwe munthu wadyera udziletse kuti usaonetse dyera lakolo.
3 No seas glotón en sus finos banquetes, porque lo ofrecen con motivaciones engañosas.
Usasirire zakudya zake, pakuti zimenezo ndi zakudya zachinyengo.
4 No te desgastes tratando de volverte rico. ¡Sé sabio y no te afanes en ello!
Usadzitopetse wekha ndi kufuna chuma, ukhale ndi nzeru ya kudziretsa.
5 La riqueza desaparece en un abrir y cerrar de ojos, abriendo repentinamente alas, y volando al cielo como el águila.
Ukangoti wachipeza chumacho uwona posachedwa kuti palibepo. Chumacho chimachita ngati chamera mapiko mwadzidzidzi ndi kuwuluka kunka kumwamba ngati chiwombankhanga.
6 No aceptes ir a comer con personas mezquinas, ni codicies sus finos banquetes,
Usadye chakudya cha munthu waumbombo, usalakalake zakudya zake zokoma;
7 porque tal como son sus pensamientos, así son ellos. Ellos dicen: “¡Ven, come y bebe!” Pero en sus mentes no tienen ningún interés en ti.
paja iye ndi munthu amene nthawi zonse amaganizira za mtengo wake ngakhale amati kwa iwe, “Idya ndi kumwa,” koma sakondweretsedwa nawe.
8 Vomitarás cada pedazo que hayas comido, y las palabras de aprecio se habrán consumido.
Udzasanza zimene wadyazo ndipo mawu ako woyamikira adzapita pachabe.
9 No hables con los tontos porque ellos se burlarán de tus palabras sabias.
Usayankhule munthu wopusa akumva, pakuti adzanyoza mawu ako anzeru.
10 No muevas las fronteras antiguas, y no invadas los campos que pertenecen a huérfanos,
Usasunthe mwala wa mʼmalire akalekale kapena kulowerera mʼminda ya ana amasiye,
11 porque su Protector es poderoso y él peleará su caso contra ti.
paja Mpulumutsi wawo ndi wamphamvu; iye adzawateteza pa milandu yawo kutsutsana nawe.
12 Enfoca tu mente en la instrucción; escucha las palabras de conocimiento.
Mtima wako uzikhala pa malangizo ndipo makutu ako azimvetsera mawu a chidziwitso.
13 No evites disciplinar a tus hijos, pues un golpe no los matará.
Usaleke kumulangiza mwana; ngati umulanga ndi chikwapu sadzafa.
14 Si corriges con castigo físico a tu hijo, lo salvarás de la muerte. (Sheol h7585)
Ukamukwapula ndi tsatsa udzapulumutsa moyo wake. (Sheol h7585)
15 Hijo mío, si piensas con sabiduría me harás feliz;
Mwana wanga, ngati mtima wako ukhala wanzeru, inenso mtima wanga udzakondwera.
16 Me deleitaré cuando hables con rectitud.
Mtima wanga udzakondwera pamene ndidzakumva ukuyankhula zolungama.
17 No mires a los pecadores con envidia, sino recuerda siempre honrar al Señor,
Mtima wako usachite nsanje ndi anthu ochimwa, koma uziopa Yehova tsiku ndi tsiku.
18 porque ciertamente hay un futuro para ti, y tu esperanza no será destruida.
Ndithu za mʼtsogolo zilipo ndipo chiyembekezo chakocho sichidzalephereka.
19 Presta atención, hijo mío, y sé sabio. Asegúrate de enfocar tu mente en seguir el camino recto.
Tamvera mwana wanga, ndipo ukhale wanzeru, mtima wako uwuyendetse mʼnjira yabwino.
20 No te juntes con los que beben mucho vino, o con los que se sacian de carne.
Usakhale pakati pa anthu amene amaledzera kapena pakati pa anthu amene amadya nyama mwadyera.
21 Porque los que se emborrachan y comen de más, pierden todo lo que tienen; y pasan el tiempo adormilados, por lo cual solo les quedan trapos para vestir.
Paja anthu oledzera ndi adyera amadzakhala amphawi ndipo aulesi adzavala sanza.
22 Presta atención a tu padre, y no rechaces a tu madre cuando sea vieja.
Mvera abambo ako amene anakubala, usanyoze amayi ako pamene akalamba.
23 Invierte en tener la verdad y no la vendas. Invierte en la sabiduría, la instrucción y la inteligencia.
Gula choonadi ndipo usachigulitse; ugulenso nzeru, mwambo ndiponso kumvetsa zinthu bwino.
24 Los hijos que hacen el bien alegran a sus padres; un hijo sabio trae alegría a su padre.
Abambo a munthu wolungama ali ndi chimwemwe chachikulu; Wobala mwana wanzeru adzakondwera naye.
25 Haz que tu padre y tu madre se alegren; trae alegría a la que te parió.
Abambo ndi amayi ako asangalale; amene anakubereka akondwere!
26 Hijo mío, dame toda tu atención, y sigue mi ejemplo con alegría.
Mwana wanga, undikhulupirire ndipo maso ako apenyetsetse njira zanga.
27 Una prostituta es como quedar atrapado en un foso. La mujer inmoral es como quedar atrapado en un pozo estrecho.
Paja mkazi wachiwerewere ali ngati dzenje lozama; ndipo mkazi woyendayenda ali ngati chitsime chopapatiza.
28 Tal como un ladrón, ella se recuesta para esperar y agarrar a los hombres por sorpresa, para que sean infieles a sus mujeres.
Amabisala ngati mbala yachifwamba, ndipo amuna amakhala osakhulupirika chifukwa cha iyeyu.
29 ¿Quién estará en problemas? ¿Quién sufrirá dolor? ¿Quién estará en discusión? ¿Quién se quejará? ¿Quién saldrá lastimado sin razón alguna? ¿Quién tendrá los ojos enrojecidos?
Ndani ali ndi tsoka? Ndani ali ndi chisoni? Ndani ali pa mkangano? Ndani ali ndi madandawulo? Ndani ali ndi zipsera zosadziwika uko zachokera? Ndani ali ndi maso ofiira?
30 Los que pasan mucho tiempo bebiendo vino, los que siempre están probando un nuevo cóctel.
Ndi amene amakhalitsa pa mowa, amene amapita nalawa vinyo osakanizidwa.
31 No dejes que la apariencia del vino te tiente, ya sea por su color rojo o por sus burbujas en la copa, o por la suavidad con que se asienta.
Usatengeke mtima ndi kufiira kwa vinyo, pamene akuwira mʼchikho pamene akumweka bwino!
32 Al final morderá como una serpiente, y te causará dolor como víbora.
Potsiriza pake amaluma ngati njoka, ndipo amajompha ngati mphiri.
33 Alucinarás, verás cosas extrañas, y tu mente confundida te hará decir toda clase de locuras.
Maso ako adzaona zinthu zachilendo ndipo maganizo ndi mawu ako adzakhala osokonekera.
34 Te tropezarás como si rodaras por el océano. Serás sacudido como quien se recuesta en el mástil de una embarcación, diciendo:
Udzakhala ngati munthu amene ali gone pakati pa nyanja, kapena ngati munthu wogona pa msonga ya mlongoti ya ngalawa.
35 “La gente me golpeó, pero no me dolió; me dieron azotes, pero no sentí nada. Ahora debo levantarme porque necesito otro trago”.
Iwe udzanena kuti, “Anandimenya, koma sindinapwetekedwe! Andimenya koma sindinamve kanthu! Kodi ndidzuka nthawi yanji? Ndiye ndifunefunenso vinyo wina.”

< Proverbios 23 >