< Proverbios 2 >

1 Hijo mío, si aceptas mi palabra y valoras mis instrucciones;
Mwana wanga, ngati ulandira mawu anga ndi kusunga malamulo anga mu mtima mwako,
2 si prestas atención a la sabiduría y procuras entender;
ndiponso kutchera khutu lako ku nzeru ndi kuyikapo mtima pa kumvetsa zinthu;
3 si clamas pidiendo inteligencia y gritas pidiendo ayuda para comprender;
ngati upempha kuti uzindikire zinthu inde kupempha ndi mtima wonse kuti ukhale womvetsa zinthu,
4 si la buscas como si fuera plata, y la persigues como si fuera un tesoro oculto,
ngati ufunafuna nzeruyo ngati siliva ndi kuyisakasaka ngati chuma chobisika,
5 entonces entenderás cómo debes relacionarte con el Señor y conocerás verdaderamente a Dios.
ndiye udzamvetsa bwino tanthauzo la kuopa Yehova; ndipo udzapezanso tanthauzo la kumudziwa Yehova.
6 El Señor es la fuente de la sabiduría. Su palabra proporciona el conocimiento y la razón.
Pakuti Yehova ndiye amapereka nzeru, ndipo mʼkamwa mwake mumachokera chidziwitso ndi kumvetsa zinthu.
7 Él da sano juicio a los que viven en rectitud, y defiende a los que tienen buen discernimiento.
Anthu olungama zinthu zimawayendera bwino chifukwa Yehova amakhala nawo. Paja Yehova ndiye chishango cha amene amayenda mwangwiro,
8 Él sostiene a los que actúan con justicia y protege a los que confían en él.
pakuti ndiye mlonda wa njira zolungama. Iye amasamala mayendedwe a anthu ake okhulupirika.
9 Entonces podrás reconocer lo que es recto y justo, y todo lo bueno, así como la forma en que debes vivir.
Choncho udzamvetsa tanthauzo la ungwiro, chilungamo, kusakondera ndi njira iliyonse yabwino.
10 Porque la sabiduría inundará tu mente, y el conocimiento te hará feliz.
Pakuti nzeru idzalowa mu mtima mwako, kudziwa zinthu kudzakusangalatsa.
11 Las buenas decisiones te mantendrán por el buen camino, y estarás a salvo si piensas usando la razón.
Kuganizira bwino za mʼtsogolo kudzakusunga; kumvetsa zinthu bwino kudzakuteteza.
12 Esto te guardará de los caminos del mal, de los hombres mentirosos
Nzeru idzakupulumutsa ku mayendedwe oyipa, kwa anthu amabodza,
13 que se alejan del camino recto para andar en caminos de oscuridad.
amene amasiya njira zolungama namayenda mʼnjira zamdima,
14 Ellos son felices haciendo el mal, y les gusta la perversión.
amene amakondwera pochita zoyipa namasangalala ndi kuyipa kwa ntchito zawo zonyansa.
15 Viven vidas extraviadas, cometiendo actos engañosos.
Amenewa ndi anthu a njira zawo zokhotakhota, ndipo makhalidwe awo ndi achinyengo.
16 También te guardará de la mujer que actúa con inmoralidad, de mujeres que tal como una prostituta tratan de seducirte con elogios.
Nzeruyo idzakupulumutsanso kwa mkazi wachigololo; kwa mkazi wachilendo woyankhula moshashalika,
17 Una mujer que ha abandonado al hombre con el que se casó en su juventud, y ha olvidado las promesas que hizo ante Dios.
amene wasiya mwamuna wa chitsikana wake ndi kuyiwala pangano limene anachita pamaso pa Mulungu wake.
18 Lo que sucede en su casa conduce a la muerte, y seguir sus caminos te llevará a la tumba.
Pakuti nyumba yake imatsetserekera ku imfa; njira zake zimamufikitsa ku manda.
19 Ninguno que va donde ella regresa, pues nunca más logran encontrar el camino de regreso a la vida.
Opita kwa iye palibe ndi mmodzi yemwe amabwerera kapena kupezanso njira zamoyo.
20 Así que tú sigue el camino del bien, y asegúrate de ir por los senderos de quienes hacen lo recto.
Choncho iwe uziyenda mʼnjira za anthu abwino, uzitsata njira za anthu ochita chilungamo.
21 Porque solo los rectos habitarán la tierra. Solo los honestos permanecerán en ella.
Pakuti anthu olungama ndiwo ati adzakhale mʼdziko ndipo anthu angwiro ndiwo ati adzakhazikike mʼmenemo;
22 Pero los malvados serán expulsados de ella, y los infieles serán arrancados de raíz.
Koma anthu oyipa adzachotsedwa mʼdzikomo, ndipo anthu onyenga adzachotsedwamo.

< Proverbios 2 >