< Números 33 >

1 Este es un registro de los viajes realizados por los israelitas al salir de Egipto en sus divisiones tribales lideradas por Moisés y Aarón.
Malo otsatirawa ndi omwe Aisraeli anayima pa maulendo awo atatuluka mʼdziko la Igupto mʼmagulu awo motsogozedwa ndi Mose ndi Aaroni.
2 Moisés registró las diferentes partes de su viaje según las instrucciones del Señor. Estos son los viajes que hicieron listados en orden desde donde comenzaron:
Mose analemba malo amene anayambira maulendo awo molamulidwa ndi Yehova. Maulendo awo ndi malo omwe anayambira ndi awa:
3 Los israelitas dejaron Ramsés el día quince del primer mes, el día después de la Pascua. Salieron triunfantes mientras todos los egipcios observaban.
Aisraeli ananyamuka kuchokera ku Ramesesi pa tsiku la 15 la mwezi woyamba, itangotha Paska. Iwo anatuluka nayenda molimba mtima Aigupto onse akuona,
4 Los egipcios enterraban a todos sus primogénitos que el Señor había matado, porque el Señor había hecho caer sus juicios sobre sus dioses.
pamene ankayika maliro a ana awo oyamba kubadwa, omwe Yehova anawakantha pakati pawo chifukwa Yehova anaweruza milungu yawo.
5 Los israelitas dejaron Ramsés e instalaron un campamento en Sucot.
Aisraeli atachoka ku Ramesesi, anamanga misasa yawo ku Sukoti.
6 Se fueron de Sucot y acamparon en Etam, en la frontera con el desierto.
Atachoka ku Sukoti anakamanga misasa yawo ku Etamu, mʼmbali mwa chipululu.
7 Se alejaron de Etam, volviendo a Pi-hahiroth, frente a Baal-zefón, y acamparon cerca de Migdol.
Ndipo atachoka ku Etamu, anabwerera ku Pihahiroti, kummawa kwa Baala-Zefoni, ndipo anamanga misasa yawo pafupi ndi Migidoli.
8 Se mudaron de Pi-hahirot y cruzó por el medio del mar hacia el desierto. Viajaron durante tres días al desierto de Etham y establecieron un campamento en Marah.
Atachoka ku Pihahiroti anadutsa mʼkati mwa nyanja kupita ku chipululu ndipo atayenda masiku atatu mʼchipululu cha Etamu, anamanga misasa yawo ku Mara.
9 Se desplazaron desde Mara y llegaron a Elim, donde había doce manantiales de agua y setenta palmeras, y acamparon allí.
Atachoka ku Mara anafika ku Elimu, kumene kunali akasupe a madzi khumi ndi awiri ndi mitengo ya migwalangwa 70 ndipo anamanga misasa yawo kumeneko.
10 Se trasladaron de Elim y acamparon al lado del Mar Rojo.
Atachoka ku Elimu anakamanga misasa yawo mʼmbali mwa Nyanja Yofiira.
11 Se trasladaron desde el Mar Rojo y acamparon en el Desierto del Pecado.
Atachoka ku Nyanja Yofiira anakamanga misasa yawo mʼchipululu cha Sini.
12 Se trasladaron del desierto de Sin y acamparon en Dofca.
Atachoka ku chipululu cha Sini anakamanga ku Dofika.
13 Se mudaron de Dofca y acamparon en Alús.
Atachoka ku Dofika anakamanga misasa yawo ku Alusi.
14 Se mudaron de Alús y acamparon en Refidím. No había agua allí para que la gente bebiera.
Atachoka ku Alusi anakamanga misasa yawo ku Refidimu, kumene kunalibe madzi woti anthu ndi kumwa.
15 Se fueron de Refidim y acamparon en el desierto del Sinaí.
Atachoka ku Refidimu anakamanga ku chipululu cha Sinai
16 Se fueron del desierto del Sinaí y acamparon en Kibroth-hataava.
Atachoka ku chipululu cha Sinai anakamanga misasa yawo ku Kiburoti-Hataava.
17 Se mudaron de Kibroth-hattaavah y acamparon en Hazerot.
Atachoka ku Kiburoti-Hataava anakamanga misasa yawo ku Heziroti.
18 Se trasladaron de Hazerot y establecieron un campamento en Ritma.
Atachoka ku Heziroti anakamanga ku Ritima.
19 Se trasladaron de Ritma y establecieron un campamento en Rimón-fares.
Atachoka ku Ritima anakamanga ku Rimoni-Perezi.
20 Se trasladaron de Rimmon-fares y acamparon en Libna.
Atachoka ku Rimoni-Perezi anakamanga ku Libina.
21 Se trasladaron de Libna y establecieron un campamento en Rissa.
Atachoka ku Libina anakamanga ku Risa.
22 Se trasladaron de Rissa y establecieron un campamento en Ceelata.
Atachoka ku Risa anakamanga ku Kehelata.
23 Se trasladaron de Ceelata y acamparon en el Monte Sefer.
Atachoka ku Kehelata anakamanga ku phiri la Seferi.
24 Se trasladaron del Monte Sefer y acamparon en Harada.
Atachoka ku phiri la Seferi anakamanga ku Harada.
25 Se trasladaron de Harada y acamparon en Macelot.
Atachoka ku Harada anakamanga ku Mekheloti.
26 Se trasladaron de Macelot y acamparon en Tahat.
Atachoka ku Mekheloti anakamanga ku Tahati.
27 Se fueron de Tahat y acamparon en Tara.
Atachoka ku Tahati anakamanga ku Tera.
28 Se mudaron de Tara y acamparon en Mitca.
Atachoka ku Tera anakamanga ku Mitika.
29 Se mudaron de Mitca y acamparon en Hasmona.
Atachoka ku Mitika anakamanga ku Hasimona.
30 Se fueron de Hasmona y acamparon en Moserot.
Atachoka ku Hasimona anakamanga ku Moseroti.
31 Se mudaron de Moserot y acamparon en Bene-jaacán.
Atachoka ku Moseroti anakamanga ku Beni Yaakani.
32 Se mudaron de Bene-jaacán y acamparon en Hor-haggidgad.
Atachoka ku Beni Yaakani anakamanga ku Hori-Hagidigadi.
33 Se trasladaron de Hor-haggidgad y acamparon en Jotbata.
Atachoka ku Hori-Hagidigadi anakamanga ku Yotibata.
34 Se mudaron de Jotbata y establecieron un campamento en Abrona.
Atachoka ku Yotibata anakamanga ku Abirona.
35 Se mudaron de Abrona y acamparon en Ezión-geber.
Atachoka ku Abirona anakamanga ku Ezioni-Geberi.
36 Se trasladaron de Ezion-geber y acamparon en Cades, en el desierto de Zin.
Atachoka ku Ezioni-Geberi anakamanga ku Kadesi, mʼchipululu cha Zini chimene ndi Kadesi.
37 Se trasladaron de Cades y acamparon en el monte Hor, en la orilla de Edom.
Anachoka ku Kadesi ndi kukamanga ku phiri la Hori, mʼmalire mwa dziko la Edomu.
38 El sacerdote Aarón subió al monte Hor como el Señor le había ordenado, y murió allí el primer día del quinto mes, en el cuadragésimo año después de que los israelitas hubieran salido de Egipto.
Molamulidwa ndi Yehova, wansembe Aaroni anakwera ku phiri la Hori kumene anakamwalirira pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu, mʼchaka cha makumi anayi, Aisraeli atatuluka mʼdziko la Igupto.
39 Aarón tenía 123 años cuando murió en el Monte Hor.
Aaroni anamwalira pa phiri la Hori ali ndi zaka 123.
40 (El rey cananeo de Arad, que vivía en el Néguev en el país de Canaán, se enteró de que los israelitas estaban en camino).
Mfumu ya Akanaani ya ku Aradi yomwe inkakhala ku Negevi kummwera kwa Kanaani, inamva kuti Aisraeli akubwera.
41 Los israelitas se trasladaron del Monte Hor y establecieron un campamento en Zalmona.
Atachoka ku phiri la Hori anakamanga ku Zalimoni.
42 Se trasladaron de Zalmona y acamparon en Punón.
Atachoka ku Zalimoni anakamanga ku Punoni.
43 Se trasladaron de Punón y acamparon en Obot.
Atachoka ku Punoni anakamanga ku Oboti.
44 Se trasladaron de Oboth y acamparon en Iye-abarim, en la frontera de Moab.
Atachoka ku Oboti anakamanga ku Iye-Abarimu.
45 Se mudaron de Iye-abarim y acamparon en Dibon-gad.
Atachoka ku Iye-Abarimu anakamanga ku Diboni Gadi.
46 Se mudaron de Dibon-gad y acamparon en Almon-diblataim.
Atachoka ku Diboni Gadi anakamanga ku Alimoni-Dibulataimu.
47 Se mudaron de Almon-diblataim y acamparon en las montañas de Abarim, frente a Nebo.
Atachoka ku Alimoni-Dibulataimu anakamanga mʼmapiri a Abarimu, pafupi ndi Nebo.
48 Se trasladaron de las montañas de Abarim y acamparon en las llanuras de Moab, junto al Jordán, frente a Jericó.
Atachoka ku mapiri a Abarimu anakamanga ku zigwa za Mowabu mʼmbali mwa Yorodani moyangʼanana ndi Yeriko.
49 Allí, en las llanuras de Moab, acamparon al lado del Jordán, desde Beth-jesimot hasta Abel-sitim.
Ali ku zigwa za Mowabu anamanga mʼmbali mwa Yorodani kuchokera ku Beti-Yesimoti mpaka ku Abeli-Sitimu.
50 Aquí fue donde, en la llanura de Moab junto al Jordán, frente a Jericó, el Señor le dijo a Moisés,
Pa zigwa za Mowabu, mʼmbali mwa Yorodani moyangʼanana ndi ku Yeriko, Yehova anawuza Mose kuti,
51 “Dile a los israelitas: Tan pronto crucen el Jordán y entren en el país de Canaán,
“Nena kwa Aisraeli kuti, ‘Pamene muwoloka Yorodani kulowa mʼdziko la Kanaani,
52 deben expulsar a todos los que viven en la tierra, destruir todas sus imágenes talladas e ídolos de metal, y derribar todos sus templos paganos.
mukathamangitse nzika zonse za mʼdzikomo pamaso panu. Mukawononge mafano awo onse a miyala ndi osula ndi malo awo achipembedzo.
53 Debes tomar el país y establecerte allí, porque te he dado la tierra y te pertenece.
Mukalande dzikolo ndi kukhalamo chifukwa ndakupatsani dziko limenelo kuti mukhalemo.
54 Debes dividir la tierra y asignarla por sorteo a las diferentes familias tribales. Dale una porción más grande a una familia más grande, y una porción más pequeña a una familia más pequeña. La asignación de cada uno se decide por sorteo, y todos ustedes recibirán una asignación dependiendo de su tribu.
Mukagawane dzikolo pochita maere monga mwa mafuko anu. Kwa omwe ali ambiri, cholowa chambiri, ndipo amene ali ocheperapo, chocheperanso. Chilichonse chimene chidzawagwere iwo mwa maere chidzakhala chawo. Mukaligawane monga mwa mafuko a makolo anu.
55 “Pero si no expulsan a todos los que viven en la tierra, las personas que dejen permanecer serán como arena en sus ojos y espinas en sus costados. Les causarán problemas cuando se establezcan en el país.
“‘Koma ngati simukathamangitsa nzika zimene zili mʼdzikomo, amene mukawalole kukhalamo adzakhala ngati zisonga mʼmaso mwanu ndi ngati minga mʼmbali mwanu. Adzakubweretserani mavuto mʼdziko limene mudzakhalemolo.
56 Eventualmente, el castigo que planeé para ellos se los infligiré a ustedes”.
Ndipo pamenepo ndidzachitira inu zomwe ndinaganiza kuwachitira iwowo.’”

< Números 33 >