< Levítico 18 >

1 El Señor le dijo a Moisés:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 “Dile a los israelitas: Yo soy el Señor tu Dios.
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
3 No sigas los caminos de Egipto, donde vivías, y no sigas los caminos de Canaán, donde te llevaré. No adoptes sus prácticas.
Musamachite zomwe amachita anthu a ku Igupto kumene munkakhala kuja, ndiponso musamachite zomwe amachita anthu a ku Kanaani kumene ndikukupititsani. Musatsatire miyambo yawo.
4 Haz lo que te digo y guarda mis reglas. Yo soy el Señor tu Dios.
Inu muzimvera malamulo anga ndipo muzisamalitsa kutsatira malangizo anga. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
5 Si guardas mis reglas y haces lo que te digo, vivirás. Yo soy el Señor.
Choncho sungani malangizo ndi malamulo anga, popeza munthu amene amvera zimenezi adzakhala ndi moyo. Ine ndine Yehova.
6 “No tengas relaciones sexuales con un pariente cercano.
“‘Munthu aliyense asagonane ndi wachibale wake. Ine ndine Yehova.
7 No avergüences a tu padre teniendo sexo con tu madre. Ella es tu madre; no tengas sexo con ella.
“‘Usachititse manyazi abambo ako pogonana ndi amayi ako. Iwo ndi amayi ako. Usagonane nawo.
8 No tengas sexo con ninguna de las esposas de tu padre y avergüenza a tu padre.
“‘Usagonane ndi mkazi wa abambo ako (osakhala amayi okubala). Ukatero ukuchititsa manyazi abambo ako.
9 No tengas sexo con tu hermana, si es hija de tu padre o de tu madre, o si nació en la misma casa que tú o en otro lugar.
“‘Usagonane ndi mlongo wako, mwana wamkazi wa abambo ako, kapena mwana wamkazi wa amayi ako, kaya anabadwira mʼnyumba mwanu kapena kwina.
10 No tengas sexo con tu nieta, la hija de tu hijo o la hija de tu hija, porque eso sería algo vergonzoso para ti.
“‘Usagonane ndi mdzukulu wako: mwana wa mwana wako wamwamuna kapena mwana wa mwana wako wamkazi. Kutero nʼkudzichotsa ulemu.
11 No tengas sexo con la hija de ninguna de las esposas de tu padre y tu padre, ella es tu hermana.
“‘Usagonane ndi mwana wamkazi wa mkazi wa abambo ako, amene abambo akowo anabereka; popeza ameneyo ndi mlongo wako.
12 No tengas sexo con la hermana de tu padre. Ella es un pariente cercano de tu padre.
“‘Usagonane ndi mlongo wa abambo ako; popeza ameneyo ndi thupi limodzi ndi abambo ako.
13 No tengas relaciones sexuales con la hermana de tu madre. Ella es un pariente cercano de tu madre.
“‘Usagonane ndi mchemwali wa amayi ako chifukwa ameneyo ndi thupi limodzi ndi amayi ako.
14 No avergüences a tu tío teniendo sexo con su esposa. Ella es tu tía.
“‘Usachititse manyazi mchimwene wa abambo ako pogonana ndi mkazi wake popeza amenewo ndi azakhali ako.
15 No tengas sexo con tu nuera. Ella es la esposa de tu hijo. No tengas sexo con ella.
“‘Usagonane ndi mpongozi wako popeza ameneyo ndi mkazi wa mwana wako. Choncho usamuchititse manyazi.
16 No te acuestes con la esposa de tu hermano y avergüénzate de él.
“‘Usagonane ndi mkazi wa mchimwene wako popeza potero ukuchititsa manyazi mʼbale wakoyo.
17 No tengas sexo con una mujer y su hija. No tengas sexo con la hija de su hijo o la hija de su hija. Son sus parientes cercanos. Eso es algo que detesto.
“‘Usagonane ndi mkazi ndiponso mwana wake wamkazi. Usagonane ndi mwana wamkazi wa mwana wake wamwamuna, kapena mwana wamkazi wa mwana wake wamkazi. Amenewo ndi thupi limodzi ndi mkaziyo. Kutero ndikuchita chinthu choyipa kwambiri.
18 No te cases con la hermana de tu esposa y tengas sexo con ella mientras tu esposa esté viva. Serán esposas hostiles entre sí.
“‘Usakwatire mchemwali wa mkazi wako ndi kumagonana naye mkazi wakoyo ali moyo ngati wopikisana naye.
19 No tengas sexo con una mujer durante el tiempo que esté sucia debido a su período.
“‘Usamuyandikire mkazi kuti ugonane naye pa nthawi yake yosamba.
20 No cometas ningún acto sexual con la esposa de otro hombre. Esto te contaminaría y te haría sucio.
“‘Usagonane ndi mkazi wa mnzako ndi kudziyipitsa naye.
21 “No le des ninguno de tus hijos como sacrificio humano a Moloc, porque no debes deshonrar el carácter de tu Dios. Yo soy el Señor.
“‘Usapereke mwana wako aliyense kuti akhale nsembe yamoto kwa Moleki ndi kuyipitsa dzina la Yehova. Ine ndine Yehova.
22 “No tengas sexo con un hombre como con una mujer. Eso es algo asqueroso.
“‘Usagonane ndi mwamuna ngati mkazi; chimenecho ndi chinthu chonyansa.
23 No tengas sexo con ningún animal. Esto te contaminaría y te ensuciaría.
“‘Usagonane ndi nyama ndi kudziyipitsa nayo. Mkazi asadzipereke kwa nyama kuti agonane nayo. Chimenecho ndi chisokonezo.
24 Una mujer no debe entregarse a un animal para tener sexo con él. Eso es algo asqueroso. No se contaminen y se ensucien haciendo algo así. Esa es la razón por la que estoy expulsando a estas naciones de la tierra, se han contaminado a sí mismos por todas estas prácticas.
“‘Musadzidetse ndi zinthu zimenezi chifukwa umo ndi mmene mitundu ina imene ndikuyithamangitsa pamaso panu inadzidetsera.
25 Incluso la tierra se ha contaminado, así que la estoy castigando por los pecados cometidos por la gente que vive allí, y la tierra los vomitará.
Choncho dziko linayipa ndipo ndinalilanga chifukwa cha tchimo lake. Motero dzikolo linasanza anthu ake okhalamo.
26 “Peroustedes deben hacer lo que yo os diga y guardar mis reglas. No deben hacer ninguno de estos actos repugnantes, ya sea un israelita o un extranjero que viva entre ustedes.
Koma inu mukasunge malangizo ndi malamulo anga. Mbadwa ndiponso alendo amene akukhala pakati panu asakachite china chilichonse cha zinthu zonyansazi,
27 Las personas que vivían en la tierra antes de ti practicaban todas estas cosas repugnantes, y la tierra se contaminó.
pakuti zinthu zonsezi ndi zomwe ankachita anthu amene ankakhala mʼdzikomo inu musanafike, ndipo dziko linayipitsidwa.
28 Si contaminas la tierra, te vomitará como lo hizo con las naciones anteriores a ti.
Koma inu musachite zimenezi kuti dziko lingakusanzeni mutaliyipitsa monga linasanzira mitundu imene imakhalamo inu musanafike.
29 “Por consiguiente, cualquiera que haga cualquiera de estas cosas repugnantes debe ser expulsado de su pueblo.
“‘Aliyense wochita zinthu zonyansa zimenezi achotsedwe pakati pa anthu anzake.
30 Debes aceptar mi demanda de que no sigas ninguna de estas prácticas repugnantes hechas antes de tu llegada. No se contaminen ni se hagan impuros. Yo soy el Señor su Dios”.
Choncho mverani malangizo anga oletsa kuchita miyambo yonyansayi imene ankatsatira anthu amene analipo inu musanafike ndi kudziyipitsa nayo. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”

< Levítico 18 >