< Lamentaciones 3 >
1 Soy el hombre que ha experimentado el sufrimiento bajo la vara de la ira de Dios.
Ine ndine munthu amene ndaona masautso ndi ndodo ya ukali wake.
2 Me ha alejado, obligándome a caminar en las tinieblas en lugar de la luz.
Wandipititsa kutali ndipo wandiyendetsa mu mdima osati mʼkuwala;
3 De hechome golpea una y otra vez todo el día.
zoonadi anandikantha ndi dzanja lake mobwerezabwereza tsiku lonse.
4 Me ha desgastado; me ha hecho pedazos.
Wakalambitsa khungu langa ndi mnofu wanga, ndipo waphwanya mafupa anga.
5 Me ha asediado, rodeándome de amargura y miseria.
Wandizinga ndi kundizungulira ndi zowawa ndi zolemetsa.
6 Me ha obligado a vivir en las tinieblas, como los muertos desde hace tiempo.
Wandikhazika mu mdima ngati amene anafa kale.
7 Ha levantado un muro a mi alrededor para que no pueda escapar; me ha atado con pesadas cadenas.
Wandimangira khoma kotero kuti sindingathawe, wandimanga ndi maunyolo.
8 Aunque siga clamando por ayuda, se niega a escuchar mi oración.
Ngakhale pamene ndifuwula kapena kupempha chithandizo, amakana pemphero langa.
9 Ha puesto piedras en mi camino y me envía por senderos torcidos.
Wanditsekera njira yanga ndi miyala yosema; ndipo wakhotetsa tinjira tanga.
10 Es un oso que me acecha, un león escondido listo para atacar,
Wandidikirira ngati chimbalangondo, wandibisalira ngati mkango.
11 Me arrastró de mi camino y me hizo pedazos, dejándome indefenso.
Wandikokera pambali ndi kundingʼambangʼamba, ndipo wandisiya wopanda thandizo.
12 Cargó su arco con una flecha y me usó como blanco,
Wakoka uta wake ndipo walunjikitsa mivi yake pa ine.
13 Me disparó en los riñones con sus flechas.
Walasa mtima wanga ndi mivi ya mʼphodo mwake.
14 Ahora todos se ríen de mí, cantando canciones que se burlan de mí todo el día.
Ndinakhala choseketsa cha anthu anga onse; amandinyodola mʼnyimbo zawo tsiku lonse.
15 Me ha llenado de amargura; me ha llenado de amargo ajenjo.
Wandidyetsa zowawa ndipo wandimwetsa ndulu.
16 Me ha roto los dientes con arenilla; me ha pisoteado en el polvo.
Wathyola mano anga ndi miyala; wandiviviniza mʼfumbi;
17 Me ha arrancado la paz; he olvidado todo lo bueno de la vida.
Wandichotsera mtendere; ndayiwala kuti kupeza bwino nʼchiyani.
18 Por eso digo: Mi expectativa de una larga vida ha desaparecido, junto con todo lo que esperaba del Señor.
Choncho ndikuti, “Ulemerero wanga wachoka ndi zonse zimene ndimayembekeza kwa Yehova.”
19 No olvides todo lo que he sufrido en mi agonía, tan amargo como el ajenjo y el veneno.
Kukumbukira masautso anga ndi kusowa pokhala, zili ngati zowawa ndi ndulu.
20 Ciertamente no lo he olvidado. Lo recuerdo demasiado bien, por eso me hundo en la depresión.
Ine ndikuzikumbukira bwino izi, ndipo moyo wanga wathedwa mʼkati mwanga.
21 Pero aún tengo esperanza cuando pienso en esto:
Komabe ndimakumbukira zimenezi, nʼchifukwa chake ndili ndi chiyembekezo.
22 Es por el amor fiel del Señor que nuestras vidas no están destruidas, pues con sus actos de misericordia nunca nos abandona.
Ife sitinawonongekeretu chifukwa chikondi cha Yehova ndi chachikulu, ndi chifundo chake ndi chosatha.
23 Él los renueva cada mañana. ¡Qué maravillosamente fiel eres, Señor!
Zimaoneka zatsopano mmawa uliwonse; kukhulupirika kwanu nʼkwakukulu.
24 El Señor es todo lo que necesito, me digo a mí mismo: Pondré mi esperanza en él.
Mu mtima mwanga ndimati, “Yehova ndiye zanga zonse; motero ndimamuyembekezera.”
25 El Señor es bueno con los que confían en él, con cualquiera que lo siga.
Yehova ndi wabwino kwa amene amayembekezera Iye, kwa munthu amene amafunafuna Iyeyo;
26 Es bueno esperar tranquilamente la salvación del Señor.
nʼkwabwino kudikira chipulumutso cha Yehova modekha.
27 Es bueno que el ser humano aprenda a soportar con paciencia la disciplina mientras es joven.
Nʼkwabwino kuti munthu asenze goli pamene ali wamngʼono.
28 Debe sentarse solos en silencio, porque es Dios quien lo ha disciplinado.
Akhale chete pa yekha, chifukwa Yehova wamusenzetsa golilo.
29 Debe inclinarse con el rostro hacia el suelo, porque aún puede haber esperanza.
Abise nkhope yake mʼfumbi mwina chiyembekezo nʼkukhalapobe.
30 Debe poner la mejilla a quien quiera abofetearlos; debe aceptar los insultos de los demás.
Apereke tsaya lake kwa iye amene angamumenye, ndipo amuchititse manyazi.
31 Porque el Señor no nos abandonará para siempre.
Chifukwa Ambuye satayiratu anthu nthawi zonse.
32 Aunque nos venga la tristeza, él nos muestra misericordia porque su amor fiel es muy grande.
Ngakhale amabweretsa zowawa, Iye adzawachitira chifundo, chifukwa chikondi chake ndi chosatha.
33 Porque no quiere herir ni causarle dolor a ninguno.
Pakuti sabweretsa masautso mwadala, kapena zowawa kwa ana a anthu.
34 Ya sea que alguien maltrate a todos los prisioneros de la tierra
Kuphwanya ndi phazi a mʼndende onse a mʼdziko,
35 Ole niegue a alguien sus derechos mientras el Altísimo lo ve,
kukaniza munthu ufulu wake pamaso pa Wammwambamwamba,
36 O sea que alguien engañe a otro en su caso legal, estas son cosas el Señor noaprueba.
kumana munthu chiweruzo cholungama— kodi Ambuye saona zonsezi?
37 ¿Quién habló y llegó a existir? ¿No fue el Señor quien lo ordenó?
Kodi ndani angayankhule zinthu nʼkuchitika ngati Ambuye sanavomereze?
38 Cuando el Altísimo habla puede ser para un desastre o para una bendición.
Kodi zovuta ndi zabwino sizituluka mʼkamwa mwa Wammwambamwamba?
39 ¿Por qué habría de quejarse un ser humano de las consecuencias de sus pecados?
Kodi nʼchifukwa chiyani munthu aliyense wamoyo amadandaula akalangidwa chifukwa cha machimo ake?
40 Debemos mirarnos a nosotros mismos, examinar nuestros actos y volver al Señor.
Tiyeni tisanthule ndi kuyesa njira zathu, ndipo tiyeni tibwerere kwa Yehova.
41 No nos limitemos a levantar la mano a Dios hacia el cielo, sino nuestra mente también, y digamos:
Tiyeni tikweze mitima yathu ndi manja athu kwa Mulungu kumwamba ndipo tinene kuti:
42 “Nosotros somos pecadores; nosotros somos rebeldes ¡y tú no nos has perdonado!”
“Ife tachimwa ndi kuwukira ndipo inu simunakhululuke.
43 Te has envuelto en ira y nos has perseguido, matándonos sin piedad. Has destruido sin piedad.
“Mwadzikuta ndi mkwiyo ndi kutilondola ndipo mwatitha mopanda chifundo.
44 Te has envuelto en una nube que ninguna oración puede penetrar.
Mwadzikuta mu mtambo kotero mapemphero athu sakukufikani.
45 Nos has convertido en residuos y desechos para las naciones de alrededor.
Mwatisandutsa zinyatsi ndi zinyalala pakati pa mitundu ya anthu.
46 Todos nuestros enemigos abren la boca para criticarnos.
“Adani anthu atitsekulira pakamwa.
47 Estamos aterrorizados y atrapados, devastados y destruidos.
Ife tadzazidwa ndi mantha pakuti tagwa mʼdzenje, tapasuka ndi kuwonongedwa.”
48 Las lágrimas brotan de mis ojos por la muerte de mi pueblo.
Misozi mʼmaso mwanga ikungoti mbwembwembwe chifukwa anthu anga akuwonongedwa.
49 Mis ojos rebosan de lágrimas todo el tiempo. No se detendrán
Misozi idzatsika kosalekeza, ndipo sidzasiya,
50 Hasta que el Señor mire desde el cielo y vea lo que pasa.
mpaka Yehova ayangʼane pansi kuchokera kumwamba ndi kuona.
51 Lo que he visto me atormenta por lo que ha sucedido a todas las mujeres de mi ciudad.
Mtima wanga ukupweteka poona zimenezi chifukwa cha akazi onse a mu mzinda.
52 Sin razón alguna mis enemigos me atraparon como a un pájaro.
Akundisaka ngati mbalame, amene anali adani anga, popanda chifukwa.
53 Intentaron matarme arrojándome a un pozo y tirándome piedras.
Ayesa kundipha pondiponya mʼdzenje ndi kundiponya miyala;
54 El agua me inundó hastala cabeza, y pensé que moriría.
madzi anamiza mutu wanga ndipo ndinkaganiza kuti imfa yayandikira.
55 Desde lo más profundo de la fosa te llamé, Señor.
Ndinayitana dzina lanu Inu Yehova, kuchokera mʼdzenje lozama.
56 Tú me oíste cuando oré: “Por favor, no ignores mi grito de auxilio”.
Inu munamva kudandaula kwanga. “Mundimvere kulira kwanga kopempha thandizo.”
57 Viniste a mí cuando te llamé, y me dijiste: “¡No tengas miedo!”
Munafika pafupi pamene ndinakuyitanani, ndipo munati, “Usaope.”
58 ¡Has tomado mi caso y me has defendido; has salvado mi vida!
Inu Ambuye munandiwombola ku mlandu wanga; munapulumutsa moyo wanga.
59 Señor, tú has visto las injusticias que se han cometido contra mí; ¡Defiéndeme, por favor!
Yehova, mwaona zoyipa zimene andichitira. Mundiweruzire ndinu!
60 Has observado lo vengativos que son y las veces que han conspirado contra mí.
Mwaona kuzama kwa kubwezera kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine.
61 Señor, tú has oído cómo me han insultado y lo que han tramado contra mí,
Inu Yehova mwamva kunyoza kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine,
62 ¡Cómo mis enemigos hablan contra mí y se quejan de mí todo el tiempo!
manongʼonongʼo a adani anga ondiwukira ine tsiku lonse.
63 ¡Mira! Ya sea que estén sentados o de pie, siguen burlándose de mí en sus canciones.
Tawaonani! Kaya ali pansi kapena kuyimirira, akundinyoza mu nyimbo zawo.
64 ¡Págales como se merecen, Señor, por todo lo que han hecho!
Inu Yehova, muwabwezere chowayenera, chifukwa cha zimene manja awo achita.
65 Dales algo para que sus mentes queden cubiertas! ¡Que tu maldición caiga sobre ellos!
Phimbani mitima yawo, ndipo matemberero anu akhale pa iwo!
66 Persíguelos en tu cólera, Señor, y deshazte de ellos de la tierra!
Muwalondole mwaukali ndipo muwawonongeretu pa dziko lapansi.