< Job 5 >
1 “Llama si quieres, pero ¿quién te va a responder? ¿A qué ángel te vas a dirigir?
“Itana ngati ungathe, koma ndani adzakuyankhe? Kodi ndi kwa mngelo uti ungapezeko thandizo?
2 Ciertamente la ira mata al necio y la envidia al simple.
Mkwiyo umapha chitsiru, ndipo njiru imawononga wopusa.
3 He visto a un necio hacerse fuerte, pero enseguida maldije su casa.
Ine ndinaona chitsiru chitamera mizu, koma mwadzidzidzi nyumba yake inatembereredwa.
4 Sus hijos nunca están a salvo; son aplastados en el tribunal sin nadie que los defienda.
Ana ake alibe ndi chitetezo chomwe; amaponderezedwa mʼbwalo la milandu popanda owateteza.
5 El hambriento se come todo lo que cosecha, tomando incluso lo que está protegido por un seto de espinas, mientras otros procuran robar su riqueza.
Anthu anjala amamudyera zokolola zake, amamutengera ndi za pa minga pomwe, ndipo anthu akhwinthi amafunkha chuma chake.
6 Porque el mal no nace del polvo, ni los problemas crecen de la tierra.
Pakuti masautso satuluka mʼfumbi, ndipo kuwukira sikuchokera mʼdothi.
7 Pero los seres humanos nacen para los problemas con la misma certeza que las chispas de un fuego vuelan hacia arriba.
Komatu munthu amabadwira kuti azunzike monga momwe mbaliwali zimathethekera mlengalenga.
8 “Si fuera yo, iría donde Dios y expondría mi caso ante él.
“Koma ndikanakhala ine, ndikanamudandawulira Mulungu; ndikanapereka mlandu wanga kwa Iye.
9 Él es quien hace cosas asombrosas, increíbles; ¡milagros que no se pueden contar!
Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingatheke kuwerengedwa.
10 Él hace llover sobre la tierra y envía agua a los campos.
Iye amagwetsa mvula pa dziko lapansi, ndipo amathirira minda ya anthu.
11 Exalta a los humildes y rescata a los que lloran.
Iye amakweza anthu wamba, ndipo iwo amene akulira amawayika pa malo otetezedwa.
12 Frustra los planes de los astutos para que no tengan éxito.
Iyeyo amalepheretsa chiwembu cha anthu ochenjera, kotero kuti cholinga chawo sichipindula kanthu.
13 Él atrapa a los sabios en sus propios pensamientos astutos, y los planes de la gente retorcida se ven truncados.
Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo, ndipo zolinga za atambwali amazithetsa msangamsanga.
14 De día están a oscuras, y a mediodía tropiezan como si fuera de noche.
Mdima umawagwera nthawi yamasana; nthawi yamasana amayenda moyambasayambasa monga nthawi ya usiku.
15 Pero Dios es el que salva de sus comentarios cortantes, así como salva a los pobres de las acciones de los poderosos.
Mulungu amapulumutsa amphawi ku lupanga la mʼkamwa mwawo; amawapulumutsa mʼmanja mwa anthu amphamvu.
16 Así los desvalidos tienen esperanza, y los malvados tienen que cerrar la boca.
Choncho osauka ali ndi chiyembekezo, ndipo anthu opanda chilungamo amawatseka pakamwa.
17 Mira qué feliz es la persona a la que Dios corrige, así que no desprecies la disciplina del Todopoderoso.
“Wodala munthu amene Mulungu amamudzudzula; nʼchifukwa chake usanyoze chilango cha Wamphamvuzonse.
18 Porque él causa dolor, pero proporciona alivio; él hiere, pero sus manos curan.
Pakuti Iye amavulaza koma amamanganso mabalawo; Iye amakantha munthu, komanso manja ake amachiritsa.
19 Él te salvará de muchos desastres; una multitud de males no te afectará.
Pakuti adzakupulumutsa ku masautso nthawi ndi nthawi, mavuto angachuluke bwanji, sadzakukhudza ndi pangʼono pomwe.
20 En tiempos de hambre te librará de la muerte, y en tiempos de guerra te salvará del poder de la espada.
Pa nthawi ya njala adzakulanditsa ku imfa, ndipo nthawi ya nkhondo adzakupulumutsa ku lupanga.
21 Estarás protegido de la calumnia de lengua afilada; y cuando llegue la violencia no tendrás miedo.
Adzakuteteza kwa anthu osinjirira, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha pamene chiwonongeko chafika.
22 Te reirás de la violencia y del hambre; no tendrás miedo de los animales salvajes,
Uzidzaseka pa nthawi ya chiwonongeko ndi ya njala, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha ndi zirombo za mʼdziko lapansi.
23 porque estarás en paz con las piedras del campo y los animales salvajes estarán en paz contigo.
Pakuti udzachita pangano ndi miyala ya mʼmunda mwako, ndipo nyama zakuthengo zidzakhala nawe mwamtendere.
24 Estarás seguro de que tu casa está a salvo, porque irás a donde vives y no habrá cosa alguna que te falte.
Udzadziwa kuti nyumba yako ndi malo otetezedwa; udzawerengera katundu wako ndipo sudzapeza kanthu kamene kasowapo.
25 También estarás seguro de que tendrás muchos hijos; tu descendencia será como la hierba de la tierra.
Udzadziwa kuti ana ako adzakhala ambiri, ndipo zidzukulu zako zidzakhala ngati udzu wa mʼdziko lapansi.
26 Vivirás hasta una edad madura como una gavilla de grano cuando se cosecha.
Udzafika ku manda utakalamba, monga mitolo ya zokolola pa nyengo yake.
27 Mira, lo hemos examinado y es verdad. Escucha lo que te digo y aplícalo a ti mismo”.
“Ife tafufuza zimenezi ndipo ndi zoona, choncho uzimvere ndi kuzitsata.”