< Job 38 >
1 Entonces el Señor respondió a Job desde el torbellino:
Apo Yehova anamuyankha Yobu mʼkamvuluvulu. Ndipo anati:
2 “¿Quién es el que cuestiona mi sabiduría hablando con tanta ignorancia?
“Kodi uyu ndani amene akusokoneza uphungu wanga poyankhula mawu opanda nzeru?
3 Prepárate, y sé fuerte, porque voy a interrogarte y debes responderme:
Onetsa chamuna; ndikufunsa ndipo undiyankhe.
4 “¿Dónde estabas cuando puse los cimientos de la tierra? Dime, si tienes ese conocimiento.
“Kodi unali kuti pamene ndinkayika maziko a dziko lapansi? Ndiwuze ngati ukudziwa.
5 ¿Quién decidió sus dimensiones? ¿No lo sabes? ¿Quién extendió una línea de medición?
Ndani amene analemba malire ake? Ndithudi iwe ukudziwa! Ndani amene anayeza ndi chingwe dzikoli?
6 ¿Sobre qué se apoyan sus cimientos? ¿Quién puso su piedra angular,
Kodi maziko ake anawakumba potani, kapena ndani anayika mwala wake wapangodya,
7 cuando las estrellas de la mañana cantaron juntas y todos los ángeles gritaban de alegría.
pamene nyenyezi za kummawa zinkayimba pamodzi ndipo angelo onse a Mulungu ankafuwula mokondwa?
8 “Quien fijó los límites del mar cuando nació?
“Kodi ndani amene anatsekera nyanja pamene inkalengedwa, pamene inkachita ngati kutumphuka pansi pa dziko,
9 ¿Quién la vistió de nubes y la envolvió en un manto de profunda oscuridad?
pamene ndinasandutsa mitambo kukhala chovala chake ndi kuyikulunga mu mdima wandiweyani,
10 Yo establecí sus límites, marcando sus fronteras.
pamene ndinayilembera malire ake ndikuyikira zitseko ndi mipiringidzo yake.
11 Le dije: ‘Puedes venir aquí, pero no más lejos. Aquí es donde se detienen tus orgullosas olas’.
Pamene ndinati, ‘Ufike mpaka apa ndipo usapitirire apa ndiye pamene mafunde ako amphamvuwo azilekezera?’
12 “Durante tu vida, ¿has ordenado alguna vez que comience la mañana?
“Kodi chibadwire chako unalamulapo dzuwa kuti lituluke mmawa, kapena kuti mʼbandakucha ukhalepo pa nthawi yake,
13 ¿Has dicho alguna vez a la aurora dónde debe aparecer para que se apodere de los rincones de la tierra y sacuda a los malvados?
kuti kuwalako kuwunikire dziko lonse lapansi ndi kuthamangitsa anthu oyipa?
14 La tierra se cambia como la arcilla bajo un sello; sus rasgos destacan como una prenda arrugada.
Chifukwa cha kuwala kwa usana mapiri ndi zigwa zimaonekera bwino ngati zilembo za chidindo pa mtapo; zimaonekera bwino ngati makwinya a chovala.
15 La ‘luz’ de los malvados les es quitada; sus actos de violencia son detenidos.
Kuwala kwa dzuwako sikuwafikira anthu oyipa, ndipo dzanja lawo silingathe kuchita kanthu.
16 “¿Has entrado en las fuentes del mar? ¿Has explorado sus profundidades ocultas?
“Kodi unayendapo pansi penipeni pa nyanja kapena pa magwero ake ozama?
17 ¿Te han mostrado dónde están las puertas de la muerte? ¿Has visto las puertas de las tinieblas?
Kodi anakuonetsapo zipata za imfa? Kodi unaonako ku dziko la anthu akufa kumene kuli mdima wandiweyani?
18 ¿Sabes hasta dónde se extiende la tierra? ¡Dime si sabes todo esto!
Kodi kukula kwa dziko lapansi umakudziwa? Undiwuze ngati ukuzidziwa zonsezi.
19 ¿En qué dirección vive la luz? ¿Dónde habitan las tinieblas?
“Kodi njira yopita kumene kumakhala kuwala ili kuti? Nanga mdima umakhala kuti?
20 ¿Puedes llevarlas a casa? ¿Conoces el camino hacia donde viven?
Kodi iwe ungathe kuziperekeza kwawoko zimenezi? Kodi ukuyidziwa njira yopita kwawoko?
21 ¡Claro que lo sabes, porque ya habías nacido entonces! ¡Has vivido tanto tiempo!
Ndithu, iwe ukuyidziwa, poti paja nthawi imeneyo nʼkuti utabadwa kale! Wakhala ndi moyo zaka zambiridi!
22 “¿Has estado donde se guarda la nieve? ¿Has visto dónde se guarda el granizo?
“Kodi unalowamo mʼnyumba zosungira chisanu chowundana kapena unayionapo nyumba yosungira matalala,
23 Los he guardado para el tiempo de la angustia, para el día de la guerra y de la batalla.
zimene ndazisungira nthawi ya mavuto ndi nthawi yomenyana ndi ya nkhondo?
24 ¿Conoces el camino hacia donde viene la luz, o hacia donde sopla el viento del este sobre la tierra?
Kodi umadziwa njira ya kumene kumachokera chingʼaningʼani kapena njira ya kumene kumachokera mphepo ya kummawa imene ili pa dziko lonse lapansi?
25 ¿Quién abre un canal para que fluya la lluvia? ¿Quién crea un camino para el rayo?
Kodi ndani amene amakonza ngalande za mvula, nanga ndani anakonza njira yoyendamo mphenzi,
26 “¿Quién lleva la lluvia a una tierra deshabitada, a un desierto donde no vive nadie,
kuthirira madzi dziko limene sikukhala munthu, chipululu chopandamo munthu,
27 para regar un páramo reseco y hacer crecer la hierba verde?
kukhutitsa nthaka yowuma yagwaa ndi kumeretsamo udzu?
28 ¿Tiene la lluvia un padre? ¿Quién fue el padre de las gotas de rocío?
Kodi mvula ili ndi abambo ake? Nanga madzi a mame anawabereka ndani?
29 ¿Quién fue la madre del hielo? ¿Tiene madre la escarcha del aire?
Kodi madzi owundana anawabereka ndani? Ndani amene anabereka chisanu chochokera kumwamba
30 El agua se convierte en hielo duro como una roca; su superficie se congela.
pamene madzi amawuma gwaa ngati mwala, pamene madzi a pa nyanja amazizira, nalimba kuti gwaa?
31 ¿Puedes unir las estrellas de las Pléyades? ¿Puedes soltar el cinturón de la constelación de Orión?
“Kodi iwe ungayimitse kuyenda kwa nyenyezi? Kodi ungathe kuletsa kuyenda kwa nsangwe ndi akamwiniatsatana?
32 ¿Puedes guiar a las estrellas de Mazarot en el momento adecuado? ¿Puedes dirigir la constelación de la Osa Mayor y sus otras estrellas?
Kodi ungathe kuwongolera nyenyezi pa nyengo yake kapena kutsogolera nyenyezi yayikulu ya chimbalangondo pamodzi ndi ana ake?
33 ¿Conoces las leyes de los cielos? ¿Puedes aplicarlas a la tierra?
Kodi malamulo a mlengalenga umawadziwa? Kodi ungathe kukhazikitsa ulamuliro wa Mulungu pa dziko lapansi?
34 “¿Puedes gritarles a las nubes y ordenarles que derramen lluvia sobre ti?
“Kodi iwe ungathe kulamula mitambo kuti igwetse mvula ya chigumula?
35 ¿Puedes enviar rayos y dirigirlos, para que te respondan diciendo: ‘Aquí estamos’?
Kodi ungathe kutumiza zingʼaningʼani kuti zingʼanime? Kodi zimabwera pamaso pako ndi kuti, ‘Tili pano?’
36 ¿Quién ha puesto la sabiduría dentro de la gente? ¿Quién ha dado entendimiento a la mente?
Kodi ndani anayika nzeru mu mtima, ndani analonga mʼmaganizo nzeru zomvetsa zinthu?
37 ¿Quién es tan inteligente como para contar las nubes? ¿Quién puede voltear los cántaros de agua del cielo sobre sus lados
Wanzeru ndani amene angathe kuwerenga mitambo? Ndani angathe kupendeketsa mitsuko ya madzi akuthambo
38 cuando el polvo se ha cocido en una masa sólida?
pamene fumbi limasanduka matope, ndipo matopewo amawumbika?
39 “¿Puedes cazar una presa para el león? ¿Puedes alimentar a los cachorros de león
“Kodi ndani amawusakira chakudya mkango waukazi ndi kukhutitsa misona ya mikango
40 cuando se agazapan en sus guaridas y acechan en los arbustos?
pamene ili khale mʼmapanga mwawo kapena pamene ikubisala pa tchire?
41 ¿Quién proporciona alimento al cuervo cuando sus crías claman a Dios, débiles de hambre?”
Kodi amamupatsa khwangwala chakudya chake ndani pamene ana ake akulirira kwa Mulungu ndi kumayendayenda chifukwa chosowa zakudya?