< Job 26 >
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 “Qué útil has sido para este débil hombre que soy. Qué solidario has sido con el débil.
“Wamuthandizadi munthu wopanda mphamvu! Walimbitsadi dzanja la munthu wofowoka!
3 Qué buenos consejos le has dado a este ignorante, demostrando que tienes mucha sabiduría.
Wapereka malangizo kwa munthu amene alibe nzeru! Ndipotu waonetsadi nzeru zochuluka!
4 ¿Quién te ayudó a decir estas palabras? ¿Quién te ha inspirado a decir tales cosas?
Kodi wakuthandiza ndani kuti uyankhule mawu awa? Ndipo ndi mzimu wa yani umene unayankhula pakamwa pako?
5 “Los muertos tiemblan, los que están bajo las aguas.
“Mizimu ya anthu akufa ikunjenjemera pansi pa madzi, ndi zonse zokhala mʼmadzimo.
6 El Seol está desnudo ante Dios, Abadón está descubierto. (Sheol )
Dziko la anthu akufa ndi lapululu pamaso pa Mulungu; chiwonongeko ndi chosaphimbidwa. (Sheol )
7 Extiende el cielo del norte sobre el espacio vacío; cuelga el mundo sobre la nada.
Mulungu anayala thambo la kumpoto pa phompho; Iye anakoloweka dziko lapansi mʼmalo mwake pamene panali popanda nʼkanthu komwe.
8 Recoge la lluvia en sus nubes de tormenta que no se rompen bajo el peso.
Amasunga madzi ambiri mʼmitambo yake, koma mitamboyo siphulika chifukwa cha kulemera kwa madziwo.
9 Él vela su trono; lo cubre con sus nubes.
Iye amaphimba mwezi wowala, amawuphimba ndi mitambo yake.
10 Sobre la superficie de las aguas puso una frontera; fijó un límite que divide la luz de las tinieblas.
Mulungu anawalembera madzi malire wonga uta, kukhala malire pakati pa kuwunika ndi mdima.
11 Las columnas del cielo tiemblan; tiemblan de miedo ante su reprimenda.
Mizati yochirikiza mitambo yakumwamba imanjenjemera, ndi kudabwa pa kudzudzula kwake.
12 Calmó el mar con su poder; porque sabía qué hacer aplastó a Rahab.
Ndi mphamvu zake anatontholetsa nyanja; ndi nzeru zake anakantha chirombo cha mʼmadzi chija chotchedwa Rahabe.
13 El aliento de su voz embelleció los cielos; con su mano atravesó la serpiente que se desliza.
Ndi mpweya wake anayeretsa zamumlengalenga, dzanja lake linapha chinjoka chothawa chija.
14 Esto es sólo un poco de todo lo que hace; lo que oímos de él es apenas un susurro, así que quién puede entender su poder atronador?”
Zimenezi ndi pangʼono chabe mwa ntchito yake; tingomva pangʼono za Iye ngati kunongʼona! Kodi ndani angathe kudziwa kukula kwa mphamvu zake?”