< Job 14 >
1 “La vida es corta y está llena de problemas,
“Munthu wobadwa mwa amayi amakhala masiku owerengeka ndipo ndi odzaza ndi mavuto okhaokha.
2 como una flor que florece y se marchita, como una sombra pasajera que pronto desaparece.
Amaphuka ngati duwa ndipo kenaka amafota; amathawa ngati mthunzi ndipo sakhalitsa.
3 ¿Acaso te fijas en mí, Dios? ¿Por qué tienes que arrastrarme a los tribunales?
Kodi munthu wotereyo nʼkumuyangʼanitsitsa? Kodi mungamubweretse pamaso panu kuti mumuzenge mlandu?
4 ¿Quién puede sacar algo limpio de lo impuro? Nadie.
Ndani angatulutse chabwino mʼchoyipa? Palibe ndi mmodzi yemwe!
5 Tú has determinado cuánto tiempo viviremos: el número de meses, un límite de tiempo para nuestras vidas.
Masiku a munthu ndi odziwikiratu; munakhazikitsa chiwerengero cha miyezi yake ndipo munamulembera malire amene sangathe kuwalumpha.
6 Así que déjanos tranquilos y danos un poco de paz, para que, como el obrero, podamos disfrutar de unas horas de descanso al final del día.
Choncho Inu mumufulatire ndipo mumuleke apumule kufikira atakondwera nawo moyo ngati munthu waganyu.
7 “Incluso un árbol cortado tiene la esperanza de volver a brotar, de echar brotes y seguir viviendo.
“Mtengo uli nacho chiyembekezo: ngati wadulidwa, udzaphukiranso ndipo nthambi zake sizidzaleka kuphukira.
8 Aunque sus raíces envejezcan en la tierra y su tronco muera en el suelo,
Mizu yake ingathe kukalamba mʼnthaka ndipo chitsa chake nʼkuwola pa dothi,
9 sólo un hilo de agua hará que brote y se ramifique como una planta joven.
koma pamene chinyontho chafika udzaphukira ndipo udzaphuka nthambi ngati mtengo wanthete.
10 “Pero los seres humanos mueren, su fuerza disminuye; perecen, y ¿dónde están entonces?
Koma munthu amafa nayikidwa mʼmanda, amapuma mpweya wotsiriza ndipo kutha kwake nʼkomweko.
11 Como el agua que se evapora de un lago y un río que se seca y desaparece,
Monga madzi amaphwera mʼnyanja kapena monga mtsinje umaphwera nuwuma,
12 así los seres humanos se acuestan y no vuelven a levantarse. NO despertarán de su sueño hasta que los cielos dejen de existir.
momwemonso munthu amagona ndipo sadzukanso; mpaka zamlengalenga zidzathe, anthu sadzauka kapena kudzutsidwa ku tulo tawo.
13 “Quisiera que me escondieran en el Seol; escóndeme allí hasta que tu ira desaparezca. Fija allí un tiempo definido para mí, y acuérdate de mi. (Sheol )
“Aa, Inu mukanangondibisa mʼmanda ndi kundiphimba kuti ndisaoneke mpaka mkwiyo wanu utapita! Achikhala munandiyikira nthawi, kuti pambuyo pake mundikumbukirenso. (Sheol )
14 ¿Volverán a vivir los muertos? Entonces tendría esperanza durante todo mi tiempo de angustia hasta que llegue mi liberación.
Munthu akafa, kodi adzakhalanso ndi moyo? Masiku anga onse a moyo wovutikawu ndidzadikira mpaka itafika nthawi yomasulidwa.
15 Me llamarías y yo te respondería; me añorarías, al ser que has creado.
Inu mudzandiyitane ndipo ndidzakuyankhani; inu mudzafunitsitsa kuona cholengedwa chimene munachipanga ndi manja anu.
16 Entonces me cuidarías y no me vigilarías para ver si peco.
Ndithudi pamenepo mudzayangʼana mayendedwe anga koma simudzalondola tchimo langa.
17 Mis pecados estarían sellados en una bolsa y tú cubrirías mi culpa.
Zolakwa zanga zidzakulungidwa mʼthumba; inu mudzaphimba tchimo langa.
18 “Pero así como las montañas se desmoronan y caen, y las rocas se derrumban;
“Koma monga phiri limakokolokera ndi kuswekasweka ndipo monga thanthwe limasunthira kuchoka pa malo ake,
19 así como el agua desgasta las piedras, como las inundaciones arrastran el suelo, así destruyes la esperanza que tienen los pueblos.
monganso madzi oyenda amaperesera miyala ndipo madzi othamanga amakokololera nthaka, momwemonso Inu mumawononga chiyembekezo cha munthu.
20 Los dominas continuamente y desaparecen; distorsionas sus rostros al morir y entonces los despides.
Inu mumamugonjetsa kamodzinʼkamodzi ndipo munthuyo nʼkutheratu; Inu mumasintha maonekedwe a nkhope yake ndipo mumamutaya kutali.
21 Sus hijos pueden llegar a ser importantes o caer de sus puestos, pero ellos no saben ni se enteran de nada de esto.
Ana ake akamalemekezedwa, iyeyo sazidziwa zimenezo; akamachititsidwa manyazi iye saziona zimenezo.
22 Cuando la gente muere sólo conoce su propio dolor y está triste por sí misma”.
Iye amangomva zowawa za mʼthupi lake ndipo amangodzilirira yekha mwini wakeyo.”