< Isaías 9 >
1 Aun así, no habrá más oscuridad para los que sufrieron. En el pasado humilló a la tierra de Zabulón y a la tierra de Neftalí, pero en el futuro dará honor a la Galilea de los extranjeros que está en la ruta que va del Jordán al mar.
Anthu amene anali ndi nkhawa, sadzakhalanso otaya mtima. Masiku amakedzana Mulungu ananyozetsa dziko la Zebuloni ndi dziko la Nafutali, koma kutsogolo kuno dera lonse la Galileya, limene lili dziko la anthu a mitundu ina, kuyambira ku nyanja yayikulu, mʼmbali mwa Yorodani, adzalisandutsa laulemu.
2 El pueblo que camina en la oscuridad verá una luz brillante; una luz brillará sobre los que viven en una tierra de total oscuridad.
Anthu oyenda mu mdima awona kuwala kwakukulu; kwa iwo okhala mʼdziko la mdima wandiweyani kuwunika kwawafikira.
3 Hará que la nación crezca enormemente y la hará extremadamente feliz. El pueblo festejará ante ti como festejan los pueblos en la época de la cosecha, como festejan los soldados al repartir el botín.
Inu mwauchulukitsa mtundu wanu ndipo mwawonjezera chimwemwe chawo. Iwo akukondwa pamaso panu, ngati mmene anthu amakondwera nthawi yokolola, ngatinso mmene anthu amakondwera pamene akugawana zolanda ku nkhondo.
4 Porque romperás el yugo que los agobia, la barra sobre sus hombros y la vara de los opresores que los golpean, como hiciste cuando derrotaste al ejército madianita.
Monga munachitira pogonjetsa Amidiyani, inu mwathyola goli limene limawalemera, ndodo zimene amamenyera mapewa awo, ndiponso mikwapulo ya anthu owazunza.
5 Porque toda bota del ejército que pisoteó ruidosamente a la gente, y todo uniforme empapado en sangre, será quemado, serán combustible para el fuego.
Nsapato iliyonse ya munthu wankhondo, ndiponso chovala chilichonse chodonthekera magazi zidzatenthedwa pa moto ngati nkhuni.
6 Porque nos nacerá un niño, se nos dará un hijo. Él llevará la responsabilidad de gobernar. Se llamará Consejero maravilloso, Dios poderoso, Padre eterno, Príncipe de la paz.
Chifukwa mwana watibadwira, mwana wamwamuna wapatsidwa kwa ife, ndipo ulamuliro udzakhala pa phewa lake. Ndipo adzamutcha dzina lake lakuti Phungu Wodabwitsa, Mulungu Wamphamvu, Atate Amuyaya, ndi Mfumu ya Mtendere.
7 Su gobierno y la paz que trae no conocen límites y nunca llegarán a su fin. Se sentará en el trono de David y gobernará su reino, haciéndolo seguro. Actuará con principios de justicia y bondad, desde el momento en que comience su gobierno y por toda la eternidad. El Señor Todopoderoso está decidido a que esto ocurra.
Ulamuliro ndi mtendere wake zidzakhala zopanda malire. Iye adzalamulira ufumu wake ali pa mpando waufumu wa Davide, ndipo adzawukhazikitsa ndi kuwuchirikiza mwa chiweruzo cholungama ndi pochita zachilungamo kuyambira nthawi imeneyo mpaka muyaya. Ndi mtima wake wonse, Yehova Wamphamvuzonse watsimikiza kuchita zimenezi.
8 El Señor ha enviado un mensaje dirigido a Jacob, y sus consecuencias caerán sobre Israel.
Ambuye atumiza mawu otsutsa Yakobo; ndipo mawuwo agwera pa Israeli.
9 Todo el pueblo se dará cuenta pronto: Efraín y los pueblos que viven en Samaria. Con orgullo y arrogancia dicen:
Anthu onse okhala mu Efereimu ndi okhala mu Samariya, adzadziwa zimenezi. Iwo amayankhula modzikuza kuti,
10 “Los edificios de ladrillo se han derrumbado, pero los reconstruiremos con piedra labrada; las higueras de sicómoro han sido cortadas, pero las reemplazaremos con cedros”.
“Ngakhale njerwa zagumuka, koma ife tidzamanga ndi miyala yosema. Mitanda ya mkuyu yagwetsedwa, koma ife tidzayika mitanda ya mkungudza mʼmalo mwake.”
11 Pero el Señor ha fortalecido a los enemigos de Rezín contra Israel y los ha alentado.
Koma Yehova wadzutsa adani kuti alimbane nawo ndipo wawafulumiza adani awo kuti amenyane nawo.
12 Los arameos del este y los filisteos del oeste han devorado con avidez a Israel. En todo esto sigue enojado y su mano sigue levantada.
Asiriya ochokera kummawa ndi Afilisti ochokera kumadzulo ndipo ayasama pakamwa kuti adye a Israeli. Komabe, mkwiyo wake sunawachokere, mkono wake uli chitambasulire.
13 Pero el pueblo no volvió al que lo castigó; no vino a adorar al Señor Todopoderoso.
Koma anthu sanabwerere kwa amene anawakantha uja, ngakhale kufunafuna Yehova Wamphamvuzonse.
14 Así que en un solo día el Señor le cortará a Israel la cabeza y la cola, las palma y los juncos.
Choncho Yehova adzadula mutu wa Israeli pamodzi ndi mchira womwe, nthambi ya kanjedza ndi bango lomwe tsiku limodzi;
15 Los ancianos y la gente honrada son la cabeza, y los profetas que enseñan la mentira son la cola.
mutuwo ndiye akuluakulu ndi olemekezeka, mchira ndiye aneneri ophunzitsa zabodza.
16 Los líderes del pueblo los han engañado; los que se guiaban por ellos están confundidos.
Amene amatsogolera anthuwa ndiwo amawasocheretsa, ndipo otsogoleredwa amatayika.
17 Por eso el Señor no está contento con sus jóvenes, no tiene compasión de sus huérfanos y viudas, porque todos ellos son hipócritas y hacen el mal: todos hablan con necedad. Por todo esto él sigue enojado y su mano permanece alzada.
Nʼchifukwa chake Ambuye adzakondwera nawo achinyamata, ngakhale kuwachitira chifundo ana amasiye ndi akazi amasiye, pakuti aliyense ndi wosapembedza Mulungu ndiponso ndi wochimwa ndipo aliyense amayankhula zopusa. Komabe, mkwiyo wake sunawachokere, mkono wake uli chitambasulire.
18 Porque la maldad arde como un fuego, quemando zarzas y espinas, incendiando el bosque y enviando una columna de humo que se eleva.
Ndithu kuyipa kwa anthuwo kumayaka ngati moto; moto wake umanyeketsa mkandankhuku ndi minga, umayatsa nkhalango yowirira, ndipo utsi wake umachita kuti toloo ngati mtambo.
19 La ira del Señor Todopoderoso quema la tierra. El pueblo es como combustible para el fuego, y nadie trata de ayudar a nadie.
Dziko lidzatenthedwa ndi ukali wa Yehova Wamphamvuzonse, dziko lidzatenthedwa ndipo anthu adzakhala ngati nkhuni zosonkhera moto; palibe munthu amene adzachitire chifundo mʼbale wake.
20 La gente destruye a los que están a su diestra, pero siguen teniendo hambre de más; luego destruyen a los que están a su siniestra, pero siguen sin estar satisfechos. Al final incluso se destruyen a sí mismos!
Kudzanja lamanja adzapeza chakudya nʼkudya, koma adzakhalabe ndi njala; kudzanja lamanzere adzapeza chakudya nʼkudya, koma sadzakhuta. Aliyense azidzadya ana ake omwe.
21 Manasés destruye a Efraín, y Efraín destruye a Manasés. Juntos se vuelven para destruir a Judá. En todo esto él sigue enojado y su mano sigue alzada.
Manase adzadya Efereimu ndipo Efereimu adzadya Manase; onsewa pamodzi adzadya Yuda. Komabe pa zonsezi, mkwiyo wake sunawachokere, mkono wake uli chitambasulire.