< Ezequiel 40 >

1 Al principio del año, el día diez del mes del vigésimo quinto año de nuestro exilio, (catorce años después de la toma de Jerusalén), fue el día exacto en que el poder del Señor vino sobre mí y me llevó allí a la ciudad.
Kumayambiriro a chaka cha 25, cha ukapolo wathu, tsiku la khumi lamwezi, patapita zaka khumi ndi zinayi mzinda wa Yerusalemu utawonongedwa, pa tsiku lomwelo dzanja la Yehova linali pa ine ndipo Iye anapita nane ku Yerusalemu.
2 Dios me llevó al país de Israel en visión y me posó en una montaña muy alta. En el lado sur de la montaña había edificios que parecían ser una ciudad.
Mʼmasomphenyawo Yehova ananditenga ndi kupita nane ku dziko la Israeli ndipo anandiyika pa phiri lalitali kwambiri, moti ndinaona ngati mzinda.
3 Cuando me llevó allí, vi a un hombre que parecía de bronce brillante. Llevaba en la mano un cordón de lino y una vara de medir, y estaba de pie en la entrada.
Atandifikitsa kumeneko ndinaona munthu wonyezimira ngati mkuwa. Iye anali atayima pa chipata ndipo mʼdzanja lake munali chingwe cha nsalu yabafuta ndi ndodo yoyezera.
4 “Hijo de hombre”, me dijo, “mira con tus ojos, escucha con tus oídos. Concéntrate en todo lo que voy a mostrarte, porque esa es la razón por la que te han traído aquí. Debes explicar al pueblo de Israel lo que se te ha mostrado, todo lo que ves”.
Munthuyo anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, penyetsetsa ndipo umvetse bwinobwino. Uyikepo mtima wako pa zonse zimene ndikukuonetsa pakuti anakubweretsa kuno kuti uwone zimenezi. Tsono ukawawuze Aisraeli zonse zimene uzione.”
5 Pude ver un muro que rodeaba el Templo. La vara de medir que sostenía el hombre medía seis codos largos (un codo largo es un codo más un palmo). Midió el muro con un grosor de seis codos y una altura de seis codos.
Ine ndinaona khoma litazungulira mbali zonse za Nyumba ya Mulungu. Mʼdzanja la munthuyo munali bango lopimira limene kutalika kwake kunali kwa mamita atatu. Atayeza chipupacho anapeza kuti kuchindikira kwake kunali mamita atatu, ndiponso kutalika kwake kunalinso mamita atatu.
6 Luego subió los escalones de la puerta que daba al este. Midió que el umbral de la puerta tenía seis codos de profundidad.
Anapita ku chipata chakummawa. Anakwera pa makwerero a nyumbayo, nayeza chiwundo choyamba cha chipatacho; kutalika kwake kunali mamita atatu.
7 Más allá, había nichos que medían seis por seis codos, con cinco codos entre los nichos. El umbral de la entrada interior que daba al pórtico medía seis codos.
Kudutsa chiwundo choyambachi, panali zipinda za alonda zisanu ndi chimodzi, zitatu kudzanja lamanja, zitatu kudzanja lamanzere. Chilichonse chinali cha mamita atatu mulitali mwake, chimodzimodzinso mulifupi mwake. Mipata ya pakati pa zipindazo inali ya mamita awiri ndi theka. Ndipo chiwundo cha pa chipata pafupi ndi khonde lapachipata, chinali mamita atatu.
8 Luego midió el pórtico de entrada.
Ndipo iye anayeza khonde la chipata ndipo chinali cha mamita atatu.
9 Tenía una profundidad de ocho codos, y sus postes eran de dos codos de grosor. El pórtico de entrada daba al Templo.
Anayeza khonde ndipo linali mamita anayi. Mphuthu zake zinali mita imodzi kuchindikira kwake. Khonde lamʼkati lapachipata linali kumapeto kwenikweni pafupi ndi Nyumba ya Mulungu.
10 A cada lado de la entrada de la puerta oriental había tres nichos que medían lo mismo. Los postes de cada lado también medían lo mismo.
Mʼkati mwa chipata chakummawa munali zipinda za alonda zitatu mbali iliyonse. Zitatu zonsezo zinali zofanana, ndipo khonde la pakati pa zipindazo linali lofanana.
11 El ancho de la puerta de entrada medía diez codos. Su longitud era de trece codos.
Kenaka anayeza chipata cholowera; mulifupi mwake munali mamita asanu ndipo mulitali mwake munali mamita asanu ndi limodzi ndi theka.
12 Un muro de un codo de alto estaba delante de la alcoba, y las alcobas medían seis codos por seis codos.
Kutsogolo kwa chipinda chilichonse cha alonda kunali khoma lalifupi lotalika theka la mita, ndipo mbali iliyonse ya zipinda za alondazo inali yotalika mamita atatu.
13 Luego midió la puerta de entrada desde el techo de una alcoba hasta el techo de la de enfrente. Había veinticinco codos desde una puerta hasta la opuesta.
Ndipo anayeza kutalika kwa mulifupi mwa chipata cholowera, kuchokera ku khoma lakumbuyo la chipinda chimodzi mpaka ku khoma la chipinda china; kuchokera ku chitseko mpaka ku chitseko china. Kutalika kwake kunali mamita khumi ndi awiri ndi theka.
14 Luego midió la distancia entre los postes en sesenta codos. La puerta daba la vuelta al patio.
Anayezanso khonde lamʼkati ndipo linali la mamita makumi atatu. Ndipo mozungulira khondelo munali bwalo. Muyesowu sukuphatikiza khonde loyangʼanana ndi bwalo.
15 Había cincuenta codos desde la entrada de la puerta hasta el extremo del pórtico interior.
Kuchokera pa chipata cholowera mpaka ku mapeto a khonde la chipata, kutalika kwake kunali mamita 27.
16 Las alcobas y sus pilares tenían ventanas estrechas en todo el interior de la puerta. Los pórticos también tenían ventanas en todo el interior. Todos los postes estaban decorados con diseños de palmeras.
Makoma a zipinda ndiponso makoma a pakati pa zipindazo anali ndi mazenera. Khonde lamʼkati linalinso ndi mazenera mʼkati mwake. Pa makoma onsewo anajambulapo zithunzi za kanjedza.
17 Me llevó al patio exterior. Vi que se habían construido habitaciones y un pavimento alrededor del patio. Había treinta habitaciones que daban al pavimento.
Kenaka munthuyo anandilowetsa mʼbwalo lakunja, ndipo ndinaona zipinda zina ndi msewu wa miyala wozungulira bwalo lonse. Zipinda zonse zinali makumi atatu ndipo zinkayangʼana msewuwo.
18 El pavimento se denominaba pavimento inferior y se extendía a lo largo de los lados de las puertas y tenía la misma longitud que éstas.
Utali wa mulifupi mwa msewuwo unkayenda mamita 27 kufanana ndi utali wa chipata cholowera. Uwu unali msewu wa mʼmunsi.
19 Midió la distancia desde el frente de la puerta inferior hasta el lado más alejado del patio interior como cien codos, tanto hacia el lado este como hacia el norte.
Tsono, anayeza kutalika kwa bwalo kuyambira chipata cholowera choyamba mpaka polowera pa chipata chakunja cha bwalo la mʼkati. Kutalika kwake kunali mamita makumi asanu.
20 También midió la longitud y la anchura de la puerta del patio exterior que daba al norte.
Kenaka munthuyo anayeza mulitali ndi mulifupi mwa chipata chimene chimayangʼana kumpoto, chotulukira kunja.
21 Sus tres nichos a ambos lados, sus postes y su pórtico medían lo mismo que la primera puerta, y tenía cincuenta metros de largo y veinticinco de ancho.
Zipinda za alonda zimene zinalipo zitatu mbali iliyonse, makoma ake ndi khonde zinali ndi muyeso wofanana ndi wachipata choyamba chija. Kutalika kwake kunali mamita 27 ndipo mulifupi mwake munali mamita 13.
22 Las ventanas, el pórtico y los adornos de las palmeras eran los mismos que los de la puerta que daba al este. Tenía siete peldaños que conducían a ella, con su pórtico frente a ellos.
Mipata yake, khonde lake ndi zojambula za kanjedza zinali ndi miyeso yofanana ndi za chipata chakummawa. Chipatacho chinali ndi makwerero asanu ndi awiri ndipo kotsirizira kwa chipatacho kunali khonde.
23 Había una entrada al patio interior que daba a la puerta norte, al igual que la puerta este. Midió la distancia desde la entrada hasta la puerta como cien codos.
Panalinso chipata cholowera ku bwalo lamʼkati chofanana ndi chakummawa chimene chimayangʼanana ndi chipata chakumpoto, chofanana ndi cha mbali ya kummawa. Anachiyeza kuchokera ku chipata china mpaka ku chipata china. Kutalika kwake kunali mamita makumi asanu.
24 Me llevó al lado sur, y vi una puerta que daba al sur. Midió sus postes y su pórtico, y medían lo mismo que los anteriores.
Ndipo munthuyo anapita nane ku mbali yakummwera ndipo ndinaona chipata chakummwera. Iye anayeza mphuthu zake ndi khonde ndipo zinali ndi miyeso yofanana ndi ya zina zija.
25 Tanto la puerta como el pórtico tenían ventanas a su alrededor que eran como las otras ventanas. Tenía cincuenta codos de largo y veinticinco de ancho.
Mʼzipinda za chipata cholowera chimenechi ndi mʼkhonde lake munali mipata yofanana ndi ya mʼzipinda zina. Mulitali mwake munali mamita 27, mulifupi mwake munali mamita 13.
26 Tenía siete escalones que subían a ella, y su pórtico estaba orientado hacia ellos. Tenía un poste a cada lado con dibujos de palmeras.
Chipatacho chinali ndi makwerero asanu ndi awiri ndi khonde kotsirizira kwake. Chipindacho chinali ndi zojambula za kanjedza ku mbali zonse za makoma.
27 El patio interior también tenía una entrada que daba al sur, y midió la distancia desde la entrada hasta la puerta del sur como cien codos.
Bwalo lamʼkati linalinso ndi chipata kummwera. Munthuyo analiyeza kuchokera ku chipata chimenechi mpaka ku chipata chakunja. Kutalika kwake kunali mamita makumi asanu.
28 Me llevó al patio interior por la puerta sur, y midió la puerta sur. Medía lo mismo que las anteriores.
Ndipo munthu uja anandilowetsa mʼbwalo lamʼkati kudzera ku chipata chakummwera. Anayeza chipatachi ndipo chinali chofanana ndi zinzake zija.
29 Sus alcobas, sus postes y su pórtico tenían las mismas medidas que los anteriores. La puerta y su pórtico tenían ventanas alrededor. Medía cincuenta codos de largo y veinticinco de ancho.
Zipinda zake za alonda, makoma ake ndi khonde lake zinali zofanana ndi zina zija. Chipata cholowera ndi khonde lake zinali ndi mipata mʼmbali zonse. Mulitali mwake munali mamita 27 ndipo mulifupi munali mamita 13.
30 (Los otros pórticos circundantes medían veinticinco codos de largo y cinco de profundidad).
(Khonde lililonse la makonde atatu a zipata zolowera bwalo lamʼkati aja linali la mamita ozungulira mʼbwalo lamʼkati anali mamita 13 mulitali mwake, mamita awiri ndi theka mulifupi mwake).
31 El pórtico daba al patio exterior y sus pilares estaban decorados con dibujos de palmeras. Tenía ocho escalones para llegar a él.
Khonde lake linayangʼanana ndi bwalo lakunja. Pa mphuthu pake anajambulapo zithunzi za kanjedza mbali zonse ziwiri, ndipo linali ndi makwerero asanu ndi atatu.
32 Me llevó al patio interior, en el lado este. Midió la puerta y medía lo mismo que las anteriores.
Kenaka munthuyo anapita nane ku bwalo la mʼkati mbali ya kummawa, ndipo anayeza chipata cholowera; chinali chofanana ndi zinzake zina zija.
33 Los nichos, los postes y el pórtico medían lo mismo que los anteriores. La puerta y el pórtico tenían ventanas alrededor. Tenía cincuenta codos de largo y veinticinco de ancho.
Zipinda zake za alonda, makoma ake ndi khonde lake zinali zofanana ndi zina zija. Chipata cholowera ndi khonde lake chinali ndi mipata mʼmbali zonse. Mulitali mwake munali mamita 27 ndipo mulifupi mwake munali mamita 13.
34 El pórtico daba al patio exterior y sus postes estaban decorados con dibujos de palmeras. Tenía ocho escalones para llegar a ella.
Khonde lake linayangʼanana ndi bwalo lakunja. Pa mphuthu pake anajambulapo zithunzi za kanjedza mbali zonse ziwiri, ndipo linali ndi makwerero asanu ndi atatu.
35 Me llevó a la puerta norte y la midió. Medía lo mismo que las anteriores,
Kenaka anapita nane ku chipata chakumpoto ndipo anachiyeza. Chinali chofanana ndi zina zija.
36 incluyendo sus alcobas, postes y pórtico. La puerta y su pórtico tenían ventanas alrededor. Tenía cincuenta codos de largo y veinticinco de ancho.
Zipinda zake za alonda, makoma ake ndiponso khonde lake zinali zofanana ndi zina zija, ndipo chinalinso ndi mipata mbali zonse ziwiri. Mulitali mwake munali mamita 27 ndipo mulifupi mwake munali mamita 13.
37 El pórtico daba al patio exterior y sus postes estaban decorados con palmeras por todos lados. Tenía ocho escalones para subir.
Khonde lake limayangʼanana ndi bwalo lakunja. Pa mphuthu zake anajambulapo zithunzi za kanjedza mbali zonse ziwiri, ndipo linali ndi makwerero asanu ndi atatu.
38 Junto al pórtico de las puertas interiores había una sala con una puerta. Allí se lavaba el holocausto.
Panali chipinda ndipo khomo lake linali pafupi ndi khonde la chipata cholowera chamʼkati. Mʼchipinda mʼmenemo ankatsukira nyama ya nsembe yopsereza.
39 Dentro del pórtico de la puerta había dos mesas a ambos lados, donde se sacrificaban los animales para los holocaustos, las ofrendas por el pecado y las ofrendas por la culpa.
Pa khonde la chipatacho panali matebulo awiri, lina kuno lina uko. Ankapherapo nsembe zopsereza, nsembe zopepesera machimo ndi nsembe zopepesera kupalamula.
40 Afuera, en el camino hacia la entrada de la puerta norte, había dos mesas a un lado del pórtico de la puerta y dos mesas al otro lado.
Panali matebulo anayi, awiri a iwo anali kunja kwa khoma la khonde pafupi ndi makwerero olowera pa chipata chakumpoto ndi awiri enawo anali mbali inayo ya makwerero.
41 Así que había cuatro mesas en el interior de la puerta y otras cuatro en el exterior, haciendo un total de ocho mesas. Aquí se sacrificaban los sacrificios.
Choncho ku mbali imodzi ya chipata kunali matebulo anayi, ndiponso ku mbali inayo kunali matebulo anayi. Onse pamodzi anali matebulo asanu ndi atatu. Pa matebulopo ankapherapo nyama za nsembe zopsereza.
42 También había cuatro mesas de piedra tallada para el holocausto. Cada una medía un codo y medio de largo, un codo y medio de ancho y un codo de alto. Sobre estas mesas se colocaban los utensilios para sacrificar los holocaustos y los demás sacrificios.
Matebulo anayiwa anali a miyala yosema. Lililonse mulitali mwake linali la masentimita 75, mulifupi mwake linali la masentimita 75, ndipo msinkhu wake unali wa masentimita makumi asanu. Pa matebulopo amayikapo zipangizo zophera nsembe zopsereza ndi nsembe zina.
43 En las paredes del interior de la sala se colocaban ganchos del ancho de una mano. Sobre estas mesas se colocaba la carne de la ofrenda.
Choncho pa matebulopo ankayikapo nyama za nsembe zopsereza. Mbedza zitatu zazitali ngati chikhatho amazikoleka pa makoma pozungulira ponse.
44 Fuera de la puerta interior, pero dentro del patio interior, había dos habitaciones. Una estaba junto a la puerta norte y daba al sur; la otra, junto a la puerta sur, daba al norte.
Munthu uja anapita nane mʼkati mwa bwalo ndipo ndinaona zipinda ziwiri. Chimodzi chinali pafupi ndi chipata chakumpoto kuyangʼana kummwera ndi china chinali pafupi ndi chipata chakummwera kuyangʼana kumpoto.
45 El hombre me dijo: “La sala que da al sur es para los sacerdotes encargados del Templo,
Munthuyo anandiwuza kuti, “Chipinda chimene chikuyangʼana kummwera ndi cha ansembe amene amayangʼanira Nyumba ya Mulungu,
46 y la sala que da al norte es para los sacerdotes encargados del altar. Estos sacerdotes son los descendientes de Sadoc y son los únicos levitas a los que se les permite acercarse al Señor y ministrar ante él”.
ndipo chipinda chimene chikuyangʼana kumpoto ndi cha ansembe amene amayangʼanira guwa lansembe. Amenewa ndiwo ana a Zadoki, ndipo ndi okhawo mwa zidzukulu za Levi amene ayenera kutumikira pamaso pa Yehova mʼNyumba ya Mulungu.”
47 Midió el patio cuadrado: cien codos de largo y cien de ancho. El altar estaba en el patio, frente al Templo.
Kenaka munthuyo anayeza bwalo; linali lofanana mbali zonse kutalika kwake, mulitali mwake munali mamita 53, ndipo mulifupi mwake munali mamita 53. Ndipo guwa lansembe linali kutsogolo kwa Nyumba ya Mulungu.
48 Me llevó al pórtico del Templo y midió los pilares del pórtico de cinco codos a cada lado. La puerta tenía catorce codos de ancho y sus lados medían tres codos.
Munthuyo anapita nane pa khonde la Nyumba ya Mulunguyo. Anayeza mphuthu za khondelo ndipo zinali mamita awiri ndi theka mbali zonse. Mulifupi mwa chipatacho munali mamita asanu ndi awiri ndipo mulifupi mwa makoma ake munali mamita awiri mbali zonse.
49 El pórtico medía veinte codos de ancho y doce de profundidad, y tenía diez escalones para subir. Había columnas junto a los postes, una a cada lado.
Mulitali mwa khonde munali mamita khumi, mulifupi mwake munali mamita asanu ndi limodzi kuchokera kutsogolo mpaka kumbuyo. Panali makwerero khumi, ndipo mbali zonse kunali nsanamira.

< Ezequiel 40 >