< Eclesiastés 7 >
1 Una buena reputación es mejor que un perfume costoso, y el día de tu muerte es mejor que el día de tu nacimiento.
Mbiri yabwino ndi yopambana mafuta onunkhira bwino, ndipo tsiku lomwalira ndi lopambana tsiku lobadwa.
2 Es mejor ir a un funeral que a una fiesta. Al final, todo el mundo muere, y los que aún están vivos deberían pensar en ello.
Kuli bwino kupita ku nyumba yamaliro kusiyana ndi kupita ku nyumba yamadyerero: Pakuti imfa ndiye mathero a munthu aliyense; anthu amoyo azichisunga chimenechi mʼmitima mwawo.
3 La pena es mejor que la risa, porque la tragedia nos ayuda a pensar.
Chisoni nʼchabwino kusiyana ndi kuseka, pakuti nkhope yakugwa ndi yabwino chifukwa imakonza mtima.
4 Los sabios piensan en el impacto de la muerte, mientras que los necios sólo piensan en divertirse.
Mtima wa munthu wanzeru nthawi zonse umalingalira za imfa, koma mitima ya zitsiru imalingalira za chisangalalo.
5 Es mejor escuchar la crítica de un sabio que la canción de los necios.
Kuli bwino kumva kudzudzula kwa munthu wanzeru kusiyana ndi kumvera mayamiko a zitsiru.
6 La risa de los necios es como el crujir de las ramas de espino que se queman debajo de una olla: sin sentido y que se extinguen rápidamente.
Kuseka kwa zitsiru kuli ngati kuthetheka kwa moto kunsi kwa mʼphika, izinso ndi zopandapake.
7 Extorsionar a los demás convierte a los sabios en insensatos, y aceptar sobornos corrompe la mente.
Kuzunza ena kumasandutsa munthu wanzeru kukhala chitsiru, ndipo chiphuphu chimawononga mtima.
8 Terminar algo es mejor que empezarlo. Ser paciente es mejor que ser orgulloso.
Mathero ake a chinthu ndi abwino kupambana chiyambi chake, ndipo kufatsa nʼkwabwino kupambana kudzikuza.
9 No te apresures a enojarte, porque la ira controla la mente de los insensatos.
Usamafulumire kukwiya mu mtima mwako, pakuti mkwiyo ndi bwenzi la zitsiru.
10 No preguntes: “¿Por qué los viejos tiempos eran mejores que ahora?”. Preguntar eso demuestra que no eres sabio.
Usamafunse kuti, “Nʼchifukwa chiyani masiku amakedzana anali abwino kupambana masiku ano?” pakuti si chinthu chanzeru kufunsa mafunso oterewa.
11 La sabiduría es buena, es como recibir una herencia. Beneficia a todos en la vida.
Nzeru ngati cholowa, ndi chinthu chabwino ndipo imapindulitsa wamoyo aliyense pansi pano.
12 Porque la sabiduría trae seguridad, al igual que el dinero, pero la ventaja para los que tienen sabiduría es que se mantienen sanos y salvos.
Nzeru ndi chitetezo, monganso ndalama zili chitetezo, koma phindu la chidziwitso ndi ili: kuti nzeru zimasunga moyo wa munthu amene ali nazo nzeruzo.
13 Piensa en lo que hace Dios. Si él hace que algo se doble, ¡no podrás enderezarlo!
Taganizirani zimene Mulungu wazichita: ndani angathe kuwongola chinthu chimene Iye anachipanga chokhota?
14 En un buen día, alégrate. Cuando llegue un día malo, párate a pensar. Dios hizo cada día, de modo que no sabes lo que te sucederá después.
Pamene zinthu zili bwino, sangalala; koma pamene zinthu sizili bwino, ganizira bwino: Mulungu ndiye anapanga nthawi yabwinoyo, ndiponso nthawi imene si yabwinoyo. Choncho munthu sangathe kuzindikira chilichonse cha mʼtsogolo mwake.
15 A lo largo de mi vida he visto muchas cosas que son difíciles de entender. Gente buena que muere joven a pesar de hacer lo correcto, y a la gente malvada que vive una larga vida de maldad.
Pa moyo wanga wopanda phinduwu ndaona zinthu ziwiri izi: munthu wolungama akuwonongeka mʼchilungamo chake, ndipo munthu woyipa akukhala moyo wautali mʼzoyipa zake.
16 No pienses que puedes hacer lo correcto con mucha observancia religiosa, y no pretendas ser tan sabio. ¿Quieres destruirte a ti mismo?
Usakhale wolungama kwambiri kapena wanzeru kwambiri, udziwonongerenji wekha?
17 Por otro lado, no te decidas a vivir una vida malvada, ¡no seas insensato! ¿Por qué morir antes de tiempo?
Usakhale woyipa kwambiri, ndipo usakhale chitsiru, uferenji nthawi yako isanakwane?
18 Debes tener en cuenta estas advertencias. Los que siguen a Dios estarán seguros de evitar ambas cosas.
Nʼkwabwino kuti utsate njira imodzi, ndipo usataye njira inayo. Munthu amene amaopa Mulungu adzapewa zinthu ziwiri zonsezi.
19 La sabiduría da a una persona sabia más poder que diez consejeros de la ciudad.
Nzeru zimapereka mphamvu zambiri kwa munthu wanzeru kupambana olamulira khumi a mu mzinda.
20 No hay una sola persona buena en todo el mundo que haga siempre lo correcto y no peque nunca.
Palibe munthu wolungama pa dziko lapansi amene amachita zabwino zokhazokha ndipo sachimwa.
21 No te tomes a pecho todo lo que dice la gente, pues de lo contrario podrías oír a tu siervo hablar mal de ti,
Usamamvetsere mawu onse amene anthu amayankhula, mwina udzamva wantchito wako akukutukwana,
22 ¡pues sabes cuántas veces tú mismo has hablado mal de los demás!
pakuti iwe ukudziwa mu mtima mwako kuti nthawi zambiri iwenso unatukwanapo ena.
23 He examinado todo esto usando los principios de la sabiduría. Me dije: “Pensaré con sabiduría”. Pero la sabiduría se me escapó.
Zonsezi ndinaziyesa ndi nzeru zanga ndipo ndinati, “Ine ndatsimikiza mu mtima mwanga kuti ndikhale wanzeru,” koma nzeruyo inanditalikira.
24 Todo lo que existe está fuera de nuestro alcance, es demasiado profundo para nuestro entendimiento. ¿Quién puede comprenderlo?
Nzeru zimene zilipo, zili kutali ndipo ndi zozama kwambiri, ndani angathe kuzidziwa?
25 Dirigí mis pensamientos a descubrir, investigar y averiguar más sobre la sabiduría y lo que tiene sentido. Quería saber más sobre lo estúpido que es el mal y lo ridículo que es ser un insensato.
Kotero ndinayikapo mtima wanga kuti ndidziwe, ndifufuze ndi kumafunafuna nzeru ndi mmene zinthu zimakhalira ndipo ndinafunanso kudziwa kuyipa kwa uchitsiru ndiponso kupusa kwake kwa misala.
26 Descubrí algo más horrible que la muerte: una tontería como la mujer que trata de atraparte, que quiere usar su mente y sus manos para capturarte y atarte. Los que siguen a Dios no serán atrapados, pero los pecadores caerán en su trampa.
Ndinapeza kanthu kowawa kupambana imfa, mkazi amene ali ngati khoka, amene mtima wake uli ngati khwekhwe, ndipo manja ake ali ngati maunyolo. Munthu amene amakondweretsa Mulungu adzathawa mkaziyo, koma mkaziyo adzakola munthu wochimwa.
27 Esto es lo que descubrí después de sumar dos y dos juntos para intentar averiguar qué significaba todo aquello, dice el Maestro.
Mlaliki akunena kuti, “Taonani, chimene ndinachipeza ndi ichi: “Kuwonjezera chinthu china pa china kuti ndidziwe mmene zinthu zimachitikira,
28 Aunque realmente busqué, no encontré lo que buscaba. La gente dice: “Encontré un hombre entre mil, pero ni una sola mujer”.
pamene ine ndinali kufufuzabe koma osapeza kanthu, ndinapeza munthu mmodzi wolungama pakati pa anthu 1,000, koma pakati pawo panalibepo mkazi mmodzi wolungama.
29 Pero descubrí esto: Dios hizo al ser humano para hacer lo que es correcto, pero ellos han seguido sus propias ideas.
Chokhacho chimene ndinachipeza ndi ichi: Mulungu analenga munthu, anamupatsa mtima wolungama, koma anthu anatsatira njira zawozawo zambirimbiri.”