< 2 Samuel 8 >

1 Poco después de esto, David atacó y subyugó a los filisteos, quitándoles Metheg-ammah.
Patapita nthawi, Davide anagonjetsa Afilisti ndi kuwapambana ndipo analanda Metegi Ama kuchoka mʼmanja mwa Afilistiwo.
2 David también derrotó a los moabitas. Los hizo tumbarse en el suelo y los midió con un tramo de cuerda. Midió dos tramos para los que debían morir, y un tramo de cuerda para los que debían vivir. Entonces los sometió bajo su gobierno, y les exigió que pagaran impuestos.
Davide anagonjetsanso Amowabu. Iye anawalamula kuti agone pansi mʼmizere itatu pa gulu lililonse ndipo anawayeza ndi chingwe. Pa gulu lililonse ankapha anthu amene anali pa mizere iwiri yoyamba, kusiyapo mzere wachitatu. Kotero Amowabu anakhala pansi pa ulamuliro wa Davide ndipo ankapereka msonkho.
3 David también derrotó a Hadad-ezer, hijo de Rehob, rey de Soba, cuando intentaba imponer su control a lo largo del río Éufrates.
Komanso Davide anagonjetsa Hadadezeri mwana wa Rehobu, mfumu ya Zoba, pamene anapita kukakhazikitsa ulamuliro wake mʼmbali mwa mtsinje wa Yufurate.
4 David capturó 1.000 de sus carros, 7.000 jinetes y 20.000 soldados de a pie. Ató por las patas a todos los caballos que llevaban carros, pero dejó suficientes caballos para 100 carros de guerra.
Davide analanda magaleta 1,000, anthu 7,000 okwera magaleta pamodzi ndi asilikali oyenda pansi 20,000. Iye anadula mitsempha ya akavalo onse okoka magaleta, koma anasiyapo akavalo 100 okha.
5 Cuando los arameos de Damasco vinieron a ayudar al rey Hadad-ezer de Soba, David mató a veintidós mil de ellos.
Aramu wa ku Damasiko atabwera kudzathandiza Hadadezeri mfumu ya Zoba, Davide anakantha asilikali 22,000.
6 Colocó guarniciones en el reino arameo con capital en Damasco, e hizo que los arameos se sometieran a él y les exigió el pago de impuestos. El Señor le daba victorias a David por donde quiera que iba.
Iye anakhazikitsa maboma mu ufumu wa Aramu wa ku Damasiko, ndipo Aaramu anakhala pansi pa ulamuliro wake ndipo ankapereka msonkho. Yehova ankamupatsa chipambano Davide kulikonse kumene ankapita.
7 David tomó los escudos de oro que le pertenecían a los oficiales de Hadad-ezer y los llevó a Jerusalén.
Davide anatenga zishango zagolide za akuluakulu ankhondo a Hadadezeri ndi kubwera nazo ku Yerusalemu.
8 El rey David también tomó una gran cantidad de bronce de Beta y Berotai, ciudades que habían pertenecido a Hadad-ezer.
Mfumu Davide inatenga mkuwa wambiri kuchokera ku Beta ndi Berotai, mizinda ya Hadadezeri.
9 Cuando Toi, rey de Hamat, se enteró de que David había destruido todo el ejército de Hadadzer, rey de Soba,
Tou, mfumu ya Hamati atamva kuti Davide wagonjetsa gulu lonse lankhondo la Hadadezeri,
10 envió a su hijo Joram a David para que se hiciera amigo de él y lo felicitara por su victoria en la batalla contra Hadad-ezer. Toi y Hadadezer habían estado en guerra con frecuencia. Joram trajo toda clase de regalos de oro, plata y bronce.
anatumiza mwana wake Yoramu kwa mfumu Davide kukamulonjera ndi kukamuyamikira chifukwa cha kupambana kwake pa nkhondo yake ndi Hadadezeriyo, amene analinso pa nkhondo ndi Tou. Yoramu anabweretsa ziwiya zasiliva, zagolide ndi zamkuwa.
11 El rey David le dedicó estos regalos al Señor, junto con la plata y el oro que había tomado de todas las naciones que había sometido:
Mfumu Davide inapereka zinthu zimenezi kwa Yehova, monga anachitira ndi siliva ndi golide zochokera ku mayiko onse amene anawagonjetsa:
12 Edom, Moab, los amonitas, los filisteos y los amalecitas; así como el botín tomado a Hadad-ezer, hijo de Rehob, rey de Soba.
Edomu ndi Mowabu, Aamoni ndi Afilisti, ndi Aamaleki. Iye anaperekanso zolanda ku nkhondo zochokera kwa Hadadezeri mwana wa Rehobu, mfumu ya Zoba.
13 David también se dio a conocer cuando regresó tras derrotar a dieciocho mil edomitas en el Valle de la Sal.
Ndipo Davide anatchuka atabwera kokakantha Aedomu 18,000 mu Chigwa cha Mchere.
14 Colocó guarniciones por todo Edom, y todos los edomitas se sometieron a David. El Señor le dio a David victorias dondequiera que fuera.
Iye anayika maboma mʼdera lonse la Edomu, ndipo Aedomu onse anakhala pansi pa Davide. Yehova ankapambanitsa Davide kulikonse kumene ankapita.
15 David gobernó sobre todo Israel. Hizo lo que era justo y correcto para todo su pueblo.
Davide analamulira dziko lonse la Israeli ndipo ankachita zonse mwachilungamo ndi molondola pamaso pa anthu ake onse.
16 Joab, hijo de Sarvia, era el comandante del ejército, y Josafat, hijo de Ahilud, llevaba los registros oficiales.
Yowabu mwana wa Zeruya anali mkulu wa ankhondo; Yehosafati mwana wa Ahiludi anali mlembi wa zochitika.
17 Sadoc, hijo de Ahitob, y Ahimelec, hijo de Abiatar, eran sacerdotes, mientras que Seraías era el secretario.
Zadoki mwana wa Ahitubi ndi Ahimeleki mwana wa Abiatara anali ansembe; Seraya anali mlembi;
18 Benaía, hijo de Joiada, estaba a cargo de los queretanos y peletanos; y los hijos de David eran sacerdotes.
Benaya mwana wa Yehoyada anali mtsogoleri wa Akereti ndi Apeleti; ndipo ana a Davide anali ansembe.

< 2 Samuel 8 >