< 2 Crónicas 22 >

1 El pueblo de Jerusalén nombró a Ocozías, el hijo menor de Joram, rey en sucesión de su padre, ya que los invasores que habían entrado en el campamento con los árabes habían matado a todos los hijos mayores. Así que Ocozías, hijo de Joram, se convirtió en rey de Judá.
Anthu a mu Yerusalemu anayika Ahaziya mwana wamngʼono kwambiri wa Yehoramu kukhala mfumu mʼmalo mwake, popeza gulu lankhondo limene linabwera ndi Aarabu ku misasa, linapha ana onse aakulu. Motero Ahaziya mwana wa Yehoramu mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
2 Ocozías tenía veintidós años cuando llegó a ser rey, y reinó en Jerusalén durante un año. Su madre se llamaba Atalía, nieta de Omri.
Ahaziya anali wa zaka 22 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu chaka chimodzi. Dzina la amayi ake linali Ataliya, chidzukulu cha Omuri.
3 Ocozías también siguió los malos caminos de la familia de Acab, pues su madre lo animaba a hacer cosas malas.
Nayenso anayenda mʼnjira ya banja la Ahabu, pakuti amayi ake anamulimbikitsa kuchita zolakwika.
4 Hizo lo que era malo a los ojos del Señor, tal como lo había hecho la familia de Acab. Pues después de la muerte de su padre ellos fueron sus consejeros, para su ruina.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga momwe banja la Ahabu linachitira, pakuti atamwalira abambo ake, iwo anakhala alangizi ake, kumene kunali kudziwononga kwake.
5 También siguió su consejo al unirse a Joram, hijo de Acab, rey de Israel, para atacar a Hazael, rey de Harán, en Ramot de Galaad. Los arameos hirieron a Joram,
Iyeyo anatsatiranso uphungu wawo pamene anapita ndi Yehoramu, mwana wa Ahabu, mfumu ya Israeli kukachita nkhondo ndi Hazaeli mfumu ya Aramu ku Ramoti Giliyadi. Aaramu anavulaza Yehoramu,
6 y éste regresó a Jezreel para recuperarse de las heridas que había recibido en Ramá luchando contra Hazael, rey de Harán. Ocozías, hijo de Joram, rey de Judá, fue a Jezreel a visitar a Joram, hijo de Acab, porque éste estaba herido.
kotero iye anabwerera ku Yezireeli kuti akachire mabala amene anamuvulaza ku Ramoti pa nkhondo ndi Hazaeli mfumu ya Aaramu. Ndipo Ahaziya, mwana wa Yehoramu mfumu ya Yuda anapita ku Yezireeli kukaona Yehoramu mwana wa Ahabu chifukwa anavulazidwa.
7 La caída de Azarías vino de Dios cuando fue a ver a Joram. Cuando Azarías llegó allí, fue con Joram a encontrarse con Jehú, hijo de Nimri. El Señor había ungido a Jehú para que destruyera a Acab y a su familia.
Mulungu anakonza kuti Ahaziya akaphedwe pa ulendo wake wokacheza. Ahaziya atafika, iye ndi Yoramu anapita kukakumana ndi Yehu mwana wa Nimisi, amene Yehova anamudzoza kuti akawononge banja la Ahabu.
8 Mientras Jehú llevaba a cabo el juicio sobre la familia de Acab, se encontró con los líderes de Judá y los parientes de Azarías que ayudaban a Ocozías, y los mató.
Pamene Yehu ankalanga banja la Ahabu anapeza atsogoleri a ku Yuda ndiponso ana aamuna a abale ake a Ahaziya amene amatumikira Ahaziya, ndipo anawapha.
9 Entonces Jehú fue en busca de Ocozías. Sus hombres lo encontraron en Samaria y lo capturaron, y lo llevaron a Jehú, donde lo mataron. Lo enterraron, pues dijeron: “Es el nieto de Josafat, que se comprometió completamente a seguir al Señor”. No quedó nadie de la familia de Ocozías para gobernar el reino.
Kenaka anapita kukafunafuna Ahaziya, ndipo anthu ake anagwira Ahaziya pamene amabisala mu Samariya. Anabwera naye kwa Yehu ndipo anaphedwa. Iwo anamuyika mʼmanda, pakuti anati, “Iyeyu anali mwana wa Yehosafati amene anafunafuna Yehova ndi mtima wake wonse.” Kotero panalibe wamphamvu mʼbanja la Ahaziya kuti nʼkukhala mfumu.
10 Cuando la madre de Ocozías se enteró de que su hijo había muerto, procedió a matar a todos los que quedaban de la familia real de Judá.
Ataliya, amayi ake a Ahaziya, ataona kuti mwana wawo wafa, ananyamuka nakapha onse a banja laufumu la Yuda.
11 Pero Josabet, hija del rey Joram, agarró a Joás, hijo de Ocozías, y lo apartó de los hijos del rey que estaban a punto de ser asesinados, y lo colocó a él y a su nodriza en un dormitorio. Como Josabet, hija del rey Joram y esposa del sacerdote Joiada, era hermana de Ocozías, escondió a Joás de Atalía para que no pudiera matarlo.
Koma Yehoseba, mwana wamkazi wa mfumu Yehoramu, anatenga Yowasi mwana wa Ahaziya, momuba ndi kumuchotsa pakati pa ana aamuna a mfumu amene amati aphedwe ndipo anamuyika iye ndi mlezi wake mʼchipinda chogona. Motero Yehoseba, mwana wamkazi wa mfumu Yehoramu, mkazi wa wansembe Yehoyada, yemwe anali mlongo wake wa Ahaziya anamubisa mwanayo kuti Ataliya asamuphe.
12 Y mantuvieron a Joás escondido con ellos en el Templo de Dios durante seis años, mientras Atalía gobernaba el país.
Mwanayo anakhala mobisala pamodzi ndi iwo mu Nyumba ya Mulungu kwa zaka zisanu ndi chimodzi muulamuliro wa Ataliya.

< 2 Crónicas 22 >