< 1 Timoteo 2 >

1 En primer lugar quiero animarte a orar por todos: haz peticiones y agradece en nombre de ellos.
Tsono choyamba ndikukupemphani kuti mupempherere anthu onse. Mapemphero anu akhale opemba, opempha, opempherera ena ndi oyamika.
2 De este mismo modo ora por los reyes y por todo tipo de líderes, para que podamos tener una vida tranquila y pacífica, siempre pensando en Dios y tomando la vida con seriedad.
Mupempherere mafumu ndi onse aulamuliro, kuti tikhale moyo wamtendere ndi bata, woopa Mulungu ndi oyera mtima.
3 Esto es bueno, y es lo que agrada a Dios, nuestro Salvador.
Izi ndi zabwino ndipo zimakondweretsa Mulungu Mpulumutsi wathu,
4 Porque él desea que todos seamos salvos y comprendamos la verdad.
amene amafuna kuti anthu onse apulumutsidwe ndipo kuti adziwe choonadi.
5 Pues hay un Dios, y un mediador entre Dios y la humanidad, el hombre Cristo Jesús.
Pakuti pali Mulungu mmodzi yekha ndi Mʼkhalapakati mmodzi yekha pakati pa Mulungu ndi anthu, munthu uja Khristu Yesu.
6 Él se entregó a fin de que todos pudiéramos ser rescatados nuevamente, demostrando la evidencia a su debido tiempo.
Iyeyu anadzipereka kukhala dipo lowombolera anthu onse. Umenewu ndi umboni umene waperekedwa mu nthawi yake yoyenera.
7 Fui designado para compartir este mensaje y ser su mensajero, ser un maestro para los extranjeros sobre la fe en Dios y la verdad (no miento, digo la verdad).
Nʼchifukwa chake anandisankha kukhala mlaliki ndiponso mtumwi wophunzitsa anthu a mitundu ina mawu achikhulupiriro choona. Sindikunama ayi, ndikunena zoona.
8 Lo que realmente quiero es que los hombres en todas partes oren a Dios con sinceridad. ¡Sin enojos ni discusiones!
Choncho ndikufuna kuti paliponse popemphera, amuna azikweza manja awo kwa Mulungu mopanda mkwiyo kapena kukangana.
9 Del mismo modo, las mujeres deben vestir con prudencia, con modestia y apropiadamente. Deben ser atractivas pero no por su corte de cabello o por el uso de oro, perlas o ropas costosas,
Ndikufunanso kuti amayi azivala mwaulemu, modzilemekeza ndi moyenera. Adzikongoletse koma osati ndi tsitsi loluka mowonjeza muyeso kapena zokongoletsa zagolide kapena mikanda yamtengowapatali kapena ndi zovala zamtengowapatali.
10 sino por las cosas buenas que hacen, como es apropiado en las mujeres que dicen seguir a Dios.
Koma adzikongoletse ndi ntchito zabwino zoyenera mayi wopembedza Mulungu.
11 Las mujeres deben aprender en silencio, respetando su lugar.
Amayi azikhala chete pophunzitsidwa ndi mtima ogonjera kwathunthu.
12 Yo no permito que las mujeres sean instructoras, o que dominen a los hombres; háganlas permanecer en silencio.
Ine sindikulola kuti amayi aziphunzitsa kapena kulamulira amuna; koma akhale chete.
13 Pues Adán fue creado primero, y luego Eva.
Pakuti Adamu ndiye anayamba kupangidwa kenaka Hava.
14 Adán no fue engañado, pero Eva sí fue engañada por completo, y cayó en pecado.
Ndipo Adamu si amene ananyengedwa koma mkazi ndiye amene ananyengedwa nachimwa.
15 No obstante, las mujeres serán salvadas por convertirse en madres, siempre y cuando sigan con fe y amor, y vivan vidas prudentes en santidad.
Ndipo mkazi adzapulumutsidwa pobereka mwana ngati apitiriza kukhala mʼchikhulupiriro, mʼchikondi ndi mʼkuyera mtima pamodzi ndi kudzichepetsa konse.

< 1 Timoteo 2 >