< 1 Reyes 15 >

1 Abías llegó a ser rey de Judá en el año dieciocho del reinado de Jeroboam, hijo de Nabat.
Mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Yeroboamu mwana wa Nebati, Abiya anakhala mfumu ya Yuda,
2 Reinó en Jerusalén durante tres años. Su madre se llamaba Macá, hija de Abisalón.
ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka zitatu. Amayi ake anali Maaka, mwana wa Abisalomu.
3 Abías cometió todos los pecados que su padre había cometido antes que él. No estaba totalmente dedicado al Señor su Dios como lo había estado su antepasado David.
Abiya anachita zoyipa zonse zimene abambo ake anazichita. Sanali wangwiro pamaso pa Yehova Mulungu wake, monga linachitira kholo lake Davide.
4 Aun así, por amor a David, el Señor su Dios permitió que sus descendientes siguieran gobernando como una lámpara, un hijo que gobernara después de él y que hiciera fuerte a Jerusalén.
Komabe chifukwa cha Davide, Yehova Mulungu wake anamupatsa nyale mu Yerusalemu pomupatsa mwana wolowa mʼmalo mwake ndi kumukhazikitsa kukhala wamphamvu mu Yerusalemu;
5 Porque David había hecho lo que era justo ante los ojos del Señor, y no se había desviado de nada de lo que el Señor había ordenado durante toda su vida, excepto en el caso de Urías el hitita.
pakuti Davide anachita zolungama pamaso pa Yehova ndipo sanalephere kusunga chilichonse chimene Yehova anamulamula masiku onse a moyo wake kupatula nkhani ija ya Uriya Mhiti.
6 (Roboam y Jeroboam siempre estuvieron en guerra entre sí).
Panali nkhondo pakati pa Rehobowamu ndi Yeroboamu masiku onse a moyo wa Abiya.
7 El resto de lo que sucedió en el reinado de Abías y todo lo que hizo está registrado en el Libro de las Crónicas de los Reyes de Judá. Abías y Jeroboam siempre estuvieron en guerra entre sí.
Tsono ntchito zina za Abiya, ndi zina zonse anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda? Panali nkhondo pakati pa Abiya ndi Yeroboamu.
8 Abías murió y fue enterrado en la Ciudad de David. Su hijo Asa lo sucedió como rey.
Ndipo Abiya anamwalira nayikidwa mʼmanda momwe anayikidwa makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Asa, mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
9 Asa llegó a ser rey de Judá en el vigésimo año del reinado de Jeroboam, rey de Israel.
Mʼchaka cha makumi awiri cha Yeroboamu mfumu ya Israeli, Asa anakhala mfumu ya Yuda,
10 Reinó en Jerusalén cuarenta y un años. Su abuela se llamaba Macá, hija de Abisalón.
ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 41. Agogo ake akazi anali Maaka mwana wa Abisalomu.
11 Asá hizo lo justo a los ojos del Señor, como lo había hecho su antepasado David.
Asa anachita zolungama pamaso pa Yehova monga anachitira Davide kholo lake.
12 Expulsó del país a las prostitutas del culto y se deshizo de todos los ídolos que habían fabricado sus antepasados.
Iye anachotsa mʼdzikomo amuna onse ochita zadama pochita chipembedzo chawo ndiponso anachotsa mafano onse amene makolo ake anawapanga.
13 Incluso despidió a su abuela Macá como reina madre, porque había hecho un ídolo repugnante. Asa hizo cortar el ídolo y lo quemó en el valle del Cedrón.
Iye anachotsanso gogo wake Maaka pa udindo wake wa amayi a mfumu, chifukwa choti anapanga fano lonyansa la Asera. Asa anagwetsa fanolo nakalitentha ku Chigwa cha Kidroni.
14 Aunque los altares paganos no fueron removidos, Asá se comprometió completamente con el Señor durante toda su vida.
Ngakhale sanachotse malo opembedzerapo mafano, mtima wa Asa unali wodzipereka kwathunthu kwa Yehova masiku onse a moyo wake.
15 Llevó a la casa del Señor la plata y el oro y los demás objetos que él y su padre habían dedicado.
Asa anabweretsa ku Nyumba ya Yehova zinthu zimene abambo ake anazipereka, ndiponso zinthu zimene iye mwini anazipereka: zagolide, siliva ndi ziwiya zotengera.
16 Asá y Basá, rey de Israel, estaban siempre en guerra entre sí.
Panali nkhondo pakati pa Asa ndi Baasa mfumu ya Israeli nthawi yonse ya ulamuliro wawo.
17 Basá, rey de Israel, atacó a Judá y fortificó Ramá para impedir que la gente viniera o fuera a Asa, rey de Judá.
Baasa mfumu ya Israeli anapita kukathira nkhondo dziko la Yuda, ndipo anamangira linga mzinda wa Rama kuletsa kuti wina aliyense asatuluke kapena kulowa mʼdziko la Asa, mfumu ya Yuda.
18 Entonces Asa tomó toda la plata y el oro que quedaba en los tesoros del Templo del Señor y del palacio real. Lo entregó a sus siervos y los envió a Ben-hadad, hijo de Tabrimón, hijo de Hezión, rey de Harán, que vivía en Damasco, junto con este mensaje:
Tsono Asa anatenga siliva yense pamodzi ndi golide zimene zinatsala ku malo osungira chuma cha ku Nyumba ya Yehova ndiponso ku nyumba yake yaufumu. Anazipereka kwa atumiki ake, nawatuma kupita nazo kwa Beni-Hadadi mwana wa Tabirimoni, mwana wa Heziyoni, mfumu ya Aramu, amene ankakhala ku Damasiko ndipo anakamuwuza kuti,
19 “Hagamos un tratado entre nosotros, como lo hubo entre mi padre y el tuyo. Mira, te he enviado un regalo de plata y oro. Ve y rompe el tratado con Basá, rey de Israel, para que se retire y me deje en paz”.
“Tiyeni tigwirizane inu ndi ine, monga panali mgwirizano pakati pa abambo anu ndi abambo anga. Onani, ndikukutumizirani mphatso za siliva ndi golide. Tsopano kathetseni mgwirizano wanu ndi Baasa mfumu ya Israeli kuti andisiye.”
20 Ben Adad aceptó la propuesta de Asá y envió a su ejército con sus comandantes a atacar las ciudades de Israel. Capturaron las ciudades de Ijón, Dan, Abel-Bet-macá y todo Quinéret, incluyendo toda la tierra de Neftalí.
Choncho Beni-Hadadi anamvera zimene ananena mfumu Asa ndipo anatumiza olamulira magulu ake ankhondo ku mizinda ya Israeli. Ndipo iye anagonjetsa Iyoni, Dani, Abeli-Beti-Maaka ndi dera lonse la Kinereti kuphatikiza dziko lonse la Nafutali.
21 Cuando Basá se enteró de esto, dejó de fortificar Ramá y se retiró a Tirsa.
Baasa atamva zimenezi, anasiya kumangira linga Rama ndipo anakakhala ku Tiriza.
22 Entonces el rey Asá emitió un anuncio público en toda Judá, sin excepción. El pueblo obedeció y se llevó las piedras y los maderos que Basá había usado para construir Ramá. El rey Asa utilizó estos materiales de construcción para fortalecer Geba de Benjamín, así como Mizpa.
Pamenepo Mfumu Asa analamula anthu onse a ku Yuda osasiya ndi mmodzi yemwe, ndipo anachotsa ku Rama miyala ndi matabwa amene Baasa ankamangira kumeneko. Zipangizo zimenezi Mfumu Asa inamangira linga la Geba ku Benjamini ndi la ku Mizipa.
23 El resto de lo que sucedió en el reinado de Asa, todos sus logros, todo lo que hizo y las ciudades que construyó, están registrados en el Libro de las Crónicas de los Reyes de Judá. Pero cuando envejeció tuvo una enfermedad en los pies.
Tsono ntchito zina za Asa, za mphamvu zake ndi mizinda imene anayimanga ndi zina zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda? Koma pa nthawi ya ukalamba wake anadwala nthenda ya mapazi.
24 Asa murió y fue enterrado con sus antepasados en la Ciudad de David. Su hijo Josafat lo sucedió como rey.
Ndipo Asa anamwalira nayikidwa mʼmanda momwe anayikidwa makolo ake mu mzinda wa Davide kholo lake. Ndipo Yehosafati mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
25 Nadab, hijo de Jeroboam, se convirtió en rey de Israel en el segundo año del reinado de Asá de Judá. Reinó en Israel durante dos años.
Nadabu, mwana wa Yeroboamu anakhala mfumu ya Israeli mʼchaka chachiwiri cha Asa mfumu ya Yuda, ndipo analamulira Israeli zaka ziwiri.
26 Sus hechos fueron malos a los ojos del Señor. Siguió los caminos de su padre y cometió los mismos pecados que su padre había hecho cometer a Israel.
Nadabu anachita zoyipa pamaso pa Yehova, anayenda mʼnjira za abambo ake ndi mu uchimo womwe anachimwitsa nawo Israeli.
27 Basá, hijo de Ahías, de la tribu de Isacar, tramó una rebelión contra él. Basá asesinó a Nadab en la ciudad filistea de Guibetón, mientras Nadab y todo el ejército israelita la asediaban.
Baasa mwana wa Ahiya, wa banja la Isakara anakonzera Nadabuyo chiwembu, ndipo anamukantha ku Gibetoni, mzinda wa Afilisti, pamene Nadabu ndi anthu onse a ku Israeli anali atawuzungulira.
28 Basá mató a Nadab y asumió como rey en el tercer año del reinado del rey Asa de Judá.
Baasa anapha Nadabu mʼchaka chachitatu cha Asa, mfumu ya ku Yuda ndipo analowa ufumu mʼmalo mwake.
29 Tan pronto como llegó a ser rey, mató a todo el resto de la familia de Jeroboam. No dejó con vida a ninguno de los descendientes de Jeroboam: los destruyó a todos, como el Señor había dicho por medio de su siervo Ahías el silonita.
Iye atangoyamba kulamulira, anapha anthu onse a banja la Yeroboamu. Sanasiye ndi mmodzi yemwe wamoyo pa banjapo, koma anawononga anthu onse, molingana ndi mawu a Yehova amene anayankhula mwa mtumiki wake Ahiya wa ku Silo
30 Esto sucedió por los pecados que Jeroboam había cometido y había hecho cometer a Israel, y porque había hecho enojar al Señor, el Dios de Israel.
chifukwa cha machimo amene Yeroboamu anachita, ndiponso kuchimwitsa anthu a ku Israeli, naputa mkwiyo wa Yehova Mulungu wa Israeli.
31 El resto de lo que sucedió en el reinado de Nadab y todo lo que hizo están registrados en el Libro de las Crónicas de los Reyes de Israel.
Tsono ntchito za Nadabu ndi zina zonse zimene anazichita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
32 Asá y Basá, rey de Israel, estaban siempre en guerra entre sí.
Panali nkhondo pakati pa Asa ndi Baasa mfumu ya Israeli pa nthawi yonse ya ulamuliro wawo.
33 Basá, hijo de Ahías, llegó a ser rey de todo Israel en el tercer año del reinado del rey Asá en Judá. Basá reinó en Tirsa durante veinticuatro años.
Chaka chachitatu cha Asa mfumu ya Yuda, Baasa mwana wa Ahiya anakhala mfumu ya Aisraeli onse ku Tiriza, ndipo analamulira zaka 24.
34 Perolos hechos de Basáfueron malosa los ojos del Señor y siguió el camino de Jeroboam y su pecado, que él había hecho cometer a Israel.
Anachita zoyipa pamaso pa Yehova, nayenda mʼnjira za Yeroboamu ndi kuchita tchimo lake limene linachimwitsa anthu a ku Israeli.

< 1 Reyes 15 >