< 1 Crónicas 27 >

1 Esta es una lista de los israelitas, de los jefes de familia, de los comandantes de millares y de los comandantes de centenas, y de sus oficiales que servían al rey en todo lo relacionado con las divisiones que estaban de servicio cada mes durante el año. Había 24.000 hombres en cada división.
Uwu ndi mndandanda wa Aisraeli, atsogoleri a mabanja, olamulira asilikali 1,000, olamulira asilikali 100 ndi akuluakulu awo, amene ankatumikira mfumu mʼzonse zokhudza magulu a ankhondo, amene amagwira ntchito mwezi ndi mwezi chaka chonse. Gulu lililonse linali ndi anthu 24,000.
2 Al mando de la primera división para el primer mes, estaba Jashobeam, hijo de Zabdiel. Tenía 24.000 hombres en su división.
Amene amalamulira gulu loyamba pa mwezi woyamba anali Yasobeamu mwana wa Zabidieli. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
3 Era descendiente de Fares y estaba a cargo de todos los oficiales del ejército durante el primer mes.
Iyeyu anali chidzukulu cha Perezi ndipo anali mkulu wa atsogoleri onse a ankhondo mwezi woyamba.
4 Al mando de la división para el segundo mes estaba Dodai el ahohita. Miclot era su jefe de división. Tenía 24.000 hombres en su división.
Amene amalamulira gulu lachiwiri pa mwezi wachiwiri anali Dodai Mwahohi; Mikiloti ndiye anali mtsogoleri wa gulu lake. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
5 El tercer comandante del ejército para el tercer mes era Benaía, hijo del sacerdote Joiada. Era el jefe y había 24.000 hombres en su división.
Wolamulira ankhondo wachitatu, pa mwezi wachitatu anali Benaya, mwana wa wansembe Yehoyada. Iye anali mtsogoleri ndipo pa gulu lake panali ankhondo 24,000.
6 Este era el mismo Benaía que era un gran guerrero entre los Treinta, y estaba a cargo de los Treinta. Su hijo Amizabad era el jefe de su división.
Uyu ndi Benaya uja amene anali wamphamvu pa gulu la anthu makumi atatu ndipo ndiye amatsogolera anthu makumi atatu aja. Mwana wake Amizabadi ndiye amatsogolera gulu lake.
7 El cuarto, para el cuarto mes, era Asael, hermano de Joab. Su hijo Zebadías fue su sucesor. Tenía 24.000 hombres en su división.
Wachinayi pa mwezi wachinayi anali Asaheli mʼbale wake wa Yowabu; ndipo mwana wake Zebadiya ndiye analowa mʼmalo mwake. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
8 El quinto, para el quinto mes, era el comandante del ejército Shamhuth el Izrahita. Tenía 24.000 hombres en su división.
Wachisanu pa mwezi wachisanu anali Samihuti, mdzukulu wa Izira. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
9 El sexto, para el sexto mes, era Ira, hijo de Iqués de Tecoa. Tenía 24.000 hombres en su división.
Wa 6 pa mwezi wa 6 anali Ira mwana wa Ikesi wa ku Tekowa. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
10 El séptimo, para el séptimo mes, era Heles el pelonita de la tribu de Efraín. Tenía 24.000 hombres en su división.
Wa 7 pa mwezi wa 7 anali Helezi Mpeloni wa fuko la Efereimu. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
11 El octavo, para el octavo mes, era Sibecai de Husa, de la tribu de Zera. Tenía 24.000 hombres en su división.
Wa 8 pa mwezi wa 8 anali Sibekai Mhusati, wa mbumba ya Zera. Pa gulu lake panali asilikali 24,000
12 El noveno, para el noveno mes, era Abiezer, de Anatot, de la tribu de Benjamín. Tenía 24.000 hombres en su división.
Wa 9 pa mwezi wa 9 anali Abiezeri wa banja la Anatoti, wa fuko la Benjamini. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
13 El décimo, para el décimo mes, era Maharai de Netofa, de la tribu de Zera. Tenía 24.000 hombres en su división.
Wa khumi pa mwezi wa khumi anali Mahazayi wa ku Netofa, wa mbumba ya Zera. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
14 El undécimo, para el undécimo mes, era Benaía, de Piratón, de la tribu de Efraín. Tenía 24.000 hombres en su división.
Mtsogoleri wa 11, pa mwezi wa 11 anali Benaya wa ku Piratoni, wa fuko la Efereimu. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
15 El duodécimo, para el duodécimo mes, era Heldai de Netofa, de la familia de Otoniel. Tenía 24.000 hombres en su división.
Mtsogoleri wa 12, pa mwezi wa 12 anali Helidai Mnetofa, wa banja la Otanieli. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
16 Esta es la lista de los jefes para las tribus de Israel: para los rubenitas Eliezer, hijo de Zicri; para los simeonitas: Sefatías, hijo de Maaca;
Akuluakulu amene amatsogolera mafuko a Israeli ndi awa: Mtsogoleri wa fuko la Rubeni: Eliezara mwana wa Zikiri; mtsogoleri wa fuko la Simeoni: Sefatiya mwana wa Maaka;
17 para Leví: Hasabías, hijo de Quemuel; para Aarón: Sadoc;
mtsogoleri wa fuko la Levi: Hasabiya mwana wa Kemueli, mtsogoleri wa banja la Aaroni: Zadoki;
18 para Judá: Eliú, hermano de David; por Isacar Omri, hijo de Miguel;
mtsogoleri wa fuko la Yuda: Elihu, mʼbale wake wa Davide; mtsogoleri wa fuko la Isakara: Omuri mwana wa Mikayeli;
19 para Zabulón Ismaías, hijo de Abdías; por Neftalí: Jerimot, hijo de Azriel;
mtsogoleri wa fuko la Zebuloni: Isimaiya mwana wa Obadiya; mtsogoleri wa fuko la Nafutali: Yerimoti mwana wa Azirieli;
20 por los efraimitas: Oseas, hijo de Azazías; por la media tribu de Manasés Joel, hijo de Pedaías;
mtsogoleri wa fuko la Efereimu: Hoseya mwana wa Azaziya; mtsogoleri wa fuko la theka la Manase: Yoweli mwana wa Pedaya;
21 para la media tribu de Manasés en Galaad Iddo, hijo de Zacarías; por Benjamín: Jaasiel, hijo de Abner;
mtsogoleri wa fuko la theka la Manase limene linali ku Giliyadi: Ido mwana wa Zekariya; mtsogoleri wa fuko la Benjamini: Yaasieli mwana wa Abineri;
22 por Dan: Azarel, hijo de Jeroham. Estos fueron los oficiales para las tribus de Israel.
mtsogoleri wa fuko la Dani: Azareli mwana wa Yerohamu. Awa anali akuluakulu a mafuko a Israeli.
23 David no censó a los hombres menores de veinte años porque el Señor había dicho que haría a Israel tan numeroso como las estrellas del cielo.
Davide sanawerenge amuna amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kucheperapo, chifukwa Yehova analonjeza kuti adzachulukitsa Aisraeli ngati nyenyezi zamumlengalenga.
24 Joab, hijo de Sarvia, había comenzado el censo, pero no lo terminó. Israel fue castigado a causa de este censo, y los resultados no fueron registrados en la cuenta oficial del rey David.
Yowabu mwana wa Zeruya anayamba kuwerenga amuna koma sanamalize. Mkwiyo unagwera Aisraeli chifukwa cha zimenezi ndipo chiwerengerochi sanachilowetse mʼbuku la mbiri ya mfumu Davide.
25 Azmavet, hijo de Adiel, estaba a cargo de los almacenes del rey, mientras que Jonatán, hijo de Uzías, estaba a cargo de los del campo, las ciudades, las aldeas y las torres de vigilancia.
Azimaveti mwana wa Adieli ankayangʼanira nyumba zosungiramo katundu wa mfumu. Yonatani mwana wa Uziya ankayangʼanira nyumba zosungiramo katundu wa maboma ozungulira, mizinda, midzi ndi malo olondera.
26 Ezri, hijo de Quelub, estaba a cargo de los campesinos que trabajaban la tierra.
Eziri mwana wa Kelubi ankayangʼanira anthu ogwira ntchito yolima ku munda.
27 Simei, el ramatita, estaba a cargo de las viñas. Zabdi el sifmita estaba a cargo del producto de las viñas para las bodegas.
Simei wa ku Rama ankayangʼanira minda ya mpesa. Zabidi wa ku Sifamu ankayangʼanira mphesa ndi mosungiramo mwake.
28 Baal-Hanán el gederita estaba a cargo de los olivos y los sicómoros de las colinas. Joás estaba a cargo de los almacenes de aceite de oliva.
Baala-Hanani wa ku Gederi ankayangʼanira mitengo ya olivi ndi ya mikuyu ya ku Sefela. Yowasi ankayangʼanira mafuta a Olivi.
29 Sitrai de Sarón estaba a cargo del ganado en los pastos de Sarón. Safat, hijo de Adlai, estaba a cargo del ganado en los valles.
Sitirayi wa ku Saroni ankayangʼanira ziweto zimene amaweta ku Saroni. Safati mwana wa Adilayi ankayangʼanira ngʼombe zakuzigwa.
30 Obil el ismaelita estaba a cargo de los camellos. Jehedías de Meronot estaba a cargo de los asnos.
Obili Mwismaeli ankayangʼanira ngamira. Yehideya Mmerenoti ankayangʼanira abulu.
31 Jaziz el agareno estaba a cargo de las ovejas y las cabras. Todos estos eran funcionarios a cargo de lo que pertenecía al rey David.
Yazizi Mhagiri akayangʼanira nkhosa ndi mbuzi. Onsewa anali akuluakulu oyangʼanira chuma cha mfumu Davide.
32 Jonatán, tío de David, era un consejero, un hombre perspicaz y un escriba. Jehiel, hijo de Hacmoni, cuidaba de los hijos del rey.
Yonatani, malume wake wa Davide, anali phungu wake ndipo anali munthu wanzeru komanso analinso mlembi. Yehieli mwana wa Hakimoni ankasamalira ana a mfumu.
33 Ahitofel era el consejero del rey y Husai, el arquita, era el amigo del rey.
Ahitofele anali phungu wa mfumu. Husai Mwariki anali bwenzi la mfumu.
34 Después de Ahitofel vino Joiada, hijo de Benaía y de Abiatar. Joab era el comandante del ejército real.
Ahitofele atamwalira mʼmalo mwake munalowa Yehoyada mwana wa Benaya ndi Abiatara. Yowabu anali mtsogoleri wa gulu lankhondo la mfumu.

< 1 Crónicas 27 >