< 1 Crónicas 23 >
1 Cuando David envejeció, habiendo vivido una larga vida, nombró a su hijo Salomón rey de Israel.
Davide atakalamba, ali ndi zaka zambiri, anayika Solomoni mwana wake kukhala mfumu ya Israeli.
2 También convocó a todos los jefes de Israel, a los sacerdotes y a los levitas.
Iye anasonkhanitsanso pamodzi atsogoleri onse a Israeli, pamodzi ndi ansembe ndi Alevi.
3 Se contaron los levitas mayores de treinta años, y fueron 38.000 en total.
Anawerenga Alevi kuyambira a zaka makumi atatu ndi kupitirirapo, ndipo chiwerengero cha amuna onse chinali 38,000.
4 “De ellos, 24.000 estarán a cargo de las obras de la casa del Señor, mientras que 6.000 serán oficiales y jueces”, instruyó David.
Davide anati, “Mwa amenewa, amuna 24,000 aziyangʼanira ntchito za mʼNyumba ya Mulungu ndipo 6,000 akhale akuluakulu ndi oweruza.
5 “Y 4.000 serán porteros, mientras que 4.000 alabarán al Señor usando los instrumentos musicales que he proporcionado para la alabanza”.
Amuna 4,000 akhale alonda a pa zipata ndipo 4,000 azitamanda Yehova ndi zipangizo zoyimbira zimene ndazipereka ndi cholinga chimenecho.”
6 David los dividió en secciones correspondientes a Los hijos de Levi: Gersón, Coat y Merari.
Davide anagawa Aleviwo mʼmagulumagulu motsatira ana a Levi awa: Geresoni, Kohati ndi Merari.
7 Los hijos de Gersón: Ladán y Simei.
Ana a Geresoni: Ladani ndi Simei.
8 Los hijos de Ladan: Jehiel (el jefe de familia), Zetham y Joel, tres en total.
Ana a Ladani: Mtsogoleri Yehieli, Zetamu ndi Yoweli. Onse analipo atatu.
9 Los hijos de Simei: Selomit, Haziel y Harán, tres en total. Estos eran los jefes de las familias de Ladán.
Ana a Simei: Selomoti, Haziyeli ndi Harani. Onse analipo atatu. Awa anali atsogoleri a mabanja a Ladani.
10 Los hijos de Simei: Jahat, Ziza, Jeús y Bería, cuatro en total.
Ndipo ana a Simei anali: Yahati, Zina, Yeusi ndi Beriya. Awa anali ana a Semei. Onse analipo anayi.
11 Jahat (el jefe de familia), y Ziza (el segundo); pero como Jeús y Bería no tuvieron muchos hijos, fueron contados como una sola familia.
Mtsogoleri anali Yahati, ndipo Ziza anali wachiwiri, koma Yeusi ndi Beriya analibe ana aamuna ambiri. Kotero iwo anawerengedwa ngati banja limodzi ndipo anapatsidwa ntchito imodzinso yofanana.
12 Los hijos de Coat: Amram, Izhar, Hebrón y Uziel-un total de cuatro.
Ana a Kohati: Amramu, Izihari, Hebroni ndi Uzieli. Onse analipo anayi.
13 Los hijos de Amram: Aarón y Moisés. Aarón estaba dedicado al servicio con las cosas más sagradas, para que él y sus hijos presentaran siempre ofrendas al Señor, y ministraran ante él, y dieran bendiciones en su nombre para siempre.
Ana a Amramu: Aaroni ndi Mose. Aaroni ndi zidzukulu zake anapatulidwa kwamuyaya kuti azipereka zinthu zopatulika kwambiri monga nsembe pamaso pa Yehova, komanso kuti azitumikira pamaso pake ndi kumadalitsa anthu mʼdzina lake kwamuyaya.
14 En cuanto a Moisés, el hombre de Dios, sus hijos estaban incluidos en la tribu de Leví.
Ana a Mose munthu wa Mulungu anawerengedwa ngati gawo la fuko la Levi.
15 Los hijos de Moisés: Gersón y Eliezer.
Ana a Mose: Geresomu ndi Eliezara.
16 Los hijos de Gersón: Sebuel (el jefe de familia).
Zidzukulu za Geresomu: Mtsogoleri anali Subaeli.
17 Los hijos de Eliezer: Rehabías (el jefe de familia). Eliezer no tuvo más hijos, pero Rehabías tuvo muchos hijos.
Zidzukulu za Eliezara: Mtsogoleri anali Rehabiya. Eliezara analibe ana ena aamuna, koma ana a Rehabiya anali ochuluka kwambiri.
18 Los hijos de Izhar: Selomit (el jefe de familia).
Ana a Izihari: Mtsogoleri anali Selomiti.
19 Los hijos de Hebrón: Jeria (el jefe de familia), Amarías (el segundo), Jahaziel (el tercero) y Jecamán (el cuarto).
Ana a Hebroni: Mtsogoleri anali Yeriya, wachiwiri anali Amariya, Yahazieli anali wachitatu ndipo Yekameamu anali wachinayi.
20 Los hijos de Uziel: Micaías (el jefe de familia) e Isías (el segundo).
Ana a Uzieli: Mtsogoleri anali Mika ndipo wachiwiri anali Isiya.
21 Los hijos de Merari: Mahli y Musi. Los hijos de Mahli: Eleazar y Cis.
Ana a Merari: Mahili ndi Musi. Ana a Mahili: Eliezara ndi Kisi.
22 Eleazar murió sin tener hijos, sólo hijas. Sus primos, Los hijos de Cis, se casaron con ellas.
Eliezara anamwalira wopanda ana aamuna. Iye anali ndi ana aakazi okhaokha. Abale awo, ana a Kisi, ndiwo amene anawakwatira.
23 Los hijos de Musi: Mahli, Eder y Jeremot, tres en total.
Ana a Musi: Mahili, Ederi ndi Yeremoti. Onse analipo atatu.
24 Estos eran los descendientes de Leví por familias, los jefes de familia enumerados individualmente por su nombre: los que tenían veinte años o más y servían en la casa del Señor.
Izi zinali zidzukulu za Levi mwa mabanja awo, atsogoleri a mabanja monga momwe analembedwera mayina awo ndi monga momwenso anawerengedwera, banja lililonse pa lokha. Awa ndi anthu ogwira ntchito oyambira zaka makumi awiri zobadwa kapena kupitirirapo, amene amatumikira mʼNyumba ya Yehova.
25 Porque David dijo: “El Señor, el Dios de Israel, ha dado la paz a su pueblo, y vivirá en Jerusalén para siempre.
Popeza Davide anati, “Pakuti Yehova Mulungu wa Israeli, wapereka mpumulo kwa anthu ake ndipo wabwera kudzakhala mu Yerusalemu kwamuyaya,
26 Así que los levitas ya no necesitan llevar la Tienda ni nada necesario para su servicio”.
sikofunikiranso kuti Alevi azinyamula tenti kapena zipangizo za chipembedzo.”
27 De acuerdo con las instrucciones finales de David, se contaron los levitas de veinte años o más.
Potsata malangizo otsiriza a Davide, Alevi anawerengedwa kuyambira amuna a zaka makumi awiri zakubadwa kapena kupitirirapo.
28 Su misión era ayudar a los descendientes de Aarón en el servicio de la casa del Señor. Eran responsables de los patios y las habitaciones, de la limpieza de todas las cosas sagradas y del trabajo del servicio de la casa de Dios.
Ntchito ya Alevi inali kuthandiza zidzukulu za Aaroni pa ntchito yotumikira mʼNyumba ya Yehova monga kuyangʼanira mabwalo, zipinda zamʼmbali, kuyeretsa zinthu zonse zachipembedzo, ndiponso kuchita ntchito zina za mʼnyumba ya Mulungu.
29 También eran responsables del pan de la proposición que se ponía sobre la mesa, de la harina especial para las ofrendas de grano, de los panes sin levadura, de la cocción, de la mezcla y del manejo de todas las cantidades y medidas.
Iwo amayangʼanira buledi amene amayikidwa pa tebulo, ufa wa nsembe yachakudya, timitanda ta buledi wopanda yisiti: kuphika ndi kusakaniza, ndiponso miyeso yonse ndi kukula kwake.
30 También debían ponerse de pie todas las mañanas para dar gracias y alabar al Señor, y hacer lo mismo al atardecer,
Iwo amayimiriranso mmawa uliwonse kuthokoza ndi kutamanda Yehova. Amachitanso chomwecho madzulo,
31 y siempre que se presentaran holocaustos al Señor, ya fuera en los sábados, lunas nuevas y días festivos. Debían servir regularmente ante el Señor según el número que se les exigiera.
ndiponso popereka nsembe zopsereza kwa Yehova pa Sabata ndi pa chikondwerero cha Mwezi Watsopano, ndi pa nthawi yosankhidwa ya Chikondwerero. Iwo amatumikira pamaso pa Yehova nthawi zonse mwa chiwerengero chawo ndi momwe analangizidwira.
32 Así, los levitas debían cumplir con la responsabilidad de cuidar la Tienda del Encuentro y el santuario, y con sus hermanos los descendientes de Aarón, servían a la casa del Señor.
Ndipo kotero Alevi anachita ntchito yawo ya ku tenti ya msonkhano ya ku Malo Opatulika ndiponso molamulidwa ndi abale awo, zidzukulu za Aaroni, pa ntchito ya mʼNyumba ya Yehova.