< Salmos 87 >
1 De los hijos de Coré. Salmo. Cántico. ¡Él la fundó sobre los montes santos!
Salimo la Ana a Kora. Iye wakhazikitsa maziko ake pa phiri loyera;
2 Yahvé ama las puertas de Sión más que todos los tabernáculos de Jacob.
Yehova amakonda zipata za Ziyoni kupambana malo onse okhalamo a Yakobo.
3 ¡Oh ciudad de Dios, de ti se dicen cosas gloriosas!
Za ulemerero wako zimakambidwa, Iwe mzinda wa Mulungu: (Sela)
4 “Contaré a Rahab y a Babel entre los que me conocen; he aquí a Filistea y a Tiro y al pueblo de los etíopes: han nacido allí.”
“Ndidzanena za Rahabe ndi Babuloni pakati pa iwo amene amandidziwa. Dzikonso la Filisitiya, Turo pamodzi ndi Kusi, ndipo ndidzati, ‘Uyu anabadwira mʼZiyoni.’”
5 Así se dirá de Sión: “Uno por uno, todos han nacido en ella, y es el mismo Altísimo quien la consolidó.”
Ndithudi, za Ziyoni adzanena kuti, “Uyu ndi uyo anabadwira mwa iye, ndipo Wammwambamwamba adzakhazikitsa iyeyo.”
6 Y en el libro de los pueblos, Yahvé escribirá: “Estos nacieron allí.”
Yehova adzalemba mʼbuku la kawundula wa anthu a mitundu ina: “Uyu anabadwira mʼZiyoni.” (Sela)
7 Y cantarán danzando: “Todas mis fuentes están en Ti.”
Oyimba ndi ovina omwe adzati, “Akasupe anga onse ali mwa iwe.”