< Salmos 6 >
1 Al maestro de canto. Para instrumentos de cuerda. En octava. Salmo de David. Yahvé, no quieras argüirme en tu ira, ni corregirme en tu furor.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Molingana ndi seminiti. Salimo la Davide. Inu Yehova, musandidzudzule mu mkwiyo wanu, kapena kundilanga mu ukali wanu.
2 Ten misericordia de mí, oh Yahvé, porque soy débil; sáname, porque hasta mis huesos se sacuden
Ndichitireni chifundo Inu Yehova, pakuti ndalefuka; Inu Yehova chiritseni, pakuti mafupa anga ali pa ululu waukulu.
3 y mi alma está en el colmo de la turbación; mas Tú, Yahvé ¿hasta cuándo?
Moyo wanga uli pa mazunzo aakulu. Mpaka liti, Inu Yehova, mpaka liti?
4 Vuélvete, oh Yahvé, libra mi alma; sálvame por tu misericordia,
Tembenukani Inu Yehova, ndipo mundilanditse; pulumutseni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.
5 porque en la muerte no hay quien se acuerde de Ti; ¿quién te alaba en el sepulcro? (Sheol )
Palibe amene amakukumbukirani pamene wamwalira; Amakutamandani ndani ali ku manda? (Sheol )
6 Me hallo extenuado de tanto gemir, cada noche inundo en llanto mi almohada, y riego con mis lágrimas el lecho.
Ine ndatopa ndi kubuwula; usiku wonse pa bedi panga pamadzaza ndi misozi yanga; ndimanyowetsa pogona panga ndi misozi.
7 A causa de todos mis enemigos, van mis ojos apagándose de tristeza, y envejecen.
Maso anga atupa chifukwa cha chisoni; akulephera kuona chifukwa cha adani anga.
8 Apartaos de mí todos los que obráis la iniquidad; pues Yahvé ha oído la voz de mi llanto.
Chokani kwa ine inu nonse amene mumachita zoyipa, pakuti Yehova wamva kulira kwanga.
9 Yahvé escuchó mi demanda, Yahvé aceptó mi oración.
Yehova wamva kupempha kwanga kofuna chifundo; Yehova walandira pemphero langa.
10 Mis enemigos todos quedarán sonrojados y llenos de vergüenza; huirán súbitamente confundidos.
Adani anga onse adzachita manyazi ndipo adzakhala ndi mantha; adzabwerera msangamsanga mwa manyazi.