< Salmos 35 >

1 De David. Disputa mi causa, oh Yahvé, contra mis contendores; combate Tú a los que me combaten.
Salimo la Davide. Inu Yehova, mulimbane nawo amene akulimbana nane; mumenyane nawo amene akumenyana nane.
2 Echa mano al escudo y al broquel, y levántate en mi socorro.
Tengani chishango ndi lihawo; dzukani ndipo bwerani mundithandize.
3 Empuña la lanza, y cierra contra mis perseguidores. Dile a mi alma: “Tu salvación soy Yo.”
Tengani mkondo ndi nthungo, kulimbana ndi iwo amene akundithamangitsa. Uzani moyo wanga kuti, “Ine ndine chipulumutso chako.”
4 Queden confusos y avergonzados los que buscan mi vida. Vuelvan atrás, cubiertos de oprobio los que maquinan mi perdición.
Iwo amene akufunafuna moyo wanga anyozedwe ndi kuchita manyazi; iwo amene akukonza kuti moyo wanga uwonongeke abwerere mʼmbuyo mochititsa mantha.
5 Sean como la paja ante el viento, acosados por el Ángel de Yahvé.
Akhale ngati mankhusu owuluka ndi mphepo pamene mngelo wa Yehova akuwapirikitsa.
6 Sea su camino obscuro y resbaloso, cuando el Ángel de Yahvé los persiga.
Njira yawo ikhale ya mdima ndi yoterera pamene mngelo wa Yehova akuwathamangitsa.
7 Porque sin causa me tendieron su red; y sin causa cavaron una fosa para mi vida.
Popeza ananditchera ukonde popanda chifukwa ndipo popanda chifukwa andikumbira dzenje,
8 Venga sobre ellos la muerte inesperada, y préndalos la red que para mí escondieron; caigan en la fosa que ellos mismos cavaron.
chiwonongeko chiwapeza modzidzimutsa ukonde umene iwo abisa uwakole, agwere mʼdzenje kuti awonongedwe.
9 Y mi alma se regocijará en Yahvé, y se alegrará de su auxilio.
Pamenepo moyo wanga udzakondwera mwa Yehova ndi kusangalala ndi chipulumutso chake.
10 Todos mis huesos dirán: ¿Quién como Tú, Yahvé, que libras del prepotente al desvalido, y al pobre y afligido de la mano del que lo despoja?
Thupi langa lidzafuwula mokondwera, “Ndani angafanane nanu Yehova? Mumalanditsa osauka kwa amene ali ndi mphamvu zambiri, osauka ndi osowa kwa iwo amene amawalanda.”
11 Se levantaron testigos de iniquidad; me pedían cuentas de cosas que yo ni conocía.
Mboni zopanda chisoni zinayimirira, zinandifunsa zinthu zimene sindikuzidziwa.
12 Por el bien me devolvían mal, para desolación de mi alma.
Iwo anandibwezera zoyipa pa zabwino ndipo anasiya moyo wanga pa chisoni.
13 En tanto que yo, cuando ellos enfermaban, vestía de cilicio, me maceraba con el ayuno, y mis plegarias me golpeaban el seno.
Koma pamene iwo ankadwala, ine ndinavala chiguduli ndi kudzichepetsa ndekha posala zakudya. Pamene mapemphero anga anabwerera kwa ine osayankhidwa,
14 Me portaba como con un amigo, como con un hermano; me encorvaba triste, como quien llora a una madre.
ndinayendayenda ndi kulira maliro, kumulira ngati bwenzi langa kapena mʼbale wanga. Ndinaweramitsa mutu wanga mosweka mtima kukhala ngati ndikulira amayi anga.
15 Ellos, en cambio, se alegraron en mi adversidad, y se juntaron; coligados contra mí me hirieron de improviso, me laceraron sin tregua.
Koma pamene ndinaphunthwa, iwo anasonkhana mosangalala; ondithira nkhondo anasonkhana kutsutsana nane, ineyo osadziwa. Iwo sanasiye kundiyankhulira mawu onyoza.
16 Entre impíos burladores de torta redonda, rechinaron contra mí sus dientes.
Monga anthu osapembedza, iwo anandinyoza mwachipongwe; anandikukutira mano awo.
17 ¿Hasta cuándo. Señor, lo estarás viendo? libra de sus maldades mi vida, de los leones a mi único bien.
Ambuye, mpaka liti mudzakhala mukungoyangʼana? Landitsani moyo wanga ku chiwonongeko chawo, moyo wanga wopambana ku mikango.
18 Te daré gracias en la gran asamblea, te alabare ante un pueblo numeroso.
Ndidzakuyamikani mu msonkhano waukulu; pakati pa gulu lalikulu la anthu ndidzakutamandani.
19 No se alegren a costa mía mis injustos enemigos; no se hagan guiños de ojo los que sin causa me odian,
Musalole adani anga onyenga akondwere chifukwa cha masautso anga; musalole kuti amene amadana nane popanda chifukwa andiyangʼane chamʼmbali mondinyoza.
20 porque ni siquiera hablan de paz, y planean traidoramente fraudes contra los pacíficos de la tierra.
Iwowo sayankhula mwamtendere, koma amaganizira zonamizira iwo amene amakhala mwabata mʼdziko.
21 Ensanchan contra mí sus bocas y dicen: “aja, aja; lo hemos visto con nuestros propios ojos”.
Iwo amandiseka mofuwula ndipo amati, “Haa! Haa! Ndipo ndi maso athuwa ife taziona.”
22 Tú, Yahvé, sí que lo has visto; no calles, Señor, no quieras estar lejos de mí.
Yehova mwaona zimenezi; musakhale chete. Ambuye musakhale kutali ndi ine.
23 Despierta y vela por mi defensa, por mi causa, Dios mío y Señor mío.
Dzukani, ndipo nyamukani kunditeteza! Mulimbane nawo chifukwa cha ine, Mulungu wanga ndi Ambuye anga.
24 Júzgame Tú según tu justicia, Yahvé, Dios mío, que no se alegren a mi costa;
Onetsani kusalakwa kwanga mwa chilungamo chanu, Inu Yehova Mulungu wanga. Musalole kuti akondwere chifukwa cha mavuto anga.
25 que no piensen en su corazón: “Hemos salido con nuestro deseo”; no digan: “Lo hemos devorado.”
Musalole kuti aganize kuti, “Amati atani, zachitika monga momwe timafunira!” Kapena kunena kuti, “Tamutha ameneyu basi.”
26 Confundidos sean y abochornados a una los que se gozan en mi mal. Sean cubiertos de vergüenza e ignominia los que se ensoberbecen contra mí.
Onse amene amakondwera ndi masautso anga achite manyazi ndi kusokonezeka. Onse amene amadzikweza kufuna kundipambana, avekedwe manyazi ndi mnyozo ngati zovala.
27 Alégrense y gócense los que comparten mi causa, y digan siempre: “Grande es Yahvé que se deleita en la paz de su siervo.”
Koma amene amakondwera chifukwa chakuti ndine wosalakwa, afuwule mwachimwemwe ndi chisangalalo. Nthawi zonse azinena kuti, “Yehova akwezeke, Iye amene amakondwera ndi kupeza bwino kwa mtumiki wake.”
28 Y mi lengua proclamará tu justicia; y tu alabanza perpetuamente.
Pakamwa panga padzayankhula za chilungamo chanu ndi za matamando anu tsiku lonse.

< Salmos 35 >