< Salmos 2 >

1 ¿Por qué se amotinan las gentes, y las naciones traman vanos proyectos?
Nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina akufuna kuchita chiwembu? Akonzekeranji zopanda pake anthu?
2 Se han levantado los reyes de la tierra, y a una se confabulan los príncipes contra Yahvé y contra su Ungido.
Mafumu a dziko lapansi akugwirizana nazo; ndipo olamulira asonkhana pamodzi kulimbana ndi Ambuye ndi wodzozedwa wakeyo.
3 “Rompamos (dicen) sus coyundas, y arrojemos lejos de nosotros sus ataduras.”
Iwo akunena kuti, “Tiyeni timasule magoli awo ndipo titaye zingwe zawo.”
4 El que habita en los cielos ríe, el Señor se burla de ellos.
Wokhala mmwamba akuseka; Ambuye akuwanyoza iwowo.
5 A su tiempo les hablará en su ira, y en su indignación los aterrará:
Ndipo iye awadzudzula mu mkwiyo wake ndi kuwaopseza mu ukali wake, kunena kuti,
6 “Pues bien, soy Yo quien he constituido a mi Rey sobre Sión, mi santo monte.”
“Ine ndakhazikitsa mfumu yanga pa Ziyoni, phiri langa loyera.”
7 ¡Yo promulgaré ese decreto de Yahvé! Él me ha dicho: “Tú eres mi Hijo, Yo mismo te he engendrado en este día.
Ine ndidzalengeza zimene Yehova walamula: Iye anati kwa Ine, “Iwe ndiwe mwana wanga; lero Ine ndakhala Atate ako.
8 Pídeme y te daré en herencia las naciones, y en posesión tuya los confines de la tierra,
Tandipempha, ndipo ndidzachititsa kuti mitundu ya anthu ikhale cholowa chako; malekezero a dziko lapansi kuti akhale chuma chako.
9 Con cetro de hierro los gobernarás, los harás pedazos como a un vaso de alfarero.”
Iweyo udzawalamulira ndi ndodo yaufumu yachitsulo; udzawaphwanya zidutswazidutswa ngati zowumba zadothi.”
10 Ahora, pues, oh reyes, comprended, instruíos, vosotros que gobernáis la tierra.
Kotero, inu mafumu, chenjerani; chenjezedwani, inu olamulira a dziko lapansi.
11 Sed siervos de Yahvé con temor y alabadle, temblando, besad sus pies,
Tumikirani Yehova mwa mantha ndi kukondwerera ulamuliro wake monjenjemera.
12 antes que se irrite y vosotros erréis el camino, pues su ira se encenderá pronto. ¡Dichoso quien haya hecho de Él su refugio!
Mpsopsoneni mwanayo kuti angakwiye; kuti mungawonongedwe mʼnjira zanu, pakuti ukali wake utha kuuka mʼkanthawi kochepa. Odala ndi onse amene amathawira kwa Iye.

< Salmos 2 >