< Salmos 18 >

1 Al maestro de coro. Del servidor de Dios, de David, el cual dirigió al Señor las palabras de este cántico en el día en que le libró de las manos de todos sus enemigos y de las de Saúl. Y dijo: Te amo, Yahvé, fortaleza mía, mi peña, mi baluarte, mi libertador,
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide mtumiki wa Yehova. Iye anayimbira Yehova nyimbo iyi pamene Yehovayo anamupulumutsa mʼdzanja la adani ake onse ndiponso mʼdzanja la Sauli. Davide anati: Ine ndimakukondani Inu Yehova, mphamvu zanga.
2 Dios mío, mi roca, mi refugio, broquel mío, cuerno de mi salud, asilo mío.
Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga; Mulungu wanga ndi thanthwe langa mʼmene ndimathawiramo. Chishango changa ndi ndodo yachipulumutso changa, ndi linga langa.
3 Invoco a Yahvé, el digno de alabanza, y quedo libre de mis enemigos.
Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando, ndipo ndapulumutsidwa kwa adani anga.
4 Olas de muerte me rodeaban, me alarmaban los torrentes de iniquidad;
Zingwe za imfa zinandizinga; mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.
5 las ataduras del sepulcro me envolvieron, se tendían a mis pies lazos mortales. (Sheol h7585)
Anandimanga ndi zingwe za ku manda; misampha ya imfa inalimbana nane. (Sheol h7585)
6 En mi angustia invoqué a Yahvé, y clamé a mi Dios; y Él, desde su palacio, oyó mi voz; mi lamento llegó a sus oídos.
Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova; ndinalirira kwa Mulungu wanga kuti andithandize. Ali mʼNyumba yake, anamva mawu anga; kulira kwanga kunafika pamaso pake ndi mʼmakutu mwake.
7 Se estremeció la tierra y tembló; se conmovieron los cimientos de los montes y vacilaron, porque Él ardía de furor.
Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi, ndipo maziko a mapiri anagwedezeka; ananjenjemera chifukwa Iye anakwiya.
8 Humo salió de sus narices; de su boca, fuego devorador; y despedía carbones encendidos.
Mʼmphuno mwake munatuluka utsi; moto wonyeketsa unatuluka mʼkamwa mwake, makala amoto anali lawilawi mʼkamwa mwake.
9 Inclinó los cielos, y descendió con densas nubes bajo sus pies.
Iye anangʼamba thambo natsika pansi; pansi pa mapazi ake panali mitambo yakuda.
10 Subió sobre un querube y voló, y era llevado sobre las alas del viento.
Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka; nawuluka ndi mphepo mwaliwiro.
11 Se ocultaba bajo un velo de tinieblas; aguas tenebrosas y oscuras nubes lo rodeaban como un pabellón.
Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake, chophimba chake chomuzungulira chinali mitambo yakuda ya mlengalenga.
12 Se encendieron carbones de fuego al resplandor de su rostro.
Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake munkachokera matalala, makala amoto ndi ziphaliwali zongʼanima.
13 Tronó Yahvé desde el cielo, el Altísimo hizo resonar su voz;
Yehova anabangula kumwamba ngati bingu, mawu a Wammwambamwamba anamveka ponseponse.
14 y lanzó sus saetas y los dispersó; multiplicó sus rayos, y los puso en derrota.
Iye anaponya mivi yake nabalalitsa adani ake, ndi zingʼaningʼani zake anawagonjetsa.
15 Y aparecieron a la vista los lechos de los océanos; se mostraron desnudos los cimientos del orbe terráqueo, ante la amenaza de Yahvé, al resollar el soplo de su ira.
Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera; maziko a dziko lapansi anakhala poyera, Yehova atabangula mwaukali, pamene mpweya wamphamvu unatuluka mʼmphuno mwanu.
16 Desde lo alto extendió su brazo y me arrebató, sacándome de entre las muchas aguas;
Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira; anandivuwula mʼmadzi ozama.
17 me libró de mi feroz enemigo, de adversarios más poderosos que yo.
Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu, adani anga, amene anali amphamvu kuposa ine.
18 Se echaron sobre mí en el día de mi infortunio; pero salió Yahvé en mi defensa,
Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto, koma Yehova anali thandizo langa.
19 y me trajo a la anchura; me salvó porque me ama.
Iye anandipititsa kumalo otakasuka; anandipulumutsa chifukwa amakondwera nane.
20 Yahvé me ha retribuido conforme a mi rectitud; me remunera según la limpieza de mis manos.
Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa; molingana ndi makhalidwe anga abwino, Iye wandipulumutsa.
21 Porque seguí los caminos de Yahvé, y no me rebelé contra mi Dios;
Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova; ndilibe mlandu wochoka pamaso Mulungu wanga.
22 porque mantuve ante mis ojos todos sus mandamientos y nunca aparté de mí sus estatutos.
Malamulo ake onse ali pamaso panga; sindinasiye malangizo ake.
23 Fui íntegro para con Él, y me cuidé de mi maldad.
Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo.
24 Yahvé me ha retribuido conforme a mi rectitud; según la limpieza de mis manos ante sus ojos.
Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa, molingana ndi kuyera kwa manja anga pamaso pake.
25 Tú eres misericordioso con el misericordioso; con el varón recto, eres recto.
Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu; kwa anthu amakhalidwe abwino, Inu mumaonetsanso makhalidwe abwino,
26 Con el sincero, eres sincero; y con el doble, te haces astuto.
kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu, koma kwa achinyengo mumaonetsanso kunyansidwa nawo.
27 Tú salvas al pueblo oprimido, y humillas los ojos altaneros.
Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa, koma anthu amtima odzikuza mumawatsitsa.
28 Eres Tú quien mantiene encendida mi lámpara, oh Yahvé; Tú, Dios mío, disipas mis tinieblas.
Inu Yehova, sungani nyale yanga kuti iziyakabe; Mulungu wanga wasandutsa mdima wanga kukhala kuwunika.
29 Fiado en Ti embestiré a un ejército; con mi Dios saltaré murallas.
Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo; ndi Mulungu wanga nditha kuchita zosatheka ndi munthu.
30 ¡El Dios mío!... Su conducta es perfecta, Su palabra acrisolada. Él mismo es el escudo de cuantos lo buscan como refugio.
Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro; mawu a Yehova alibe cholakwika. Iye ndi chishango kwa onse amene amathawira kwa Iye.
31 Pues ¿quién es Dios fuera de Yahvé? o ¿qué roca hay si no es el Dios nuestro?
Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova? Ndipo ndani amene ndi Thanthwe kupatula Mulungu wathu?
32 Aquel Dios que me ciñó de fortaleza e hizo inmaculado mi camino.
Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu ndi kulungamitsa njira yanga.
33 El que volvió mis pies veloces como los del ciervo, y me afirmó sobre las cumbres.
Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi; Iye amandithandiza kuyimirira pamwamba pa mapiri.
34 El que adiestró mis manos para la pelea, y mi brazo para tender el arco de bronce.
Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; manja anga amatha kuthyola uta wachitsulo.
35 Tú me diste por broquel tu auxilio, me sostuvo tu diestra; tu solicitud me ha engrandecido.
Inu mumandipatsa chishango chachipambano, ndipo dzanja lanu lamanja limandichirikiza; mumawerama pansi kundikuza.
36 Ensanchaste el camino a mis pasos, y mis pies no flaquearon.
Munakulitsa njira yoyendamo ine, kuti mapazi anga asaguluke.
37 Perseguía a mis enemigos y los alcanzaba; y no me volvía hasta desbaratarlos.
Ndinathamangitsa adani anga ndi kuwapitirira; sindinabwerere mpaka atawonongedwa.
38 Los destrozaba y no podían levantarse; caían bajo mis pies.
Ndinakantha adaniwo kotero kuti sanathenso kudzuka; anagwera pa mapazi anga.
39 Tú me revestías de valor para el combate, sujetabas a mi cetro a los que me resistían.
Inu munandiveka ndi mphamvu yokachitira nkhondo, munachititsa kuti ndigonjetse adani anga.
40 Ponías en fuga a mis enemigos, dispersabas a cuantos me aborrecían.
Inu munachititsa adani anga kutembenuka, kuonetsa misana yawo pothawa, ndipo ine ndinawononga adani angawo.
41 Vociferaban, mas no había quien los auxiliase; (clamaban) a Yahvé mas Él no los oía.
Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa. Analirira kwa Yehova koma sanawayankhe.
42 Y yo los dispersaba como polvo que el viento dispersa; los pisoteaba como el lodo de las calles.
Ine ndinawaperesa ngati fumbi lowuluka ndi mphepo. Ndinawapondaponda ngati matope a mʼmisewu.
43 Me libraste de las contiendas del pueblo, me has hecho cabeza de las naciones; un pueblo que no conocía me sirve;
Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa anthu; mwandisandutsa kukhala mtsogoleri wa anthu a mitundu ina. Anthu amene sindikuwadziwa ali pansi pa ulamuliro wanga.
44 con atento oído me obedecen; los extraños me adulan.
Alendo amadzipereka okha pamaso panga; akangomva za ine amandigonjera.
45 Los extranjeros palidecen, y abandonan, temblando, sus fortalezas.
Iwo onse anataya mtima; anatuluka mʼmalinga awo akunjenjemera.
46 ¡Vive Yahvé! ¡Bendita sea mi Roca! ¡Sea ensalzado el Dios mi Salvador!
Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa! Akuzike Mulungu Mpulumutsi wanga!
47 Aquel Dios que me otorgó la venganza, que sujetó a mí las naciones;
Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango, amene amagonjetsa anthu a mitundu yonse amene ali pansi pa ulamuliro wanga,
48 que me libró de mis enemigos, que me encumbró sobre mis opositores, y me salvó de las manos del hombre violento.
amene amandipulumutsa mʼmanja mwa adani anga. Inu munandikuza kuposa adani anga; munandilanditsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
49 Por eso te alabaré entre las naciones, oh Yahvé; cantaré himnos a tu Nombre.
Choncho ine ndidzakutamandani pakati pa anthu a mitundu ina, Inu Yehova; ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.
50 Él da grandes victorias a su rey, y usa de misericordia con su ungido, con David y su linaje, por toda la eternidad.
Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake; amaonetsa chikondi chosasinthika kwa wodzozedwa wake, kwa Davide ndi zidzukulu zake kwamuyaya.

< Salmos 18 >