< Salmos 146 >

1 ¡HalIelú Yah! Alaba a Yahvé, alma mía.
Tamandani Yehova. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.
2 Toda mi vida alabaré a Yahvé; cantaré salmos a mi Dios mientras yo viva.
Ndidzatamanda Yehova ndi moyo wanga wonse; ndidzayimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wanga nthawi yonse ya moyo wanga.
3 No pongáis vuestra confianza en los príncipes, en un hijo de hombre, que no puede salvar.
Musamadalire mafumu, anthu osakhalitsa, amene sangathe kupulumutsa.
4 Apenas el soplo le abandona, él vuelve a su polvo, y entonces se acaban todos sus designios.
Pamene mizimu yawo yachoka, iwo amabwerera ku dothi; zimene ankafuna kuchita zimatha tsiku lomwelo.
5 Dichoso en cambio quien tiene en su ayuda al Dios de Jacob, y pone su esperanza en Yahvé, su Dios,
Wodala ndi amene thandizo lake ndi Mulungu wa Yakobo.
6 Creador del cielo y de la tierra, del mar y de cuanto contienen. Él conserva siempre su fidelidad;
Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi, nyanja ndi zonse zili mʼmenemo; Yehova, amene ndi wokhulupirika kwamuyaya.
7 hace justicia a los oprimidos, y da pan a los hambrientos. Es Yahvé quien desata a los cautivos;
Iye amachitira chilungamo anthu oponderezedwa ndipo amapereka chakudya kwa anthu anjala. Yehova amamasula amʼndende,
8 es Yahvé quien abre los ojos de los ciegos; Yahvé levanta a los agobiados; Yahvé ama a los justos;
Yehova amatsekula maso anthu osaona, Yehova amadzutsa onse amene awerama pansi, Yehova amakonda anthu olungama.
9 Yahvé cuida de los peregrinos; sustenta al huérfano y a la viuda, y trastorna los caminos de los malvados.
Yehova amasamalira alendo ndipo amathandiza ana ndi akazi amasiye, koma amasokoneza njira za anthu oyipa.
10 Reinará Yahvé para siempre, el Dios tuyo, oh Sión, de edad en edad. ¡HalIelú Yah!
Yehova ndiye Mfumu mpaka muyaya, Mulungu wako iwe Ziyoni, pa mibado yonse. Tamandani Yehova.

< Salmos 146 >