< Salmos 140 >
1 Al maestro de coro. Salmo de David. Líbrame, Yahvé, del hombre malo; defiéndeme del hombre violento,
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Landitseni Yehova kwa anthu oyipa; tetezeni kwa anthu ankhanza,
2 de esos que en su corazón maquinan cosas perversas, que provocan contiendas cada día;
amene mu mtima mwawo amakonza zinthu zoyipa ndi kuyambitsa nkhondo tsiku lililonse.
3 afilan su lengua como la serpiente, tienen veneno de áspid bajo sus labios.
Iwo amanola malilime awo kukhala akuthwa ngati a njoka; pa milomo yawo pali ululu wa mamba. (Sela)
4 Sálvame, Yahvé, de las manos del inicuo, guárdame del impío, de los que intentan hacerme caer.
Tetezeni Inu Yehova, kwa anthu oyipa; tchinjirizeni kwa anthu ankhanza amene amakonza zokola mapazi anga.
5 Los soberbios me esconden lazos, y tienen mallas como red; me colocan trampas junto al camino.
Anthu odzikuza anditchera msampha mobisika; iwo atchera zingwe za maukonde awo ndipo anditchera misampha pa njira yanga. (Sela)
6 Yo digo a Yahvé: Tú eres mi Dios; escucha, Yahvé, la voz de mi súplica.
Inu Yehova, ine ndikuti, “Ndinu Mulungu wanga.” Imvani kupempha kwanga Yehova.
7 Señor Yahvé, poderoso auxilio mío, Tú cubres mi cabeza en el día de la batalla.
Inu Ambuye Wamphamvuzonse, Mpulumutsi wanga wamphamvu, mumateteza mutu wanga tsiku lankhondo.
8 No satisfagas, Yahvé, los deseos del inicuo, ni cumplas sus designios.
Musawapatse anthu oyipa zokhumba zawo, Inu Yehova; musalole kuti zokonza zawo zitheke, mwina iwo adzayamba kunyada. (Sela)
9 No levanten cabeza los que me asedian; caiga sobre ellos la malicia de sus lenguas.
Mitu ya amene andizungulira iphimbidwe ndi masautso amene milomo yawo yayambitsa.
10 Lluevan sobre ellos carbones encendidos, precipítalos en abismos, para no levantarse más.
Makala amoto agwere pa iwo; aponyedwe pa moto, mʼmaenje amatope, asatulukemonso.
11 El hombre de mala lengua no durará en la tierra; los infortunios caerán de golpe sobre el violento.
Musalole kuti anthu achipongwe akhazikike mʼdziko; choyipa chilondole anthu ankhanza.
12 Sé que Yahvé tomará la defensa del desvalido, hará justicia a los pobres.
Ndikudziwa kuti Yehova amapereka chiweruzo cholungama kwa anthu osauka, ndipo amateteza zolinga za anthu osowa.
13 Ciertamente los justos celebrarán tu Nombre; los rectos habitarán en tu presencia.
Zoonadi anthu olungama adzatamanda dzina lanu, ndipo anthu owongoka mtima adzakhala pamaso panu.