< Proverbios 3 >

1 Hijo mío, no te olvides de mi ley; guarda en tu corazón mis preceptos,
Mwana wanga, usayiwale malangizo anga, mtima wako usunge malamulo anga.
2 porque te darán longevidad, (felices) años de vida y prosperidad.
Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka ndipo udzakhala pa mtendere.
3 ¡Que nunca la misericordia y la verdad se aparten de ti! Átalas a tu cuello, escríbelas en la tabla de tu corazón.
Makhalidwe ochitira ena chifundo ndi owonetsa kukhulupirika asakuchokere. Uwamangirire mʼkhosi mwako ngati mkanda ndi kuwalemba pa mtima pako.
4 Así hallarás gracia y verdadera sabiduría a los ojos de Dios y a los ojos de los hombres.
Ukatero udzapeza kuyanja ndi mbiri yabwino pamaso pa Mulungu ndi anthu.
5 Confía en el Señor con todo tu corazón y no te apoyes en tu propia inteligencia.
Uzikhulupirira Yehova ndi mtima wako wonse ndipo usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.
6 En todas tus empresas piensa en Él, y Él dirigirá tus caminos.
Pa zochita zako zonse uvomereze kuti Mulungu alipo, ndipo Iye adzawongola njira zako.
7 No te creas sabio a tus ojos, teme a Dios, y huye del mal;
Usamadzione ngati wa nzeru. Uziopa Yehova ndi kupewa zoyipa.
8 será medicina para tu cuerpo, y refrigerio para tus huesos.
Ukatero thupi lako lidzakhala la moyo wabwino ndi mafupa ako adzakhala olimba.
9 Honra a Dios con tu hacienda, y con las primicias de todos tus frutos;
Uzilemekeza Yehova ndi chuma chako chonse; zokolola zonse zoyamba kucha uzilemekeza nazonso Yehova.
10 con eso se llenará de abundancia tus graneros, y tus lagares rebosarán de mosto.
Ukatero nkhokwe zako zidzadzaza ndi zinthu zambiri, ndiponso mitsuko yako idzadzaza ndi vinyo.
11 No deseches, hijo mío, la corrección de Yahvé, ni tengas aversión cuando Él te reprenda.
Mwana wanga usanyoze malangizo a Yehova, ndipo usayipidwe ndi chidzudzulo chake.
12 Pues Yahvé castiga a aquel a quien ama, como un padre al hijo en quien se complace.
Paja Yehova amadzudzula amene amamukonda, monga abambo achitira mwana amene amakondwera naye.
13 ¡Dichoso el hombre que halló la sabiduría, el varón que ha adquirido la inteligencia!
Wodala munthu amene wapeza nzeru, munthu amene walandira nzeru zomvetsa zinthu,
14 Mejor es su adquisición que la de la plata; y más preciosos que el oro son sus frutos.
pakuti phindu la nzeru ndi labwino kuposa la siliva, phindu lakelo ndi labwino kuposanso golide.
15 Ella es más apreciable que las perlas; no hay cosa deseable que la iguale.
Nzeru ndi yoposa miyala yamtengowapatali; ndipo zonse zimene umazikhumba sizingafanane ndi nzeru.
16 En su diestra (trae) larga vida, en su siniestra riquezas y honores.
Mʼdzanja lake lamanja muli moyo wautali; mʼdzanja lake lamanzere muli chuma ndi ulemu.
17 Sus caminos son caminos deliciosos, y llenas de paz todas sus sendas.
Njira zake ndi njira zosangalatsa, ndipo mu njira zake zonse muli mtendere.
18 Es árbol de vida para los que echan mano de ella, y dichoso el que la tiene asida.
Nzeru ili ngati mtengo wopatsa moyo kwa oyigwiritsitsa; wodala munthu amene amayigwiritsa kwambiri.
19 Por la sabiduría fundó Dios la tierra, y por la inteligencia estableció los cielos;
Yehova anakhazikitsa dziko lapansi pogwiritsa ntchito nzeru. Anagwiritsanso ntchito nzeru zakudziwa bwino zinthu pamene ankakhazikitsa zakumwamba.
20 por su ciencia fueron abiertos los abismos; y destilan las nubes rocío.
Mwa nzeru zake Yehova anatumphutsa madzi kuchokera mʼnthaka ndiponso mitambo inagwetsa mvula.
21 Hijo mío, no se aparten ellas de tus ojos; guarda la sabiduría y la prudencia;
Mwana wanga usunge nzeru yeniyeni ndi khalidwe lomalingarira zinthu bwino. Zimenezi zisakuchokere.
22 pues serán vida para tu alma y adorno para tu cuello.
Zimenezi zidzakupatsa moyo, moyo wake wosangalatsa ndi wabwino ngati mkanda wa mʼkhosi.
23 Así seguirás confiado tu camino, y no vacilará tu pie.
Choncho udzayenda pa njira yako mosaopa kanthu, ndipo phazi lako silidzapunthwa;
24 Te acostarás sin temor; y si te acuestas, tu sueño será dulce.
pamene ugona pansi, sudzachita mantha; ukadzagona pansi tulo tako tidzakhala tokoma.
25 No tendrás que temer repentinos espantos, ni los ataques de los impíos cuando te acometieren;
Usaope tsoka lobwera mwadzidzidzi kapena chiwonongeko chimene chidzagwera anthu oyipa,
26 porque Yahvé estará a tu lado, y preservará tu pie de quedar preso.
pakuti Yehova adzakulimbitsa mtima ndipo adzasunga phazi lako kuti lisakodwe mu msampha.
27 No niegues un beneficio al necesitado cuando esté a tu alcance el hacerlo.
Usaleke kuchitira zabwino amene ayenera kulandira zabwino, pamene uli nazo mphamvu zochitira zimenezi.
28 No digas a tu prójimo: “Vete y vuelve, mañana te daré”, estando en tu poder el (atenderlo).
Usanene kwa mnansi wako kuti, “Pita, uchite kubweranso. Ndidzakupatsa mawa” pamene uli nazo tsopano.
29 No maquines ningún mal contra tu prójimo mientras él vive tranquilamente contigo.
Usamukonzere chiwembu mnansi wako, amene anakhala nawe pafupi mokudalira.
30 Jamás pleitees con nadie sin motivo, si no te ha hecho mal.
Usakangane ndi munthu wopanda chifukwa pamene iye sanakuchitire zoyipa.
31 No envidies al hombre violento, ni sigas sus senderos.
Usachite naye nsanje munthu wachiwawa kapena kutsanzira khalidwe lake lililonse.
32 Porque Yahvé detesta al perverso, pero tiene trato íntimo con los justos.
Pakuti Yehova amanyansidwa ndi munthu woyipa koma amayanjana nawo anthu olungama.
33 Sobre la casa del malvado pesa la maldición de Yahvé, el cual bendice la morada del justo.
Yehova amatemberera nyumba ya munthu woyipa, koma amadalitsa nyumba ya anthu olungama.
34 Se burla de los burladores, y da su gracia a los humildes.
Anthu onyoza, Iye amawanyoza, koma amakomera mtima anthu odzichepetsa.
35 La gloria es la herencia de los sabios, en tanto que los necios se acarrean ignominia.
Anthu anzeru adzalandira ulemu, koma zitsiru adzazichititsa manyazi.

< Proverbios 3 >