< Proverbios 18 >
1 Va tras sus propios deseos el que se separa (del amigo); todo su empeño consiste en pleitear.
Munthu wokonda kukhala yekha amafunafuna zomukomera yekha; iye amatsutsana ndi malangizo onse anzeru.
2 Al necio no le gusta ser sensato, se deja llevar por los gustos de su corazón.
Chitsiru chilibe chidwi chomvetsa zinthu, koma chimakondwera ndi kuyankhula maganizo ake okha.
3 Con la impiedad llega también la ignominia, y con la ignominia la deshonra.
Kuyipa mtima kukabwera, manyozonso amabwera. Manyazi amabwera pamodzi ndi kunyozeka.
4 Aguas profundas son las palabras de la boca del hombre, torrente caudaloso la fuente de la sabiduría.
Mawu a munthu ali ngati madzi akuya, kasupe wa nzeru ndiye mtsinje wotumphuka.
5 No está bien tener miramientos con el malvado, para torcer el derecho contra un justo.
Si kwabwino kukondera munthu woyipa pa milandu; kapena kupondereza munthu wosalakwa.
6 Los labios del necio se meten en contiendas, y su boca provoca litigios.
Mawu a chitsiru amautsa mkangano; pakamwa pake pamayitana mkwapulo.
7 La boca del necio es su ruina, y sus labios son un lazo para su alma.
Pakamwa pa chitsiru ndipo pamabweretsa chiwonongeko chake, ndipo milomo yake ili ngati msampha wa moyo wake.
8 Las palabras del chismoso son como dulces bocados, penetran hasta lo más hondo de las entrañas.
Mawu a miseche ali ngati chakudya chokoma; amalowa mʼmimba mwa munthu.
9 Quien es remiso en sus labores, hermano es del que disipa sus bienes.
Munthu waulesi pa ntchito yake ali pachibale ndi munthu amene amawononga zinthu.
10 Ciudadela fuerte es el nombre de Yahvé, en ella se refugia el justo y está seguro.
Dzina la Yehova lili ngati nsanja yolimba; wolungama amathawiramo napulumuka.
11 Las riquezas son para el rico una ciudad fuerte, en su fantasía le parecen una alta muralla.
Chuma cha anthu olemera chili ngati mzinda wake wolimba; chili ngati khoma lalitali limene amaganiza kuti limutchinjiriza.
12 Antes de la caída se engríe el corazón humano, y a la gloria precede la humillación.
Chiwonongeko chisanafike, mtima wa munthu umakhala wonyada, koma ulemu umatsatira kudzichepetsa.
13 Quien responde antes de escuchar, muestra su insensatez y confusión.
Ukayankha usanamvetse bwino nkhani, umenewo ndi uchitsiru ndipo umachita manyazi.
14 El espíritu sostiene al hombre en la flaqueza pero al espíritu abatido ¿quién lo sostendrá?
Mtima wa munthu utha kupirira pa matenda, koma munthu akataya mtima ndani angathe kumulimbitsanso.
15 El corazón prudente adquiere sabiduría, y el oído de los sabios busca doctrina.
Munthu wanzeru amawonjezera nzeru zina; amafunafuna kudziwa bwino zinthu.
16 Los presentes allanan al hombre el camino, y lo llevan a la presencia de los magnates.
Mphatso ya munthu imamutsekulira njira yomufikitsa pamaso pa anthu akuluakulu.
17 Inocente parece el que primero expone su causa, pero viene su adversario y lo examina.
Amene amayamba kufotokoza mlandu wake amaoneka ngati wolungama ndiye mpaka mnzake atabwera ndi kumufunsa bwino.
18 La suerte pone fin a las contiendas, y decide entre los poderosos.
Kuchita maere kumathetsa mikangano; amalekanitsa okangana amphamvu.
19 Un hermano ofendido (resiste) más que una fortaleza, y sus querellas son como los cerrojos de una ciudadela.
Mʼbale amene wamuthandiza amakhala ngati mzinda wolimba, koma kukangana naye kumatsekereza thandizo.
20 De los frutos de su boca sacia el hombre su vientre; se harta del producto de sus labios.
Munthu amapeza bwino malingana ndi zoyankhula zake. Adzakhuta ndi zipatso za pakamwa pake.
21 La muerte y la vida están en poder de la lengua; cual sea su uso, tales serán los frutos que se comen.
Mawu ako angathe kukuphetsa kapena kukukhalitsa moyo. Wokonda kuyankhulayankhula adzadya zipatso zake.
22 El que halla una esposa halla cosa buena, es un favor que le viene de Yahvé.
Wapeza mkazi wapeza chinthu chabwino ndipo Yehova amamukomera mtima.
23 Habla el pobre suplicando, mas el rico responde con aspereza.
Munthu wosauka amapempha koma munthu wolemera amayankha mwaukali.
24 Amigos hay que solo sirven para perdición, pero hay también amigos más adictos que un hermano.
Pali abwenzi amene chibwenzi chawo nʼchapamaso, koma pali bwenzi limene limakukangamira kuposa mʼbale wako.