< Oseas 10 >
1 Era Israel una vid frondosa, cargada de frutos; pero cuanto más abundó su fruto, tanto mayor fue el número de sus altares; cuanto mejor su tierra, tanto más riqueza hubo en sus massebas.
Israeli anali mpesa wotambalala; anabereka zipatso zambiri. Pamene zipatso zawo zinanka zichuluka, anawonjezera kumanga maguwa ansembe. Pamene dziko lake linkatukuka, anakongoletsa miyala yake yopatulika.
2 Está dividido su corazón, pagarán ahora sus culpas. Él hará pedazos sus altares, destruirá sus massebas.
Mtima wawo ndi wonyenga ndipo tsopano ayenera kulangidwa chifukwa cha kulakwa kwawo. Yehova adzagumula maguwa awo ansembe ndi kuwononga miyala yawo yopatulika.
3 Entonces dirán: “No tenemos rey porque no tememos a Yahvé, y ¿qué podrá hacer el rey por nosotros?”
Pamenepo anthuwo adzanena kuti, “Ife tilibe mfumu chifukwa sitinaope Yehova. Koma ngakhale tikanakhala ndi mfumu, kodi mfumuyo ikanatichitira chiyani?”
4 HabIan vanas palabras, juran en falso, hacen pactos; por eso el juicio brota como ajenjo en los surcos del campo.
Mafumu amalonjeza zambiri, amalumbira zabodza pochita mapangano. Kotero maweruzo amaphuka ngati zitsamba zakupha mʼmunda umene walimidwa.
5 Los habitantes de Samaria están llenos de temor, por las novillas de Betaven; pues su pueblo llora por (el ídolo), y sus sacerdotes tiemblan por él porque queda desvanecida su gloria.
Anthu amene amakhala mu Samariya akuchita mantha chifukwa cha fano la mwana wangʼombe ku Beti-Aveni. Anthu ake adzalirira fanolo, chimodzimodzinso ansembe ake adamawo, amene anakondwera ndi kukongola kwake, chifukwa lachotsedwa pakati pawo ndi kupita ku ukapolo.
6 El ídolo mismo será llevado a Asiria, como presente para el rey vengador. Cubrirse de confusión Efraím, e Israel tendrá que avergonzarse de sus designios.
Fanolo lidzatengedwa kupita ku Asiriya ngati mphatso kwa mfumu yayikulu. Efereimu adzachititsidwa manyazi chifukwa cha mafano ake amitengo.
7 Destruida será Samaria, quedando su rey como un pedazo de madera sobre las aguas.
Samariya ndi mfumu yake adzatengedwa kupita kutali ngati kanthambi koyenda pa madzi.
8 Serán destruidos los altos de Avén, el pecado de Israel; espinos y abrojos crecerán sobre sus altares. Entonces dirán a las montañas: ¡Cubridnos!; y a las colinas: ¡Caed sobre nosotros!
Malo opembedzerako mafano a ku Aveni adzawonongedwa. Ili ndiye tchimo la Israeli. Minga ndi mitungwi zidzamera ndi kuphimba maguwa awo ansembe. Kenaka anthu adzawuza mapiri kuti, “Tiphimbeni!” ndipo adzawuza zitunda kuti, “Tigwereni!”
9 Desde los días de Gabaá, has pecado, oh Israel, allí han perseverado (en el pecado). ¿No los alcanzará en Gabaá la guerra contra los hijos de la maldad?
“Iwe Israeli, wachimwa kuyambira mʼmasiku a Gibeya, ndipo wakhala uli pomwepo. Kodi nkhondo sinagonjetse anthu ochita zoyipa ku Gibeya?
10 Según mi deseo los castigaré; se congregarán contra ellos los pueblos, para castigarlos por su doble maldad.
Pamene ndifunire, ndidzalanga anthuwo; mitundu ya anthu idzasonkhanitsidwa kudzalimbana nawo, kuwayika mʼndende chifukwa cha uchimo wawo waukulu.
11 Efraím es una novilla bien adiestrada, que ama la trilla; mas Yo pondré (el yugo) sobre su hermosa cerviz. Unciré a Efraím, Judá tirará del arado, y Jacob abrirá los surcos.
Efereimu ndi mwana wangʼombe wamkazi wophunzitsidwa amene amakonda kupuntha tirigu, choncho Ine ndidzayika goli mʼkhosi lake lokongolalo. Ndidzasenzetsa Efereimu goli, Yuda ayenera kulima, ndipo Yakobo ayenera kutipula.
12 Sembrad en justicia y segaréis los frutos de la misericordia. Cultivad vuestra tierra inculta, pues tiempo es de buscar a Yahvé hasta que venga, para derramar sobre vosotros la justicia.
Mufese nokha chilungamo ndipo mudzakolola chipatso cha chikondi changa chosasinthika. Ndipo tipulani munda wanu wosalimidwawo; pakuti ino ndi nthawi yofunafuna Yehova, mpaka Iye atabwera kudzakugwetserani mivumbi ya chilungamo.
13 Arasteis maldad, y cosechasteis iniquidad; comisteis el fruto de la mentira. Confiaste en tus propios planes, en la multitud de tus guerreros.
Koma inu munadzala zolakwa, mwakolola zoyipa; mwadya chipatso cha chinyengo. Chifukwa mumadalira mphamvu zanu ndiponso ankhondo anu ochulukawo,
14 Por eso se levantará tumulto entre tu gente, y todas tus fortalezas serán destruidas, como Salmán destruyó a Bet-Arbel, en el día de la batalla; cuando la madre fue estrellada juntamente con los hijos.
phokoso lankhondo lidzamveka pakati pa anthu anga kotero kuti malinga anu onse adzawonongeka, monga momwe Salimani anawonongera Beti-Aribeli pa nthawi ya nkhondo; pamene anapha amayi pamodzi ndi ana awo omwe.
15 Esto trajo sobre vosotros Betel, a causa de vuestra extrema maldad.
Momwemonso zidzakuchitikira, iwe Beteli chifukwa kuyipa kwako ndi kwakukulu. Tsiku limeneli likadzafika, mfumu ya Israeli idzawonongedwa kwathunthu.