< Mateyo 26 >
1 Yesu mpwalapwisha kubeyisha makani awa, walabambila beshikwiya bakendi eti,
Yesu atamaliza kuyankhula zonsezi, anati kwa ophunzira ake,
2 “Mucinshi cena kwambeti papita masuba abili, kusekelela kwa Pasika nikutatike, neco Mwana Muntu nakatwalwe kuya kupopwa.”
“Monga mukudziwa, kwatsala masiku awiri kuti Paska ifike ndipo Mwana wa Munthu adzaperekedwa kuti apachikidwe.”
3 Pacindi copeleco, bamakulene beshimilumbo, ne bamakulene Baciyuda, balabungana mu ng'anda ya Mukulene wa Beshimilumbo bonse, lina lyakendi Kayafa.
Pamenepo akulu a ansembe ndi akuluakulu anasonkhana ku nyumba ya mkulu wa ansembe dzina lake Kayafa,
4 Balikupangana mobelela kumwikatila Yesu kwakubula nabambi kwinshiba ne kumushina.
ndipo anapangana kuti amugwire Yesu mobisa ndi kumupha.
5 Nsombi balikwambeti, “Nkatwelela kumwikata mumasuba akusekelela Pasika sobwe, pakwinga ngapaba minyungwe pakati pabantu.”
Ndipo anati, “Osati nthawi yaphwando chifukwa pangabuke chipolowe pakati pa anthu.”
6 Yesu mpwalikuba ku Betaniya, mu ng'anda ya Shimoni shimankuntu.
Yesu ali ku Betaniya mʼnyumba Simoni Wakhate,
7 Nomba mpobalikulya patebulu, palashika mutukashi walikuba wamanta nsupa mwalikuba mafuta anunkila amulo wadula, walatatika kwitila mafutawo pamutwi wa Yesu.
mayi wina anabwera kwa Iye ndi botolo la mafuta onunkhira a mtengowapatali, amene anathira pa mutu pake Iye akudya pa tebulo.
8 Nomba beshikwiya bakendi mpobalaboneco, balepilwa kwine, ne kwambeti, “Inga nikwataila cani cisa mafuta pabulyo.”
Ophunzira ataona izi anayipidwa nafunsa kuti, “Chifukwa chiyani akuwononga chotere?
9 “Mafutawa ayandikanga kwaulisha mali angi, ne kunyamfwalishako bantu bapenshi.”
Mafuta amenewa akanatha kugulitsidwa pa mtengo waukulu, ndipo ndalama zake zikanaperekedwa kwa osauka.”
10 Yesu pakwinshiba byonse mbyobalikwamba, walabepusheti, “Mulamupenshelenga cani mutukashi uyu? Ici ncalenshili ame caina.”
Yesu podziwa izi anawawuza kuti, “Chifukwa chiyani mukumuvutitsa mayiyu? Wandichitira Ine chinthu chabwino.
11 “Nimukutenga bantu bapenshi cindi conse, nsombi nteti munkutenga cindi conse sobwe,
Osauka mudzakhala nawo nthawi zonse, koma simudzakhala ndi Ine nthawi zonse.
12 nendi letili mafutawa pamubili pakame, ‘lananikili limo kantana mbikwa mu manda.’
Pamene wathira mafuta onunkhirawa pa thupi langa, wachita izi kukonzekera kuyikidwa kwanga mʼmanda.
13 Cakubinga ndamwambilishingeti, kulikonse uko bantu nkweshi bakakambaukenga Mulumbe uwu Waina pacishi conse, naco ici ncalenshi ni bakacambenga, kwambeti bantu bakanukilenga ponga.”
Zoonadi, ndikuwuzani kuti kulikonse kumene Uthenga Wabwinowu udzalalikidwa ku dziko lonse lapansi, zimene wachitazi zidzanenedwanso pomukumbukira.”
14 Panyuma pakendi umo wabeshikwiya likumi ne babili, Yuda Sikalyote walaya kuli ba makulene beshimilumbo.
Pamenepo mmodzi wa khumi ndi awiriwo wotchedwa Yudasi Isikarioti anapita kwa akulu a ansembe
15 Ne kuya kubepusheti, “Inga nimumpe cani ndamulisha Yesu kuli njamwe?” Naboyo popelapo balabelenga mali a silifa makumi atatu ne kumupa.
nafunsa kuti, “Kodi mundipatsa chiyani ngati nditamupereka Iye kwa inu?” Pamenepo anamuwerengera ndalama zokwanira masiliva makumi atatu.
16 Kufuma cindico, Yuda Sikalyote, walatatika kulangaula cindi celela ca kumwikatilapo Yesu.
Kuyambira pamenepo Yudasi anafunafuna nthawi yabwino yoti amupereke Yesu.
17 Pabusuba bwakutanguna bwakusekelela masuba ashinkwa wabula cishifufumusha, beshikwiya bakendi balesa kuli Yesu ne kumwipusheti, “Twenga kupeyo kuya kumubambila musena wa kulyelako Pasika?”
Pa tsiku loyamba laphwando la buledi wopanda yisiti, ophunzira anabwera kwa Yesu ndi kumufunsa kuti, “Kodi mukufuna tikakonze kuti malo odyera Paska?”
18 Yesu walabambileti, “Kamuyani mu munshi uwu kumuntu wakuti wakuti, muye mwambeti, cindi cabo Bashikwiyisha cilipepi, balayandanga kwisa kulyela Pasika pamo ne beshikwiya babo kwenu.”
Iye anayankha kuti, “Pitani mu mzinda kwa munthu wakutiwakuti ndipo kamuwuzeni kuti, ‘Aphunzitsi akuti, nthawi yanga yoyikidwa yayandikira. Ine ndidzadya phwando la Paska ndi ophunzira anga ku nyumba kwako.’”
19 Basa beshikwiya balensa mbuli Yesu ncalabambila, balabamba Pasika.
Pamenepo ophunzira ake anachita monga momwe Yesu anawawuzira ndipo anakonza Paska.
20 Mansailo mpokwalashipuluka, Yesu ne beshikwiya bakendi likumi ne babili balekala patebulu ne kutatika kulya.
Kutada, Yesu ndi ophunzira ake khumi ndi awiriwo anakhala pa tebulo nʼkumadya.
21 Kabacilya, Yesu walabambileti, “Cakubinga ndamwambilishingeti, umo pali njamwe langulishinga kubalwani bakame.”
Akudya, Iye anati, “Zoonadi, ndikuwuzani kuti mmodzi wa inu adzandipereka.”
22 Beshikwiya balanyumfwa nsoni, neco, balatatika kumwipusha Yesu, umo ne umo Nkambo, sena njame?
Iwo anamva chisoni kwambiri ndipo anayamba kuyankhulana naye mmodzimmodzi nati, “Kodi nʼkukhala ine Ambuye?”
23 Yesu walabakumbuleti, “Umo pali njamwe, uyo walyanga pamo nenjame mumbale iyi, epeloyo elangulishinga.
Yesu anayankha nati, “Iye amene akusunsa mʼmbale pamodzi ndi Ine, yemweyo adzandipereka.
24 ‘Mwana Muntu nafwe nditu, mbuli Mabala ncalambanga,’ Nomba ukute malele muntu laulishinga Mwana Muntu, ne calabako cena nalabula kusemwapo muntuyo.”
Mwana wa Munthu adzaphedwa monga mmene kunalembedwera za Iye. Koma tsoka kwa munthu amene apereka Mwana wa Munthu! Kukanakhala bwino kwa iye akanapanda kubadwa.”
25 Yuda Sikalyote, usa walamulisha, walepusheti, “Bashikwiyisha, cakubinga nkandela kuba ame ngomulambanga ayi?” Yesu walamukumbuleti, “Ulamba omwine.”
Ndipo Yudasi amene anamupereka Iye anati, “Monga nʼkukhala ine Aphunzitsi?” Yesu anayankha nati, “Iwe watero.”
26 Cindi ncobalikulya, Yesu walamanta shinkwa walapaila ne kulumba Lesa, walakomona komona, walayabila beshikwiya, ne kwambeti, “Mantani, kamulyani, uwu emubili wakame.”
Pamene ankadya, Yesu anatenga buledi, nayamika ndipo anamunyema nagawira ophunzira ake nanena kuti, “Tengani, idyani; ili ndi thupi langa.”
27 Kayi walamanta nkomeshi yesula waini, walalumba Lesa, ne kubapa beshikwiya basa, nekubambileti, “Kamunwa mwense.
Kenaka anatenga chikho, nayamika nachipereka kwa iwo nati, “Imwani nonsenu.
28 Iyi emilopa yakame yacipangano iletikilinga bantu bangi kwambeti, balekelelwe bwipishi bwabo.
Awa ndi magazi anga a pangano amene akhetsedwa chifukwa cha ambiri kuti akhululukidwe machimo.
29 Cakubinga, nteti nkanwepo waini umbi, mpaka busuba mbweshi nkanwe waini walinolino pamo ne njamwe mu Bwami bwa Bata.”
Ndikuwuzani kuti sindidzamwanso kuchokera ku chipatso cha mtengo wa mpesa kuyambira lero mpaka tsiku ilo pamene ndidzamwenso mwatsopano ndi inu mu ufumu wa Atate anga.”
30 Panyuma pakwimbila lwimbo lwakutembaula Lesa, bonse balapula, balaya ku mulundu wa maolifi.
Atayimba nyimbo, anatuluka kupita ku phiri la Olivi.
31 Yesu walabambila beshikwiya bakendi kwambeti, “Lelo mashiku mwense nimunkane ne kunshiya ndenka, pakwinga kwalembweti, ‘Ninkashine mwembeshi, kayi litanga lya mbelele nilikapalangane,’
Pamenepo Yesu anawawuza kuti, “Usiku omwe uno inu nonse mudzandithawa, pakuti kwalembedwa: “‘Kantha mʼbusa, ndipo nkhosa zidzabalalika.’
32 Nomba ndakapundushiwa kubafu, njameti nkatangune kuya ku Galileya.”
Koma ndikadzauka, ndidzatsogola kupita ku Galileya.”
33 Nomba Petulo walambeti, “Nambi bonse bamukane ne kumushiya, ame ndenka nteti ndimukanepo pimbi.”
Petro anayankha nati, “Ngakhale onsewa atakuthawani, ine ndekha ayi.”
34 Apo Yesu walamwambila Petulo, “Cakubinga ndakwambilishingeti, lyopele lelo mashiku, kombwe katanalila, obe nunkane tunkanda tutatu, kwambeti nkonjishipo sobwe.”
Yesu anayankha nati, “Zoonadi, ndikukuwuza kuti usiku omwe uno, asanalire tambala, udzandikana Ine katatu.”
35 Nomba Petulo walambeti, “Nambi cambweti mfwe pamo nenjamwe nteti nkamukanepo sobwe.” Nabo beshikwiya bonse balamba cimo cimo.
Koma Petro ananenetsa nati, “Ngakhale kutakhala kufa nanu pamodzi, sindidzakukanani.” Ndipo ophunzira onse ananena chimodzimodzi.
36 Yesu ne beshikwiya bakendi balaya kumusena walikukwiweti, Getisemani, uko nkwalakabambileti, “Kamwikalani pano, ame ndenga uko kuya kupaila.”
Kenaka Yesu anapita ku malo otchedwa Getsemani, ndipo anawawuza kuti, “Khalani pano pamene Ine ndikukapemphera apo.”
37 Walamantako Petulo, ne banabendi Sebedayo babili, Yesu walongumana, ne kupenga mumoyo.
Anatenga Petro ndi ana awiri a Zebedayo, ndipo anayamba kumva chisoni ndi kuvutika mu mtima.
38 Walabambileti, “Mumoyo wakame muli bulanda bunene bwakufwa nabo. Kwamwikalani pano, nomba kamucetukani.”
Pamenepo anawawuza kuti, “Moyo wanga uli ndi chisoni chofa nacho. Khalani pano ndipo dikirani pamodzi ndi Ine.”
39 Yesu walaya pantangu ntamwa pang'ana, walawa kali wakotamika cinso cakendi panshi ne kutatika kupaila, walambeti, “Ta, na kacikonsheka, mufunye nkomeshi yamapensho iyi. Nsombi kakutaba kuyanda kwakame sobwe, nsombi kube kuyanda kwenu.”
Atapita patsogolo pangʼono, anagwa pansi chafufumimba napemphera kuti, “Atate anga, ngati ndikotheka, chikho ichi chichotsedwe kwa Ine. Koma osati monga mmene ndifunira, koma monga mufunira Inu.”
40 Mpwalambeco, Yesu walabwelela kwalikuba beshikwiya basa, walabacana kabali bona tulo, neco walamwipusha Petulo, “Inga mulalilwaconi kupembelela pamo ne njame kwa kacindi kang'anowa.
Kenaka anabwera kwa ophunzira ake nawapeza ali mtulo. Iye anafunsa Petro kuti, “Kodi anthu inu, simukanakhala maso pamodzi ndi Ine kwa ora limodzi lokha?
41 Kumucetukani kayi kamupailani kwambeti kamutawila mu masunko. Walo moyo ulayandishishinga, nsombi mubili ulalefuku.”
Khalani maso ndi kupemphera kuti musagwe mʼmayesero. Mzimu ukufuna koma thupi ndi lofowoka.”
42 Kayi Yesu walabashiya nekuya kankanda katubili kuya kupaila kambeti, “Ta, na nkomeshi ya mapensho iyi, nkayelela kumpitilila mpaka nwamo, naco caina, kuyanda kwinshike.”
Anachokanso nakapemphera kachiwiri kuti, “Atate anga, ngati chikhochi sichingandichoke, mpaka nditamwa, kufuna kwanu kuchitike.”
43 Mpwalabwelako kayi walabacana kabali bona tulo, pakwinga bikope byabo byalalema ne tulo.
Atabweranso anawapeza ali mtulo chifukwa zikope zawo zinalemedwa ndi tulo.
44 Kayi Yesu walabashiya walaya kupaila katunkanda tutatu, kamba maswi amo amo.
Choncho anawasiya napitanso kukapemphera kachitatu nanenanso chimodzimodzi.
45 Panyuma pakendi, walesa kuli beshikwiya bakendi basa ne kwambeti, “Ne lino mucili monatulo, ne kupumwina ‘Cindi cilashiki,’ Mwana Muntu nabikwe mu makasa abantu baipa.”
Kenaka anabwera kwa ophunzira ake nati kwa iwo, “Kodi mukanagonabe ndi kupumula? Taonani, ora layandikira ndipo Mwana wa Munthu akuperekedwa mʼmanja mwa ochimwa.
46 “Pundukani! Tiyeni! Nte uyu shikungulisha lashiki!”
Imirirani, tiyeni tizipita! Wondipereka Ine wafika!”
47 Yesu kacamba, Yuda Sikalyote, umo wa beshikwiya likumi ne babili walashika ne likoto lyabantu kabali bamanta bibeshi ne mingwala. Bamakulene beshimilumbo, ne bamakulene ba Bayuda ebalabatuma aba bantu.
Akuyankhula choncho, Yudasi mmodzi mwa khumi ndi awiriwo anafika. Pamodzi ndi iye panali gulu lalikulu la anthu ali ndi mikondo ndi zibonga otumidwa ndi akulu a ansembe ndi akuluakulu.
48 Shikumulisha wali kalilabambili kendi cishibisho, kwambeti, “Uyo ngweshi nshonshonte, endiye ngomulayandanga, mumwikate!”
Womuperekayo anawawuziratu chizindikiro anthuwo kuti, “Amene ndidzapsompsona ndi iyeyo; mugwireni.”
49 Yuda Sikalyote walalulama palikuba Yesu ne kwambeti, Mitende Bashikwiyisha! Mpwalambeco walamushonshonta.
Pamenepo Yudasi anapita kwa Yesu nati, “Moni, Aphunzitsi!” Ndipo anapsompsona Iye.
50 Yesu walamwambileti, “Obe ndo fwambana kwinsa ncoleshili.” Popelapo basa bantu Yesu balamutanya ne kumusunga.
Yesu anayankha kuti, “Bwenzi langa, chita chimene wabwerera.” Pamenepo anthuwo anabwera patsogolo namugwira Yesu ndi kumumanga.
51 Nomba kamubonani! umo walikuba pamo ne Yesu walapulisha cibeshi, ne kumutimbula litwi musebenshi wa Shimilumbo mukulene.
Pa chifukwa ichi, mmodzi wa anzake a Yesu anagwira lupanga lake, nalisolola ndi kutema wantchito wa mkulu wa ansembe, nadula khutu lake.
52 Nomba Yesu walamwambileti, “Bwesha cibeshico mucikwama, pakwinga bonse balasebenseshenga bibeshi, nibakafwe ku bibeshi,”
Yesu anati kwa iye, “Bwezera lupanga lako mʼchimake, chifukwa onse amene amapha ndi lupanga adzafa ndi lupanga.
53 Sena ulayeyengeti nkandelela kukuwa ne kusenga Bata, balo pacindi copele cino ngabantumina bangelo bankondo bapita makoto likumi ne abili.
Kodi mukuganiza kuti sindingathe kupempha Atate anga ndipo nthawi yomweyo nʼkundipatsa magulu a angelo oposa khumi ndi awiri?
54 Na ame nyinseco, ngabinshikeconi byalambwa mu Mabala kwambeti byelela kwinshika.
Koma nanga malemba akwaniritsidwa bwanji amene akuti ziyenera kuchitika motere?”
55 Popelapo, bantu basa Yesu walabepusheti, “Nipacebo cini mulaletelele bibeshi ne mingwala, pakunjikata eti njame kapondo? Masuba onse ndekalanga nenu mu Ng'anda ya Lesa kanjiyisha.”
Pa nthawi yomweyo Yesu anati kwa gululo, “Kodi ndine mtsogoleri wa anthu owukira kuti mwabwera ndi malupanga ndi zibonga kudzandigwira? Tsiku ndi tsiku ndimakhala mʼNyumba ya Mulungu kuphunzitsa, koma simunandigwire.
56 “Nomba ibi byonse bilenshiki kwambeti mbyobalalemba bashinshimi mu Mabala bikwanilishiwe.” Popelapo beshikwiya bakendi bonse balafwamba, ne kumushiya Yesu enka.
Koma zonsezi zachitika kuti zolembedwa ndi aneneri zikwaniritsidwe.” Pamenepo ophunzira anamusiya nathawa.
57 Bantu basa mpobalamwikata Yesu, balamutwala ku ng'anda ya Kayafa Mukulene wa beshimilumbo bonse, uko nkobalabungana beshikwiyisha Milawo ya Mose, ne bamakulene ba Bayuda.
Iwo amene anamugwira Yesu anamutengera kwa Kayafa, mkulu wa ansembe, kumene aphunzitsi amalamulo ndi akuluakulu anasonkhana.
58 Petulo, walikakonka panyuma capataliko, mpaka walakengila mukati mulubuwa lwa ng'anda ya Mukulene wa beshimilumbo usa. Walengila mukati ne kuya kwikala pamo ne bamalonda baku Ng'anda ya Lesa, kwambeti abone ceti cinshike.
Koma Petro anamutsatira Iye patali, mpaka ku bwalo la mkulu wa ansembe. Analowa nakhala pansi pamodzi ndi alonda kuti aone zotsatira.
59 Beshimilumbo bamakulene, ne bonse bamu Nkuta inene ya Bayuda, bali kulangaula bakamboni bela kumubepeshela Yesu kwambeti bamushine.
Akulu a ansembe ndi akulu olamulira Ayuda amafunafuna umboni wonama wofuna kuphera Yesu.
60 Nikukabeti palesa bakamboni bangi bela kumubepeshela, nsombi baliya kucanapo bukamboni bwancinencine mbobalikulangaula. Kumapwililisho kwalesa bantu babili,
Koma sanathe kupeza uliwonse, angakhale kuti mboni zambiri zabodza zinapezeka. Pomalizira mboni ziwiri zinabwera patsogolo.
61 balambeti, “Muntuyu walikwambeti, ame ndelela kumwaya Ng'anda ya Lesa, ne kuyibaka kayi mu masuba atatu owa.”
Ndipo zinati, “Munthu uyu anati, ‘Ndikhoza kupasula Nyumba ya Mulungu ndi kuyimanganso mʼmasiku atatu.’”
62 Lino Mukulene wa beshimilumbo bonse walemana ne kumwipusha Yesu. “Sena uliya cakukumbulapo pa bintu ibi mbyobalakubepeshenga aba bantu?”
Pamenepo mkulu wa ansembe anayimirira nati kwa Yesu, “Kodi suyankha? Kodi umboni umenewu ndi otani umene anthu awa akupereka kukutsutsa Iwe?”
63 Nomba Yesu nendi walamwenowa tonto. Kayi Mukulene wa beshimilumbo bonse usa walambila Yesu, “Ndakwambilinga mu Lina lya Lesa muyumi, kwambeti winse kulumbila pakwamba na njobe Klistu, Mwanendi Lesa.”
Koma Yesu anakhalabe chete. Mkulu wa ansembe anati kwa Iye, “Ndikulamulira Iwe ndi lumbiro pamaso pa Mulungu wa Moyo: utiwuze ife ngati ndiwe Khristu Mwana wa Mulungu.”
64 Yesu walamukumbuleti, “Mulamba mobene, nsombi ndamwambilishingeti, ‘kufuma cino cindi nimukabone Mwana Muntu kaliwekala kucikasa calulyo ca Lesa wangofu shonse,’ Nimukamubone kesa mwilu mumakumbi.”
Yesu anayankha nati, “Mwanena ndinu. Koma ndikunena kwa inu nonse: mʼtsogolomo mudzaona Mwana wa Munthu atakhala kudzanja lamanja la Wamphamvuzonse ndipo akubwera ndi mitambo ya kumwamba.”
65 Mukulene wa beshimilumbobonse walatwamuna munganjo wakendi kulesha bukalu ne kwambeti, “Uku ni kumunyansha Lesa ‘Sena paciyandika bakamboni nabambi’ Mulalinyumfwili mobene ncalamunyansha Lesa.”
Pamenepo mkulu wa ansembe anangʼamba zovala zake nati, “Wanyoza Mulungu! Tifuniranji mboni zina? Taonani, tsopano mwamva mwano wake.
66 “Neco mulayeyengapongeconi?” Balo balakumbuleti, “Lacaniki ne mulandu, welela kushinwa!”
Mukuganiza bwanji?” Iwo anayankha kuti, “Ayenera kuphedwa!”
67 Popelapo balatatika kumusankila mata kumenso ne kumuma mpaka, nabambi balatatika kumuma makofi,
Kenaka anamulavulira kumaso namumenya ndi zibakera. Ena anamumenya makofi.
68 kabambeti, “Obe Klistu, Kolotela, inga lakumu niyani?”
Ndipo anati, “Tanenera kwa ife, Khristu. Wakumenya ndani?”
69 Petulo walakekala mulubuwa kunsa kwa ng'anda. Mutukashi musebenshi wa Mukulene wa beshimilumbo walesa kulyendiye ne kwambeti, “Ne njamwe mwalikwenda pamo ne Yesuyu waku Galileya.”
Tsopano Petro anakhala ku bwalo la nyumbayo, ndipo mtsikana wantchito anabwera kwa iye nati, “Iwenso unali ndi Yesu wa ku Galileya.”
70 Nsombi nendi walakana pamenso abantu bonse, walambeti, “Ncolambanga ame nkandicishipo sobwe!”
Koma iye anakana pamaso pawo nati, “Sindikudziwa chimene ukunena.”
71 Petulo mpwalikupula kaya pacishinga, kayi mutukashi naumbi musebenshi walamubona, walatatika kwambila nabambi balikubapo. “Uyu muntu walikuba pamo ne Yesu waku Nasaleti.”
Kenaka anachoka kupita ku khomo la mpanda, kumene mtsikana wina anamuonanso nawuza anthu nati, “Munthu uyu anali ndi Yesu wa ku Nazareti.”
72 Petulo walakana, cakwinsa kulumbileti, “Cakubinga ame nkandimwishipo muntuyo.”
Iye anakananso molumbira kuti, “Sindimudziwa munthuyu!”
73 Mpopalapitako kacindi kang'ana, bantu balikubapo balamwambila Petulo, “Kwelana ne ntaka ya ng'ambilo yakobe tuleshibinga kwambeti ne njobe owa mulikoto ili.”
Patapita kanthawi pangʼono, amene anayimirira pamenepo anapita kwa Petro nati, “Zoonadi, ndiwe mmodzi wa iwo, popeza mayankhulidwe ako akukuwulula.”
74 Apo Petulo walensa kulumbileti, “Lesa anshingane ne kumpa cisubulo, na ndambanga bwepeshi, ame muntuyu nkandimwishipo sobwe.” Cindi copeleco kombwe walalila.
Pamenepo anayamba kudzitemberera ndipo analumbira kwa iwo nati, “Sindimudziwa munthu ameneyo!” Nthawi yomweyo tambala analira.
75 Petulo walanuka maswi ngalamwambila Yesu akwambeti, “Kombwe katanalila nukankane tunkanda tutatu kwambeti nkonjishipo sobwe.” Popelapo Petulo walapula kayakulila ne kushinshimuka.
Ndipo Petro anakumbukira mawu amene Yesu anayankhula kuti, “Tambala asanalire, udzandikana Ine katatu.” Ndipo anatuluka panja nakalira kwambiri.