< Zaharija 7 >

1 Pripetilo se je v četrtem letu kralja Dareja, da je Gospodova beseda prišla Zahariju na četrti dan devetega meseca, torej v kislévu,
Pa chaka chachinayi cha Mfumu Dariyo, pa tsiku lachinayi la Kisilevi, mwezi wachisanu ndi chinayi, Yehova anayankhula ndi Zekariya.
2 ko so poslali v Božjo hišo Sarécerja in Regem Meleha in njune može, da molijo pred Gospodom
Anthu a ku Beteli anali atatuma Sarezeri ndi Regemu-Meleki pamodzi ndi anthu awo, kuti akapemphe chifundo kwa Yehova
3 in da govorijo duhovnikom, ki so bili v hiši Gospoda nad bojevniki in prerokom, rekoč: »Ali naj bi jokal v petem mesecu in se zadrževal, kot sem to počel ta mnoga leta?«
pokafunsa kwa ansembe a ku Nyumba ya Yehova Wamphamvuzonse ndi aneneri kuti, “Kodi ine ndizilira ndi kusala zakudya pa mwezi wachisanu, monga mmene ndakhala ndikuchitira pa zaka zambiri?”
4 Potem je prišla k meni beseda Gospoda nad bojevniki, rekoč:
Pamenepo Yehova Wamphamvuzonse anayankhula nane kuti,
5 »Govori vsemu ljudstvu dežele in duhovnikom, rekoč: ›Ko ste se postili in žalovali v petem in sedmem mesecu, celo teh sedemdeset let, ali ste se sploh postili meni, celó zame?
“Funsa anthu onse a mʼdziko ndi ansembe kuti, ‘Pamene munkasala zakudya pa mwezi wachisanu ndi wachisanu ndi chiwiri pa zaka 70 zapitazi, kodi munkasala chifukwa cha Ine?
6 In ko ste jedli in ko ste pili, mar niste jedli zase in pili zase?
Ndipo pamene munkadya ndi kumwa, kodi simunkachita zimenezi podzisangalatsa nokha?
7 Mar naj ne bi slišali besed, ki jih je Gospod klical po prejšnjih prerokih, ko je bil Jeruzalem naseljen in v uspevanju in njegova mesta okoli njega, ko so ljudje naseljevali jug in ravnino?‹«
Kodi awa si mawu amene Yehova ankanena kudzera mwa aneneri oyamba aja pamene Yerusalemu ndi mizinda yake yozungulira anali pa mtendere ndi pa ulemerero, ndi pamene Negevi ndi ku madera akumadzulo a mʼmbali mwa phiri munali anthu?’”
8 Gospodova beseda je prišla Zahariju, rekoč:
Ndipo Yehova anayankhulanso ndi Zekariya kuti,
9 »Tako govori Gospod nad bojevniki, rekoč: ›Izvajajte resnično sodbo in izkazujte usmiljenje in sočutja vsakdo svojemu bratu,
“Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Muziweruza molungama; muzichitirana chifundo ndi kumverana chisoni.
10 in ne stiskajte vdove, niti osirotelega, niti tujca, niti revnega, in naj si nihče izmed vas v svojem srcu ne domišlja zla zoper svojega brata.
Musamazunze akazi amasiye kapena ana amasiye, alendo kapena osauka. Musamaganizirane zoyipa mʼmitima mwanu.’
11 Toda zavrnili so, da bi prisluhnili in odmaknili so ramo in si zamašili svoja ušesa, da ne bi slišali.
“Koma makolo anu anakana kumvera uthenga umenewu; anawumitsa mtima nandifulatira, natseka makutu awo kuti asamve.
12 Da, svoja srca so naredili kakor diamantni kamen, da ne bi slišali postave in besed, ki jih je Gospod nad bojevniki poslal po svojem duhu po prejšnjih prerokih, zato je prišel velik bes od Gospoda nad bojevniki.
Anawumitsa mitima yawo ngati mwala wa sangalabwi ndipo sanamvere lamulo kapena mawu amene Yehova Wamphamvuzonse anawatumiza mwa Mzimu wake kudzera mwa aneneri oyamba aja. Kotero Yehova Wamphamvuzonse anakwiya kwambiri.
13 Zato se je zgodilo, da kakor je on klical in niso hoteli slišati, tako so klicali in nisem hotel slišati, « govori Gospod nad bojevniki,
“‘Pamene ndinawayitana, iwo sanamvere; choncho pamene iwo anandiyitana, Ine sindinamverenso,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
14 »temveč sem jih z vrtinčastim vetrom razkropil med vse narode, ki jih niso poznali. Tako je bila dežela za njimi zapuščena, da noben človek ni šel skoznjo niti se ni vrnil, kajti prijetno deželo so spremenili v opustošeno.«
‘Ndinawamwaza ndi kamvuluvulu pakati pa mitundu yonse ya anthu, kumene anali alendo. Dziko lawo linatsala litasakazidwa kwambiri kotero kuti palibe amene amabwera kapena kupitamo. Umu ndi mmene anasandutsira dziko labwino kukhala chipululu.’”

< Zaharija 7 >