< Psalmi 96 >
1 Oh pojte Gospodu novo pesem, pojte Gospodu, vsa zemlja.
Imbirani Yehova nyimbo yatsopano; Imbirani Yehova dziko lonse lapansi.
2 Prepevajte Gospodu, blagoslavljajte njegovo ime; iz dneva v dan naznanjajte njegovo rešitev duš.
Imbirani Yehova, tamandani dzina lake; lalikirani chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.
3 Oznanjajte njegovo slavo med pogani, njegove čudeže med vsemi ljudstvi.
Lengezani ulemerero wake pakati pa mayiko, ntchito zake zodabwitsa pakati pa mitundu yonse ya anthu.
4 Kajti Gospod je velik in silno bodi hvaljen; njega se je treba bati nad vsemi bogovi.
Pakuti wamkulu ndi Yehova ndipo ndi woyenera kwambiri kumutamanda; ayenera kuopedwa kupambana milungu yonse.
5 Kajti vsi bogovi narodov so maliki, toda Gospod je naredil nebo.
Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano, koma Yehova analenga mayiko akumwamba.
6 Čast in veličanstvo sta pred njim; moč in lepota sta v njegovem svetišču.
Ulemu ndi ufumu zili pamaso pake, mphamvu ndi ulemerero zili mʼmalo ake opatulika.
7 Dajajte Gospodu, oh sorodstva ljudstev, dajajte Gospodu slavo in moč.
Perekani kwa Yehova, inu mabanja a anthu a mitundu ina, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
8 Dajajte Gospodu slavo, primerno njegovemu imenu; prinesite daritev in pridite v njegove dvore.
Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake; bweretsani chopereka ndipo mulowe mʼmabwalo ake.
9 Oh obožujte Gospoda v lepoti svetosti. Trepetaj pred njim, vsa zemlja!
Lambirani Yehova mu ulemerero wa chiyero chake; njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi.
10 Govorite med pogani, da Gospod kraljuje. Tudi zemeljski [krog] bo utrjen, da ne bo omajan. Ljudstva bo sodil pravično.
Nenani pakati pa mitundu ya anthu, “Yehova akulamulira.” Dziko lonse lakhazikika molimba, silingasunthidwe; Iye adzaweruza mitundu ya anthu molungama.
11 Naj se nebo veseli in naj bo zemlja vesela; naj morje buči in njegova polnost.
Mayiko akumwamba asangalale, dziko lapansi likondwere; nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo;
12 Naj bo polje radostno in vse, kar je tam. Potem se bodo vsa gozdna drevesa veselila
minda ikondwere pamodzi ndi chilichonse chili mʼmenemo. Pamenepo mitengo yonse ya mʼnkhalango idzayimba ndi chimwemwe;
13 pred Gospodom, kajti on prihaja, kajti on prihaja, da sodi zemljo. S pravičnostjo bo sodil zemeljski [krog] in ljudstva s svojo resnico.
idzayimba pamaso pa Yehova, pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi; adzaweruza dziko lonse mwachilungamo ndi mitundu ya anthu onse mʼchoonadi.