< Psalmi 39 >

1 Rekel sem: »Pazil bom na svoje poti, da ne bom grešil s svojim jezikom. Ko bo zlobni pred menoj, bom svoja usta držal z uzdo.«
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kwa Yedutuni. Salimo la Davide. Ndinati, “Ndidzasamalira njira zanga ndipo ndidzasunga lilime langa kuti ndisachimwe; ndidzatseka pakamwa panga ndi chitsekerero nthawi yonse imene woyipa ali pamaso panga.”
2 Bil sem nem s tišino, molčal sem, celó pred dobrim in moja bridkost je bila razvneta.
Koma pamene ndinali chete osanena ngakhale kanthu kalikonse kabwino mavuto anga anachulukirabe.
3 Moje srce je bilo vroče znotraj mene, medtem ko sem razglabljal, je zagorel ogenj, potem sem spregovoril s svojim jezikom:
Mtima wanga unatentha mʼkati mwanga, ndipo pamene ndinkalingalira, moto unayaka; kenaka ndinayankhula ndi lilime langa:
4 » Gospod, daj mi spoznati moj konec in mero mojih dni, kolikšna je, da lahko spoznam, kako slaboten sem.
“Yehova ndionetseni mathero a moyo wanga ndi chiwerengero cha masiku anga; mundidziwitse kuti moyo wanga ndi wosakhalitsa motani.
5 Glej, moje dneve si naredil kakor dlan in moja starost je kakor nič pred teboj. Resnično, vsak človek v svojem najboljšem stanju je povsem ničevost.« (Sela)
Inu mwachititsa kuti masiku anga akhale ochepa kwambiri, kutalika kwa zaka zanga ndi kopanda phindu pamaso panu; moyo wa munthu aliyense ndi waufupi. (Sela)
6 Zagotovo vsak človek hodi v prazni podobi, zagotovo so zaman vznemirjeni. Kopiči bogastva, pa ne ve, kdo jih bo pobral.
Munthu ali ngati chithunzithunzi chake pamene akuyenda uku ndi uku: Iye amangovutika koma popanda phindu; amadzikundikira chuma, osadziwa kuti chidzakhala chayani.
7 In sedaj, Gospod, kaj [naj] pričakujem? Moje upanje je v tebi.
“Koma tsopano Ambuye kodi ndifunanso chiyani? Chiyembekezo changa chili mwa Inu.
8 Osvobodi me pred vsemi mojimi prestopki. Ne naredi me [za] grajo nespametnim.
Pulumutseni ku zolakwa zanga zonse; musandisandutse chonyozeka kwa opusa.
9 Bil sem nem, svojih ust nisem odprl, ker si ti to storil.
Ine ndinali chete; sindinatsekule pakamwa panga pakuti Inu ndinu amene mwachita zimenezi.
10 Umakni svoj udarec proč od mene. Použit sem z zamahom tvoje roke.
Chotsani mkwapulo wanu pa ine; ndagonjetsedwa ndi nkhonya ya dzanja lanu.
11 Kadar za krivičnost z grajanjem korigiraš človeka, storiš, da njegova lepota shira kakor molj. Zagotovo je vsak človek ničevost. (Sela)
Inu mumadzudzula ndi kulanga anthu chifukwa cha tchimo lawo; mumawononga chuma chawo monga njenjete; munthu aliyense ali ngati mpweya. (Sela)
12 Usliši mojo molitev, oh Gospod in pazljivo prisluhni mojemu vpitju; ob mojih solzah ne molči. Kajti jaz sem tujec s teboj in začasni prebivalec, kakor so bili vsi moji očetje.
“Imvani pemphero langa Inu Yehova, mverani kulira kwanga kopempha thandizo; musakhale chete pamene ndikulirira kwa Inu, popeza ndine mlendo wanu wosakhalitsa; monga anachitira makolo anga onse.
13 Oh prizanesi mi, da lahko obnovim moč, preden grem naprej in ne bom več.
Musandiyangʼane mwaukali, choncho ndidzatha kusangalala ndisanafe ndi kuyiwalika.”

< Psalmi 39 >