< Psalmi 32 >
1 Blagoslovljen je tisti, čigar prestopek je oproščen, čigar greh je pokrit.
Salimo la Davide. Malangizo. Ngodala munthu amene zolakwa zake zakhululukidwa; amene machimo ake aphimbidwa.
2 Blagoslovljen je človek, ki mu Gospod ne pripisuje krivičnosti in v čigar duhu ni zvijače.
Ngodala munthu amene machimo ake Yehova sawawerengeranso pa iye ndipo mu mzimu mwake mulibe chinyengo.
3 Ko sem molčal, so se moje kosti postarale zaradi mojega kričanja ves dan.
Pamene ndinali chete, mafupa anga anakalamba chifukwa cha kubuwula kwanga tsiku lonse.
4 Kajti dan in noč je bila tvoja roka težka nad menoj. Moja vlažnost je obrnjena v poletno sušo. (Sela)
Pakuti usana ndi usiku dzanja lanu linandipsinja; mphamvu zanga zinatha monga nthawi yotentha yachilimwe. (Sela)
5 Priznal sem ti svoj greh in svoje krivičnosti nisem prikrival. Rekel sem: »Svoje prestopke bom priznal Gospodu, « in ti odpuščaš krivičnost mojega greha. (Sela)
Kotero ine ndinavomereza tchimo langa kwa Inu, sindinabise mphulupulu zanga. Ndinati, “Ine ndidzawulula zolakwa zanga kwa Yehova, ndipo Inu munandikhululukira mlandu wa machimo anga.” (Sela)
6 Kajti tako bo k tebi molil vsak, kdor je bogaboječ, v času, ko se daješ najti. Zagotovo mu v poplavah velikih vodá oni ne bodo prišli blizu.
Choncho aliyense okhulupirika apemphere kwa Inuyo pomwe mukupezeka; ndithu pamene madzi amphamvu auka, sadzamupeza.
7 Ti si moje skrivališče, ohranil me boš pred stisko, naokoli me boš obdal s pesmimi osvoboditve. (Sela)
Inu ndi malo anga obisala; muzinditeteza ku mavuto ndipo muzindizinga ndi nyimbo zachipulumutso. (Sela)
8 Poučil te bom in te učil na poti, po kateri boš šel. Usmerjal te bom s svojim očesom.
Ndidzakulangiza ndi kukuphunzitsa njira imene udzayendamo; ndidzakupatsa uphungu ndi kukuyangʼanira.
9 Ne bodite kakor konj ali kakor mula, ki nimata razumevanja, čigar gobca se mora držati z žvalo in uzdo, da se ti ne približata.
Usakhale ngati kavalo kapena bulu, zimene zilibe nzeru, koma ziyenera kuwongoleredwa ndi zitsulo za mʼkamwa ndi pamutu, ukapanda kutero sizibwera kwa iwe.
10 Mnoge bridkosti bodo zlobnemu, toda kdor zaupa v Gospoda, ga bo obdajalo usmiljenje.
Zowawa ndi zambiri za anthu oyipa koma chikondi chosatha cha Yehova chimamuzinga munthu amene amadalira Iye.
11 Bodite veseli v Gospodu in veselite se, vi pravični. Vzklikajte od veselja vsi vi, ki ste iskreni v srcu.
Kondwerani mwa Yehova inu olungama; imbani, inu nonse amene muli owongoka mtima!