< Psalmi 27 >

1 Gospod je moja svetloba in rešitev moje duše, koga bi se bal? Gospod je moč mojega življenja; pred kom bom prestrašen?
Salimo la Davide. Yehova ndiye kuwunika kwanga ndi chipulumutso changa; ndidzaopa yani? Yehova ndi linga la moyo wanga; ndidzachita mantha ndi yani?
2 Kadar so prišli nadme zlobni, celó moji sovražniki in moji nasprotniki, da požro moje meso, so se spotaknili in padli.
Pamene anthu oyipa abwera kudzalimbana nane kudzadya mnofu wanga, pamene adani anga ndi achiwembu andithira nkhondo, iwo adzapunthwa ndi kugwa.
3 Čeprav bi se zoper mene utaborila vojska, se moje srce ne bo balo. Četudi bi se zoper mene dvignila vojna, bom jaz pri tem zaupljiv.
Ngakhale gulu lankhondo lindizinge, mtima wanga sudzaopa. Ngakhale nkhondo itayambika kulimbana nane, ngakhale nthawi imeneyo, ine ndidzalimbika mtima.
4 Eno stvar sem želel od Gospoda, to hočem doseči, da bom lahko prebival v Gospodovi hiši vse dni svojega življenja, da zrem Gospodovo lepoto in da poizvedujem v njegovem templju.
Chinthu chimodzi chokha chimene ndipempha kwa Yehova, ichi ndi chimene ndidzachifunafuna: kuti ndikhale mʼNyumba ya Yehova masiku onse a moyo wanga, ndi kuyangʼana kukongola kwa Yehova, ndi kumufunafuna Iye mʼNyumba yake.
5 Kajti v času stiske me bo skril v svojem paviljonu. Skril me bo v skrivnosti svojega šotorskega svetišča, postavil me bo na skalo.
Pakuti pa tsiku la msautso Iye adzanditeteza mʼmalo ake okhalamo; adzandibisa mʼkati mwa Nyumba yake ndi kukhazika ine pamwamba pa thanthwe.
6 Sedaj bo moja glava povzdignjena nad moje sovražnike okoli mene, zato bom v njegovem šotorskem svetišču daroval žrtvovanje radosti; pel bom, da, prepeval bom hvalnice Gospodu.
Kotero mutu wanga udzakwezedwa kuposa adani anga amene andizungulira; pa Nyumba yake ndidzapereka nsembe ndi mfuwu wachimwemwe; ndidzayimba nyimbo kwa Yehova.
7 Poslušaj, oh Gospod, ko kličem s svojim glasom. Tudi nad menoj imej usmiljenje in mi odgovori.
Imvani mawu anga pamene ndiyitana Inu Yehova mundichitire chifundo ndipo mundiyankhe.
8 Ko praviš: »Iščite moje obličje, « ti je moje srce reklo: »Tvoje obličje, Gospod, bom iskal.«
Mtima wanga ukuti kwa Inu, “Funafuna nkhope yake!” Nkhope yanu Yehova ndidzayifunafuna.
9 Ne skrivaj svojega obličja daleč od mene, svojega služabnika ne odslovi v jezi. Bil si moja pomoč; ne zapusti me niti se me ne odpovej, oh Bog rešitve moje duše.
Musandibisire nkhope yanu, musamubweze mtumiki wanu mwamkwiyo; mwakhala muli thandizo langa. Musandikane kapena kunditaya, Inu Mulungu Mpulumutsi wanga.
10 Ko me moj oče in moja mati zapustita, potem me bo Gospod pobral.
Ngakhale abambo ndi amayi anga anditaya Yehova adzandisamala.
11 Úči me svoje poti, oh Gospod in vodi me po ravni stezi, zaradi mojih sovražnikov.
Phunzitseni njira yanu Inu Yehova, munditsogolere mʼnjira yowongoka chifukwa cha ondizunza.
12 Ne izroči me volji mojih sovražnikov, kajti krive priče so vstale zoper mene in takšni, ki izdihujejo krutost.
Musandipereke ku zokhumba za adani anga, pakuti mboni zambiri zauka kutsutsana nane ndipo zikundiopseza.
13 Oslabel sem, razen če sem veroval, da vidim Gospodovo dobroto v deželi živih.
Ine ndikutsimikiza mtima za zimenezi; ndidzaona ubwino wa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
14 Čakaj na Gospoda, bodi odločnega poguma in okrepil bo tvoje srce. Čakaj, pravim, na Gospoda.
Dikirani pa Yehova; khalani anyonga ndipo limbani mtima nimudikire Yehova.

< Psalmi 27 >