< Pregovori 4 >

1 Prisluhnite, vi otroci, poučevanju očeta in pazite, da spoznate razumevanje.
Ananu, mverani malangizo a abambo anu; tcherani khutu kuti mupeze nzeru zodziwira zinthu.
2 Kajti dajem vam dober nauk, ne zapustite moje postave.
Zimene ndikukuphunzitsani ndi zabwino. Choncho musasiye malangizo anga.
3 Kajti jaz sem bil sin svojega očeta, nežen in edini ljubljen v očeh svoje matere.
Paja ndinalinso mwana mʼnyumba mwa abambo anga; mwana mmodzi yekha wapamtima pa amayi anga.
4 Tudi učil me je in mi rekel: »Tvoje srce naj ohrani moje besede. Drži se mojih zapovedi in živi.
Ndipo abambo anandiphunzitsa ndi mawu akuti, “Ugwiritse mawu anga pa mtima pako, usunge malamulo anga kuti ukhale ndi moyo.
5 Pridobivaj modrost, pridobivaj razumevanje, tega ne pozabi niti se ne nagni od besed iz mojih ust.
Upeze nzeru, upeze nzeru zomvetsa zinthu; usayiwale mawu anga kapena kutayana nawo.
6 Ne zapusti je, pa te bo varovala; ljubi jo, pa te bo čuvala.
Usasiye nzeru ndipo idzakusunga. Uziyikonda ndipo idzakuteteza.
7 Modrost je glavna stvar, zato pridobivaj modrost in z vsem svojim dobičkom pridobivaj razumevanje.
Fundo yayikulu pa za nzeru ndi iyi: upeze nzeru. Kaya pali china chilichonse chimene ungapeze, koma upeze nzeru yomvetsa bwino zinthu.
8 Poveličuj jo, pa te bo povišala, prinesla ti bo čast, ko jo boš objemal.
Uyilemekeze nzeruyo ndipo idzakukweza; ikumbatire nzeruyo ndipo idzakupatsa ulemu.
9 Tvoji glavi bo dala ornament milosti, izročila ti bo krono slave.«
Idzayika sangamutu yokongola yamaluwa pamutu pako; idzakupatsa chipewa chaufumu chaulemu.”
10 Prisluhni, oh moj sin in sprejmi moje izreke in mnogo bo let tvojega življenja.
Mwana wanga, umvere ndi kuvomereza zimene ndikunena, ndipo zaka za moyo wako zidzakhala zochuluka.
11 Učil sem te na poti modrosti, vodil sem te po pravih poteh.
Ndakuphunzitsa njira yake ya nzeru. Ndakutsogolera mʼnjira zolungama.
12 Kadar greš, tvoje stopinje ne bodo utesnjene in kadar tečeš, se ne boš spotaknil.
Pamene ukuyenda, mapazi ako sadzawombana; ukamadzathamanga, sudzapunthwa.
13 Trdno se oprimi poučevanja, naj ona ne odide. Obdrži jo, kajti ona je tvoje življenje.
Ugwiritse zimene ndikukuphunzitsazi osazitaya ayi. Uwasamale bwino pakuti moyo wako wagona pamenepa.
14 Ne stopaj na pot zlobnih in ne hodi po stezi zlobnih ljudi.
Usayende mʼnjira za anthu oyipa kapena kuyenda mʼnjira ya anthu ochimwa.
15 Izogibaj se je, ne hodi mimo nje in obrni se od nje ter pojdi proč.
Pewa njira zawo, usayende mʼmenemo; uzilambalala nʼkumangopita.
16 Kajti oni ne spijo, razen če niso storili vragolije in njihovo spanje je odvzeto, razen če nekomu ne povzročijo, da pade.
Pakuti iwo sagona mpaka atachita zoyipa; tulo salipeza mpaka atapunthwitsa munthu wina.
17 Kajti jedo kruh zlobnosti in pijejo vino nasilja.
Paja chakudya chawo ndicho kuchita zoyipa basi ndipo chakumwa chawo ndi chiwawa.
18 Toda steza pravičnih je kakor svetlikajoča svetloba, ki bolj in bolj sije do popolnega dne.
Koma njira ya anthu olungama ili ngati kuwala kwa mʼbandakucha kumene kumanka kuwalirawalira mpaka dzuwa litafika pa mutu.
19 Pot zlobnih je kakor tema; ne vedo ob kaj se spotaknejo.
Koma njira ya anthu oyipa ili ngati mdima wandiweyani; iwo sadziwa chomwe chimawapunthwitsa.
20 Moj sin, prisluhni mojim besedam, svoje uho nagni k mojim izrekom.
Mwana wanga, mvetsetsa zimene ndikunena; tchera khutu ku mawu anga.
21 Naj le-ti ne odidejo od tvojih oči, obdrži jih v sredi svojega srca.
Usayiwale malangizo angawa, koma uwasunge mu mtima mwako.
22 Kajti življenje so tistim, ki jih najdejo in zdravje vsemu njihovemu mesu.
Pakuti amapatsa moyo kwa aliyense amene awapeza ndipo amachiritsa thupi lake lonse.
23 Svoje srce varuj z vso marljivostjo, kajti iz njega so zadeve življenja.
Ndipotu mtima wako uziwuyangʼanira bwino ndithu pakuti ndiwo magwero a moyo.
24 Kljubovalna usta daj od sebe in sprevržene ustnice odloži daleč stran od sebe.
Usiyiretu kuyankhula zokhotakhota; ndipo ulekeretu kuyankhula zinthu zonyansa.
25 Tvoje oči naj gledajo naravnost in tvoje veke naj gledajo neposredno pred teboj.
Maso ako ayangʼane patsogolo; uziyangʼana kutsogolo molunjika.
26 Preudari stezo svojih stopal in vse tvoje poti naj bodo utrjene.
Uzilingalira bwino kumene kupita mapazi ako ndipo njira zako zonse zidzakhala zosakayikitsa.
27 Ne obrni se ne k desni roki niti ne k levi, svoje stopalo odstrani od zla.
Usapatukire kumanja kapena kumanzere; usapite kumene kuli zoyipa.

< Pregovori 4 >