< Pregovori 3 >
1 Moj sin, ne pozabi moje postave, temveč naj tvoje srce ohrani moje zapovedi,
Mwana wanga, usayiwale malangizo anga, mtima wako usunge malamulo anga.
2 kajti dolžino dni in dolgo življenje in mir bodo dodale k tebi.
Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka ndipo udzakhala pa mtendere.
3 Usmiljenje in resnica naj te ne zapustita; priveži si ju okoli svojega vratu, zapiši si ju na tablico svojega srca,
Makhalidwe ochitira ena chifundo ndi owonetsa kukhulupirika asakuchokere. Uwamangirire mʼkhosi mwako ngati mkanda ndi kuwalemba pa mtima pako.
4 tako boš našel naklonjenost in dobro razumevanje v očeh Boga in človeka.
Ukatero udzapeza kuyanja ndi mbiri yabwino pamaso pa Mulungu ndi anthu.
5 Zaupaj v Gospoda z vsem svojim srcem in ne zanašaj se na svoje lastno razumevanje.
Uzikhulupirira Yehova ndi mtima wako wonse ndipo usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.
6 Na vseh svojih poteh ga priznavaj in usmerjal bo tvoje steze.
Pa zochita zako zonse uvomereze kuti Mulungu alipo, ndipo Iye adzawongola njira zako.
7 Ne bodi moder v svojih lastnih očeh. Boj se Gospoda in odidi od zla.
Usamadzione ngati wa nzeru. Uziopa Yehova ndi kupewa zoyipa.
8 To bo zdravje tvojemu popku in mozeg tvojim kostem.
Ukatero thupi lako lidzakhala la moyo wabwino ndi mafupa ako adzakhala olimba.
9 Časti Gospoda s svojim imetjem in s prvimi sadovi vsega svojega donosa,
Uzilemekeza Yehova ndi chuma chako chonse; zokolola zonse zoyamba kucha uzilemekeza nazonso Yehova.
10 tako bodo tvoji skednji napolnjeni z obiljem in tvoje stiskalnice bodo izbruhnile z novim vinom.
Ukatero nkhokwe zako zidzadzaza ndi zinthu zambiri, ndiponso mitsuko yako idzadzaza ndi vinyo.
11 Moj sin, ne preziraj Gospodovega karanja niti ne bodi naveličan njegovega grajanja.
Mwana wanga usanyoze malangizo a Yehova, ndipo usayipidwe ndi chidzudzulo chake.
12 Kajti katerega Gospod ljubi, on graja, celo kakor oče sina, v katerem se razveseljuje.
Paja Yehova amadzudzula amene amamukonda, monga abambo achitira mwana amene amakondwera naye.
13 Srečen je človek, ki odkriva modrost in človek, ki pridobiva razumevanje.
Wodala munthu amene wapeza nzeru, munthu amene walandira nzeru zomvetsa zinthu,
14 Kajti njeno trgovsko blago je boljše kakor trgovsko blago iz srebra in njen dobiček boljši od čistega zlata.
pakuti phindu la nzeru ndi labwino kuposa la siliva, phindu lakelo ndi labwino kuposanso golide.
15 Dragocenejša je od rubinov, in vse stvari, ki si jih lahko želiš, se ne morejo primerjati z njo.
Nzeru ndi yoposa miyala yamtengowapatali; ndipo zonse zimene umazikhumba sizingafanane ndi nzeru.
16 Dolžina dni je v njeni desnici in v njeni levici bogastva in čast.
Mʼdzanja lake lamanja muli moyo wautali; mʼdzanja lake lamanzere muli chuma ndi ulemu.
17 Njene poti so poti prijetnosti in vse njene steze so mir.
Njira zake ndi njira zosangalatsa, ndipo mu njira zake zonse muli mtendere.
18 Je drevo življenja tistim, ki se je oprimejo in srečen je vsak, ki jo ohranja.
Nzeru ili ngati mtengo wopatsa moyo kwa oyigwiritsitsa; wodala munthu amene amayigwiritsa kwambiri.
19 Gospod je z modrostjo utemeljil zemljo, z razumevanjem je utrdil nebo.
Yehova anakhazikitsa dziko lapansi pogwiritsa ntchito nzeru. Anagwiritsanso ntchito nzeru zakudziwa bwino zinthu pamene ankakhazikitsa zakumwamba.
20 Z njegovim spoznanjem so izbruhnile globine in oblaki kapljajo roso.
Mwa nzeru zake Yehova anatumphutsa madzi kuchokera mʼnthaka ndiponso mitambo inagwetsa mvula.
21 Moj sin, naj ti dve ne odideta od tvojih oči; ohrani zdravo modrost in preudarnost,
Mwana wanga usunge nzeru yeniyeni ndi khalidwe lomalingarira zinthu bwino. Zimenezi zisakuchokere.
22 tako bosta življenje tvoji duši in milost tvojemu vratu.
Zimenezi zidzakupatsa moyo, moyo wake wosangalatsa ndi wabwino ngati mkanda wa mʼkhosi.
23 Potem boš na svoji stezi hodil varno in tvoje stopalo se ne bo spotikalo.
Choncho udzayenda pa njira yako mosaopa kanthu, ndipo phazi lako silidzapunthwa;
24 Ko se uležeš, ne boš prestrašen; da, ulegel se boš in tvoje spanje bo sladko.
pamene ugona pansi, sudzachita mantha; ukadzagona pansi tulo tako tidzakhala tokoma.
25 Ne bodi prestrašen od nenadnega strahu niti od opustošenja zlobnih, kadar to prihaja.
Usaope tsoka lobwera mwadzidzidzi kapena chiwonongeko chimene chidzagwera anthu oyipa,
26 Kajti Gospod bo tvoje zaupanje in tvoja stopala bo varoval pred odvzemom.
pakuti Yehova adzakulimbitsa mtima ndipo adzasunga phazi lako kuti lisakodwe mu msampha.
27 Ne zadržuj dobrega pred tistimi, ki jim je to primerno, kadar je v moči tvoje roke, da to storiš.
Usaleke kuchitira zabwino amene ayenera kulandira zabwino, pamene uli nazo mphamvu zochitira zimenezi.
28 Ne reci svojemu bližnjemu: »Pojdi, ponovno pridi in jutri ti bom dal, « če imaš to pri sebi.
Usanene kwa mnansi wako kuti, “Pita, uchite kubweranso. Ndidzakupatsa mawa” pamene uli nazo tsopano.
29 Ne snuj zla zoper svojega soseda, glede na to, da varno prebiva poleg tebe.
Usamukonzere chiwembu mnansi wako, amene anakhala nawe pafupi mokudalira.
30 Ne prepiraj se brez razloga s človekom, če ti ni ničesar hudega storil.
Usakangane ndi munthu wopanda chifukwa pamene iye sanakuchitire zoyipa.
31 Ne zavidaj zatiralcu in ne izberi nobenih njegovih poti.
Usachite naye nsanje munthu wachiwawa kapena kutsanzira khalidwe lake lililonse.
32 Kajti kljubovalnež je ogabnost Gospodu, toda njegova skrivnost je s pravičnimi.
Pakuti Yehova amanyansidwa ndi munthu woyipa koma amayanjana nawo anthu olungama.
33 Gospodovo prekletstvo je v hiši zlobnega, toda blagoslavlja prebivališče pravičnega.
Yehova amatemberera nyumba ya munthu woyipa, koma amadalitsa nyumba ya anthu olungama.
34 Zagotovo zasmehuje posmehljivce, toda milost daje ponižnim.
Anthu onyoza, Iye amawanyoza, koma amakomera mtima anthu odzichepetsa.
35 Modri bo podedoval slavo, toda napredovanje bedakov bo sramota.
Anthu anzeru adzalandira ulemu, koma zitsiru adzazichititsa manyazi.