< Pregovori 25 >

1 Tudi to so Salomonovi pregovori, ki so jih na čisto prepisali možje Ezekíja, Judovega kralja.
Iyi ndi miyambo inanso ya Solomoni, imene anthu a Hezekiya mfumu ya ku Yuda analemba.
2 Prikrivati stvar je Bogu slava, toda kraljeva čast je, da zadevo preišče.
Ulemerero wa Mulungu uli pa kubisa zinthu; ulemerero wa mafumu uli pa kufufuza zinthuzo.
3 Nebes v višino in zemlje v globino in srce kraljev se ne da raziskati.
Monga momwe kwatalikira kumwamba ndi momwe kulili kuzama kwa dziko lapansi, ndi momwemonso alili maganizo a mfumu kusadziwika kwake.
4 Odstrani žlindro od srebra in izšla bo posoda za zlatarja.
Chotsa zoyipa mʼsiliva ndipo wosula adzapanga naye ziwiya.
5 Odstrani zlobnega izpred kralja, pa bo njegov prestol utrjen v pravičnosti.
Chotsa munthu woyipa pamaso pa mfumu; ndipo ufumu wake udzakhazikika mu chilungamo.
6 Ne postavi se v prisotnost kralja in ne stoj na kraju vélikih ljudi,
Usamadzikuze ukakhala pamaso pa mfumu, ndipo usamakhale pamalo pa anthu apamwamba;
7 kajti bolje je, da ti je rečeno: »Pridi sèm gor, « kakor, da boš postavljen nižje v prisotnosti princa, ki so ga tvoje oči videle.
paja ndi bwino kuti mfumu ichite kukuwuza kuti, “Bwera pamwamba pano,” kulekana ndi kuti ikuchititse manyazi chifukwa cha wina wokuposa. Chimene wachiona ndi maso ako,
8 Ne pojdi naglo naprej, da se pričkaš, sicer ne bi vedel kaj storiti na koncu le-tega, ko te tvoj sosed osramoti.
usafulumire kupita nacho ku bwalo la milandu nanga udzachita chiyani pa mapeto pake ngati mnansi wako adzakuchititsa manyazi?
9 Svojo zadevo razpravljaj s svojim sosedom in skrivnosti ne razkrij drugemu,
Kamba mlandu ndi mnansi wako, koma osawulula chinsinsi cha munthu wina
10 da te ne bi, kdor to sliši, osramotil in se tvoja razvpitost ne odvrne proč.
kuopa kuti wina akamva mawu ako adzakuchititsa manyazi ndipo mbiri yako yoyipa sidzatha.
11 Beseda, primerno izgovorjena, je podobna jabolkom iz zlata na slikah iz srebra.
Mawu amodzi woyankhulidwa moyenera ali ngati zokongoletsera zagolide mʼzotengera zasiliva.
12 Kakor uhan iz zlata in ornament iz čistega zlata, takšen je moder grajavec nad poslušnim ušesom.
Kwa munthu womvetsa bwino, kudzudzula kwa munthu wanzeru kuli ngati ndolo zagolide kapena chodzikongoletsera china cha golide wabwino kwambiri.
13 Kakor hlad snega v času žetve, tako je zvest poslanec tistim, ki so ga poslali, kajti osvežuje dušo svojih gospodarjev.
Wamthenga wodalirika ali ngati madzi ozizira pa nthawi yokolola kwa anthu amene amutuma; iye amaziziritsa mtima bwana wake.
14 Kdorkoli se baha z lažnim darom, je podoben oblakom in vetru brez dežja.
Munthu wonyadira mphatso imene sayipereka ali ngati mitambo ndi mphepo yopanda mvula.
15 Z dolgotrajnim prizanašanjem je princ pregovorjen in blag jezik lomi kost.
Kupirira ndiye kumagonjetsa mfumu, ndipo kufewa mʼkamwa kutha kumafatsitsa munthu wowuma mtima.
16 Si našel med? Jej [ga] toliko, kolikor ti je potrebno, da ne bi bil nasičen z njim in ga izbljuval.
Ngati upeza uchi, ingodya okukwanira, kuopa ungakoledwe nawo ndi kuyamba kusanza.
17 Svoje stopalo umakni od hiše svojega soseda, da se te ne bi naveličal in te tako zasovražil.
Uzipita kamodzikamodzi ku nyumba ya mnzako ukawirikiza kupita, udzadana naye.
18 Človek, ki prinaša krivo pričevanje zoper svojega soseda, je macola, meč in ostra puščica.
Munthu wochitira mnzake umboni wonama, ali ngati chibonga kapena lupanga kapena muvi wakuthwa.
19 Zaupanje v nezvestega človeka v času stiske je podobno zlomljenemu zobu in izpahnjenemu stopalu.
Kudalira munthu wosankhulupirika pa nthawi ya mavuto, kuli ngati dzino lobowoka kapena phazi lolumala.
20 Kakor kdor odvzema obleko v hladnem vremenu in kakor kis na soliter, tak je kdor prepeva pesmi potrtemu srcu.
Kuyimbira nyimbo munthu wachisoni kuli ngati kuvula zovala pa nyengo yozizira kapena kuthira mchere pa chilonda.
21 Če je tvoj sovražnik lačen, mu daj jesti kruha in če je žejen, mu daj piti vode,
Ngati mdani wako ali ndi njala, mupatse chakudya kuti adye; ngati ali ndi ludzu mupatse madzi kuti amwe.
22 kajti kopičil boš ognjeno oglje na njegovo glavo in Gospod te bo nagradil.
Pochita izi, udzamusenzetsa makala a moto pa mutu pake, ndipo Yehova adzakupatsa mphotho.
23 Severni veter odnaša dež; tako jezno obličje počne obrekljivemu jeziku.
Monga momwe mphepo yampoto imabweretsera mvula, chonchonso mjedu umadzetsa mkwiyo.
24 Bolje je prebivati v kotu hišne strehe, kakor s prepirljivo žensko in v prostrani hiši.
Nʼkwabwino kukhala pa ngodya ya denga kuposa kukhala mʼnyumba ndi mkazi wolongolola.
25 Kakor hladne vode žejni duši, takšne so dobre novice iz daljne dežele.
Mthenga wabwino wochokera ku dziko lakutali ali ngati madzi ozizira kwa munthu waludzu.
26 Pravičen človek, padajoč pred zlobnim, je kakor skaljen studenec in pokvarjen izvir.
Munthu wolungama amene amagonjera munthu woyipa ali ngati kasupe wodzaza ndi matope kapena chitsime cha madzi oyipa.
27 Ni dobro jesti veliko medu. Tako za ljudi to ni slava, da iščejo svojo lastno slavo.
Sibwino kudya uchi wambiri, sibwinonso kudzifunira wekha ulemu.
28 Kdor nima prevlade nad svojim lastnim duhom je podoben mestu, ki je porušeno in brez zidov.
Munthu amene samatha kudziretsa ali ngati mzinda umene adani awuthyola ndi kuwusiya wopanda malinga.

< Pregovori 25 >