< Pregovori 10 >
1 Salomonovi pregovori. Moder sin dela očeta srečnega, toda nespameten sin je potrtost svoji materi.
Miyambo ya Solomoni: Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amamvetsa amayi ake chisoni.
2 Zakladi zlobnosti nič ne koristijo, toda pravičnost osvobaja pred smrtjo.
Chuma chochipeza mwachinyengo sichipindulitsa, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
3 Gospod ne bo trpel, da duša pravičnega izstrada, toda odvrže imetje zlobnega.
Yehova salola kuti munthu wolungama azikhala ndi njala; koma amalepheretsa zokhumba za anthu oyipa.
4 Reven postaja tisti, ki ravna s počasno roko, toda roka marljivega dela bogastvo.
Wochita zinthu mwaulesi amasauka, koma wogwira ntchito mwakhama amalemera.
5 Kdor zbira poleti, je moder sin, toda kdor ob žetvi spi, je sin, ki povzroča sramoto.
Amene amakolola nthawi yachilimwe ndi mwana wanzeru, koma amene amangogona nthawi yokolola ndi mwana wochititsa manyazi.
6 Blagoslovi so na glavi pravičnega, toda nasilje pokriva usta zlobnega.
Madalitso amakhala pa mutu wa munthu wolungama, koma pakamwa pa munthu woyipa pamaphimba chiwawa.
7 Spomin na pravičnega je blagoslovljen, toda ime zlobnega bo strohnelo.
Munthu wolungama anzake adzamukumbukira ngati mdalitso, koma dzina la munthu woyipa lidzayiwalika.
8 Moder v srcu bo sprejel zapovedi, toda žlobudrav bedak bo padel.
Munthu wa mtima wanzeru amasamala malamulo, koma chitsiru chomangolongolola chidzawonongeka.
9 Kdor hodi pošteno, hodi varno; toda kdor svoje poti izkrivlja, bo razpoznan.
Munthu woyenda mwangwiro amayenda mosatekeseka; koma amene amayenda njira yokhotakhota adzadziwika.
10 Kdor zavija z očesom, povzroča bridkost, toda žlobudrav bedak bo padel.
Aliyense wotsinzinira maso mwachinyengo amabweretsa mavuto, koma wodzudzula chitsiru molimba mtima amabweretsa mtendere.
11 Usta pravičnega človeka so izvir življenja, toda nasilje pokriva usta zlobnega.
Pakamwa pa munthu wolungama ndi kasupe wamoyo, koma pakamwa pa munthu woyipa pamabisa chiwawa.
12 Sovraštvo razvnema prepire, toda ljubezen pokriva vse grehe.
Udani umawutsa mikangano, koma chikondi chimaphimba zolakwa zonse.
13 Na ustnicah tistega, ki ima razumevanje, je najti modrost, toda palica je za hrbet tistega, ki je brez razumevanja.
Nzeru imapezeka pa milomo ya munthu wozindikira zinthu, koma pa msana pa munthu wopanda nzeru sipachoka chikwapu.
14 Modri ljudje kopičijo spoznanje, toda usta nespametnega so blizu uničenja.
Anzeru amasunga chidziwitso koma pakamwa pa chitsiru pamatulutsa zowononga.
15 Bogataševo premoženje je njegovo močno mesto. Uničenje revnih je njihova revščina.
Chuma cha munthu wolemera ndiye chitetezo chake; koma umphawi ndiye chiwonongeko cha osauka.
16 Trud pravičnega se nagiba k življenju, sad zlobnega h grehu.
Moyo ndiye malipiro a munthu wolungama, koma phindu la anthu oyipa ndi uchimo ndi imfa.
17 Tisti, ki se drži poučevanja, je na poti življenja, toda kdor odklanja opomin, se moti.
Wosamalira malangizo amayenda mʼnjira ya moyo, koma wonyoza chidzudzulo amasochera.
18 Kdor z lažnivimi ustnicami skriva sovraštvo in kdor izreka obrekovanje, je bedak.
Amene amabisa chidani chake ndi munthu wonama, ndipo amene amafalitsa miseche ndi chitsiru.
19 V množici besed ne manjka greha, toda kdor zadržuje svoje ustnice, je moder.
Mawu akachuluka zolakwa sizisowa, koma amene amasunga pakamwa pake ndi wanzeru.
20 Jezik pravičnega je kakor izbrano srebro, srce zlobnega je malo vredno.
Mawu a munthu wolungama ali ngati siliva wabwino kwambiri, koma mtima wa munthu woyipa ndi wopanda phindu.
21 Ustnice pravičnega hranijo mnoge, toda bedaki umrejo zaradi pomanjkanja modrosti.
Milomo ya anthu olungama imalimbikitsa ambiri; koma chitsiru chimafa chifukwa chosowa nzeru.
22 Gospodov blagoslov, ta bogatí in s tem on ne dodaja nobene bridkosti.
Mdalitso wa Yehova ndiwo umabweretsa chuma, ntchito za munthu siziwonjezerapo kanthu.
23 To je kakor zabava bedaku, da počne vragolijo, toda razumevajoč človek ima modrost.
Kwa chitsiru kuchita zinthu zoyipa ndiye chinthu chomusangalatsa, koma kwa munthu womvetsa bwino zinthu nzeru ndiyo imamusangalatsa.
24 Strah zlobnega bo prišel nanj, toda želja pravičnega bo zagotovljena.
Chimene munthu woyipa amachiopa chidzamuchitikira; chimene munthu wolungama amachilakalaka adzachipeza.
25 Kakor mine vrtinčast veter, tako zlobnega ni več, toda pravični je večen temelj.
Pamene namondwe wawomba, anthu oyipa amachotsedwa, koma anthu olungama amakhazikika mpaka muyaya.
26 Kakor kis zobem in kakor dim očem, tako je lenuh tistim, ki ga pošljejo.
Momwe amakhalira vinyo wosasa mʼkamwa ndi momwe umakhalira utsi mʼmaso, ndi momwenso amakhalira munthu waulesi kwa amene amutuma.
27 Strah Gospodov podaljšuje dneve, toda leta zlobnega bodo skrajšana.
Kuopa Yehova kumatalikitsa moyo; koma zaka za anthu oyipa zidzafupikitsidwa.
28 Upanje pravičnega bo veselje, toda pričakovanje zlobnega bo propadlo.
Chiyembekezo cha olungama chimapatsa chimwemwe, koma chiyembekezo cha anthu ochimwa chidzafera mʼmazira.
29 Gospodova pot je moč iskrenemu, toda uničenje bo za delavce krivičnosti.
Njira za Yehova ndi linga loteteza anthu ochita zabwino, koma wochita zoyipa adzawonongeka.
30 Pravični ne bo nikoli odstranjen, toda zloben ne bo poselil zemlje.
Munthu wolungama sadzachotsedwa, pamalo pake koma oyipa sadzakhazikika pa dziko.
31 Usta pravičnega prinašajo modrost, toda kljubovalen jezik bo odrezan.
Pakamwa pa munthu wolungama pamatulutsa za nzeru, koma lilime lokhota lidzadulidwa.
32 Ustnice pravičnega vedo, kaj je sprejemljivo, toda usta zlobnega govorijo kljubovalnost.
Milomo ya anthu olungama imadziwa zoyenera kuyankhula, koma pakamwa pa anthu ochimwa pamatulutsa zokhota zokhazokha.