< Abdija 1 >
1 Abdíjevo videnje. Tako govori Gospod Bog glede Edóma: »Slišali smo govorico od Gospoda in predstavnik je poslan med pogane: ›Vstanite in vzdignimo se v bitki zoper njega.‹
Masomphenya a Obadiya. Ambuye Yehova akunena kwa Edomu kuti, Tamva uthenga wochokera kwa Yehova: Nthumwi yatumidwa kupita kwa anthu a mitundu kukanena kuti, “Konzekani, tiyeni tikachite nkhondo ndi Edomu.”
2 Glej, naredil sem te majhnega med pogani, silno si preziran.
“Taona, ndidzakuchepetsani pakati pa anthu a mitundu ina; udzanyozedwa kwambiri.
3 Ponos tvojega srca te je zavedel, ti, ki prebivaš v skalnih razpokah, katerega prebivališče je visoko, ki v svojem srcu praviš: ›Kdo me bo privedel dol na tla?‹
Kudzikuza kwa mtima wako kwakusocheretsa, iwe amene umakhala mʼmapanga a mʼmatanthwe ndipo umamanga nyumba zako pa mapiri ataliatali, iwe amene umanena mu mtima mwako kuti, ‘Ndani anganditsitse pansi?’
4 Čeprav se povišuješ kakor orel in čeprav si svoje gnezdo postavil med zvezde, te bom od tam privedel dol, ‹ govori Gospod.
Koma ngakhale umawuluka ngati chiwombankhanga ndi kumanga chisa chako pakati pa nyenyezi, ndidzakutsitsa pansi kuchokera kumeneko,” akutero Yehova.
5 ›Če pridejo k tebi tatovi, če roparji ponoči (kako si iztrebljen!), mar ne bodo kradli, dokler nimajo dovolj? Če pridejo k tebi obiralci grozdja, mar ne bodo pustili nekaj grozdov?
“Anthu akuba akanabwera kwa iwe, kapena anthu olanda zinthu akanafika usiku, aa, tsoka lanji limene likukudikira iwe! Kodi akanangotengako zimene akuzifuna zokha? Ngati anthu othyola mphesa akanafika, kodi akanakusiyiraniko mphesa pangʼono pokha?
6 Kako so Ezavove stvari preiskane! Kako so njegove skrite stvari poiskane!
Koma Esau adzalandidwa zinthu zonse, chuma chake chobisika chidzabedwa!
7 Vsi možje tvoje zaveze so te privedli, celó k meji. Možje, ki so bili v miru s teboj, so te zavedli in prevladali zoper tebe. Tisti, ki jedo tvoj kruh, so položili rano pod teboj. Nobenega razumevanja ni v njem.
Anthu onse ogwirizana nawo adzakupirikitsira kumalire; abwenzi ako adzakunyenga ndi kukugonjetsa; amene amadya chakudya chako adzakutchera msampha, koma iwe sudzazindikira zimenezi.”
8 Mar ne bom na ta dan, ‹ govori Gospod, ›celo uničil modre može iz Edóma in razumevanje z Ezavove gore?
Yehova akunena kuti, “Tsiku limenelo, kodi sindidzawononga anthu onse anzeru a ku Edomu, anthu odziwa zinthu mʼmapiri a Esau?
9 In tvoji mogočni ljudje, oh Temán, bodo zaprepadeni do konca, z namenom, da bo vsakdo z Ezavove gore iztrebljen s pokolom.
Ankhondo ako, iwe Temani, adzachita mantha, ndipo aliyense amene ali mʼphiri la Esau adzaphedwa pa nkhondo.
10 Zaradi tvojega nasilja zoper tvojega brata Jakoba te bo pokrila sramota in iztrebljen boš na veke.
Chifukwa cha nkhanza zimene unachitira mʼbale wako Yakobo, udzakhala wamanyazi; adzakuwononga mpaka muyaya.
11 Na dan, ko stojiš na drugi strani, na dan, ko tujci odvedejo njegove sile ujete in tuji ljudje vstopijo v njegova velika vrata in mečejo žrebe nad Jeruzalemom, si bil celo ti kakor eden izmed njih.
Pamene adani ankamulanda chuma chake pamene alendo analowa pa zipata zake ndi kuchita maere pa Yerusalemu, pa tsikulo iwe unali ngati mmodzi wa iwo.
12 Toda ne bi smel gledati na dan svojega brata, na dan, ko je postal tujec, niti ne bi smel imeti veselja nad Judovimi otroki na dan njihovega uničenja, niti ne bi smel ponosno govoriti na dan tegobe.
Iwe sunayenera kunyoza mʼbale wako pa nthawi ya tsoka lake, kapena kunyogodola Ayuda chifukwa cha chiwonongeko chawo, kapena kuwaseka pa nthawi ya mavuto awo.
13 Ne bi smel vstopiti v velika vrata mojega ljudstva na dan njihove katastrofe. Da, ne bi smel gledati na njihovo stisko na dan njihove katastrofe niti rok položiti na njihovo imetje na dan njihove katastrofe;
Iwe sunayenera kudutsa pa zipata za anthu anga pa nthawi ya masautso awo, kapena kuwanyogodola pa tsiku la tsoka lawo, kapena kulanda chuma chawo pa nthawi ya masautso awo.
14 niti ne bi smel stati na razpotju, da bi iztrebil tiste izmed njegovih, ki so pobegnili; niti ne bi smel izročiti tistih izmed njegovih, ki so pobegnili na dan stiske.
Sunayenera kudikirira pamphambano ya misewu kuti uphe Ayuda othawa, kapena kuwapereka kwa adani awo Ayuda opulumuka pa nthawi ya mavuto awo.”
15 Kajti dan Gospodov je blizu nad vsemi pogani. Kakor si ti storil, tako bo storjeno tebi. Tvoja nagrada se bo povrnila na tvojo lastno glavo.
“Tsiku la Yehova layandikira limene adzaweruza mitundu yonse ya anthu. Adzakuchitira zomwe unawachitira ena; zochita zako zidzakubwerera wekha.
16 Kajti kakor ste pili na moji sveti gori, tako bodo vsi pogani nenehno pili, da, pili bodo in bodo požirali in bodo, kot da jih ni bilo.
Iwe unamwa pa phiri langa loyera, koteronso mitundu ina yonse idzamwa kosalekeza; iwo adzamwa ndi kudzandira ndipo adzayiwalika pa mbiri ya dziko lapansi.
17 Toda na gori Sion bo osvoboditev in tam bo svetost, in Jakobova hiša bo v last vzela njihove posesti.
Koma pa Phiri la Ziyoni padzakhala chipulumutso; phirilo lidzakhala lopatulika, ndipo nyumba ya Yakobo idzalandira cholowa chake.
18 Jakobova hiša bo ogenj in Jožefova hiša plamen, Ezavova hiša pa strnišče in v njih se bodo vneli in jih požrli, in tam ne bo nobenega ostanka Ezavove hiše, kajti Gospod je to govoril.
Nyumba ya Yakobo idzasanduka moto ndipo nyumba ya Yosefe idzasanduka lawi la moto; nyumba ya Esau idzasanduka chiputu, ndipo adzayitenthe pa moto ndi kuyipsereza. Sipadzakhala anthu opulumuka kuchokera mʼnyumba ya Esau.” Yehova wayankhula.
19 Tisti iz juga bodo vzeli v last goro Ezav, in tisti iz ravnine Filistejce in vzeli bodo v last Efrájimova polja in polja Samarije, Benjamin pa bo posedel Gileád.
Anthu ochokera ku Negevi adzakhala ku mapiri a Esau, ndipo anthu ochokera mʼmbali mwa mapiri adzatenga dziko la Afilisti. Adzakhala mʼminda ya Efereimu ndi Samariya, ndipo Benjamini adzatenga Giliyadi.
20 Ujetništvo te vojske Izraelovih otrok bo vzelo v last to od Kánaancev, celó do Zarepte; in ujetništvo Jeruzalema, ki je v Sefarádu, bo posedlo južna mesta.
Aisraeli amene ali ku ukapolo adzalandira dziko la Kanaani mpaka ku Zarefati; a ku Yerusalemu amene ali ku ukapolo ku Sefaradi adzalandira mizinda ya ku Negevi.
21 Rešitelji bodo prišli na goro Sion, da sodijo Ezavovo goro, in kraljestvo bo Gospodovo.‹«
Opulumukawo adzapita ku Phiri la Ziyoni ndipo adzalamulira mapiri a Esau. Koma ufumuwo udzakhala wa Yehova.