< 4 Mojzes 14 >

1 Vsa skupnost je povzdignila svoj glas in zajokala in ljudstvo je to noč jokalo.
Usiku umenewo gulu lonse la Aisraeli linalira mofuwula kwambiri.
2 Vsi Izraelovi otroci so godrnjali zoper Mojzesa in zoper Arona in celotna skupnost jima je rekla: »Da bi Bog dal, da bi umrli v egiptovski deželi! Ali da bi Bog dal, da bi umrli v tej divjini!
Ndipo Aisraeli onse anayankhula motsutsana ndi Mose ndi Aaroni. Gulu lonse linanena kwa iwo kuti, “Kunali bwino tikanafera ku Igupto kapena mʼchipululu muno!
3 Zakaj nas je Gospod privedel v to deželo, da pademo pod mečem, da bi bile naše žene in naši otroci plen? Ali ne bi bilo za nas bolje, da se vrnemo v Egipt?«
Nʼchifukwa chiyani Yehova akutilowetsa mʼdziko limenelo? Kodi kuti tikaphedwe ndi lupanga? Kuti akazi ndi ana athu akatengedwe ngati katundu wolanda ku nkhondo? Kodi sikungakhale bwino kuti tibwerere ku Igupto?”
4 Drug drugemu so rekli: »Postavimo si poveljnika in se vrnimo v Egipt.«
Ndipo anawuzana wina ndi mnzake kuti, “Tiyeni tisankhe mtsogoleri ndipo tibwerere ku Igupto.”
5 Potem sta Mojzes in Aron padla na svoja obraza pred vsem zborom skupnosti Izraelovih otrok.
Koma Mose ndi Aaroni anadzigwetsa pansi chafufumimba pamaso pa Aisraeli onse omwe anasonkhana pamenepo.
6 Nunov sin Józue in Jefunéjev sin Kaléb, ki sta bila izmed tistih, ki sta preiskala deželo, sta pretrgala svoja oblačila
Yoswa mwana wa Nuni ndi Kalebe mwana wa Yefune, omwe anali amodzi mwa amene anakazonda nawo dziko, anangʼamba zovala zawo
7 in spregovorila vsej skupini Izraelovih otrok, rekoč: »Dežela, skozi katero sva šla, da jo preiščeva, je silno dobra dežela.
ndipo anati kwa gulu lonse la Aisraeli, “Dziko limene tinakayendamo ndi kuliona ndi labwino kwambiri zedi.
8 Če se Gospod razveseljuje v nas, potem nas bo privedel v to deželo in nam jo izročil; deželo, v kateri tečeta mleko in med.
Ngati Yehova akukondwera nafe, adzatitsogolera kulowa mʼdziko limenelo. Dziko loyenda mkaka ndi uchi adzalipereka kwa ife,
9 Samo ne uprite se zoper Gospoda niti se ne bojte ljudstva dežele, kajti oni so za nas kruh. Njihova obramba je odšla od njih, Gospod pa je z nami. Ne bojte se jih.«
koma musawukire Yehova. Komanso musaope anthu a mʼdzikomo, pakuti tidzawagonjetsa. Chitetezo chawachokera, koma ife Yehova ali nafe. Musawaope.”
10 Toda vsa skupnost ju je zaukazala kamnati s kamni. In Gospodova slava se je prikazala v šotorskem svetišču skupnosti, pred vsemi Izraelovimi otroki.
Koma gulu lonse linayankhula zofuna kuwagenda miyala. Pamenepo ulemerero wa Yehova unaonekera kwa Aisraeli onse ku tenti ya msonkhano.
11 Gospod je rekel Mojzesu: »Doklej me bo to ljudstvo še dražilo? Kako dolgo bo, preden mi bodo verovali zaradi vseh znamenj, ki sem jih prikazal med njimi?
Yehova anawuza Mose kuti, “Anthu awa adzandinyoza mpaka liti? Sadzandikhulupirira mpaka liti, ngakhale ndachita zizindikiro zozizwitsa zonsezi pakati pawo?
12 Udaril jih bom s kužno boleznijo in jih razdedinil in iz tebe bom naredil večji narod ter mogočnejši, kakor so oni.«
Ndidzawakantha ndi mliri ndi kuwawononga. Koma ndidzakusandutsa iwe mtundu waukulu ndi wamphamvu kuposa iwo.”
13 Mojzes pa je Gospodu rekel: »Potem bodo Egipčani to slišali, (kajti v svoji moči si to ljudstvo privedel izmed njih)
Mose anati kwa Yehova, “Aigupto adzamva zimenezi! Mwa mphamvu yanu munawatulutsa anthu amenewa pakati pawo.
14 in bodo to povedali prebivalcem te dežele, kajti slišali so, da si ti Gospod med tem ljudstvom, da si ti Gospod, viden iz obličja v obličje in da tvoj oblak stoji nad njimi in da greš pred njimi, podnevi v oblačnem stebru, ponoči pa v ognjenem stebru.
Ndipo iwowo adzawuza anthu okhala mʼdziko lino zimenezi. Anthuwa amva kale kuti Inu Yehova mumakhala pakati pa anthu amenewa ndi kuti Inuyo Yehova mwawaonekera maso ndi maso. Mtambo wanu umakhala pamwamba pawo ndiponso mumayenda nawo mu mtambo woyima, masana ndi moto woyima, usiku.
15 Torej če boš pobil vse to ljudstvo kakor enega človeka, potem bodo narodi, ki so slišali o tvojem slovesu, govorili, rekoč:
Tsono mukawapha anthu onsewa nthawi imodzi, mayiko amene anamva za Inu adzati,
16 ›Ker Gospod tega ljudstva ni mogel privesti v deželo, ki jim jo je prisegel, jih je zato umoril v divjini.‹
‘Yehova walephera kuwalowetsa anthuwo mʼdziko lomwe anawalonjeza molumbira, ndipo wawapha mʼchipululu.’
17 Sedaj te rotim, naj bo moč mojega Gospoda velika, glede na to, kakor si govoril, rekoč:
“Chonde Ambuye wonetsani mphamvu yanu monga munalonjezera kuti,
18 › Gospod je potrpežljiv in zelo usmiljen, ki odpušča krivičnost in prestopek in nikakor ne očisti krivega, ki obiskuje krivičnost očetov na otrocih do tretjega in četrtega rodu.‹
‘Yehova sakwiya msanga, ndipo ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika, wokhululukira tchimo ndi kuwukira. Koma Iye sadzaleka kulanga ochimwa. Iyeyo amalanga ana chifukwa cha tchimo la makolo awo kufikira mʼbado wachitatu ndi wachinayi.’
19 Odpusti, rotim te, krivičnost tega ljudstva, glede na veličino svojega usmiljenja in kakor si odpuščal temu ljudstvu, od Egipta, celo do sedaj.«
Chifukwa cha kukula kwa chikondi chanu chosasinthika, akhululukireni anthuwa tchimo lawo monga mwakhala mukuwakhululukira kuchokera pa nthawi imene anachoka ku Igupto mpaka tsopano.”
20 Gospod je rekel: »Odpustil sem glede na tvojo besedo,
Yehova anayankha kuti, “Ndawakhululukira monga wapemphera.
21 vendar kakor resnično jaz živim, bo vsa zemlja napolnjena z Gospodovo slavo.
Komabe, ndikunenetsa kuti pali Ine, ndiponso pamene dziko lapansi ladzaza ndi ulemerero wa Yehova,
22 Ker so vsi tisti ljudje, ki so videli mojo slavo in moje čudeže, ki sem jih storil v Egiptu in v divjini in so me skušali sedaj teh desetkrat in niso prisluhnili mojemu glasu;
palibe ndi mmodzi yemwe mwa anthu amene anaona ulemerero wanga ndi zizindikiro zozizwitsa zimene ndinazichita ku Igupto ndi mʼchipululu muno, koma osandimvera ndi kundiyesa kokwanira kakhumi,
23 zagotovo ne bodo videli dežele, ki sem jo prisegel njihovim očetom niti je ne bo videl nobeden izmed tistih, ki so me dražili.
palibe ndi mmodzi yemwe wa anthu amenewa amene adzaone dziko limene ndinalonjeza ndi lumbiro kwa makolo awo. Aliyense amene anandinyoza sadzaliona dzikolo.
24 Toda ker je imel moj služabnik Kaléb, v sebi drugega duha in mi je popolnoma sledil, ga bom privedel v deželo, v katero je odšel, in njegovo seme jo bo vzelo v last.
Koma mtumiki wanga Kalebe, pakuti ali ndi mtima wosiyana ndi ena ndiponso amanditsatira ndi mtima wonse, ndidzamulowetsa mʼdziko limene anapitamolo ndipo zidzukulu zake zidzalandira dzikolo ngati cholowa chawo.
25 (Torej Amálečani in Kánaanci so prebivali v dolini.) Jutri se obrnite in se odpravite v divjino, po poti Rdečega morja.«
Ndipo popeza kuti Aamaleki ndi Akanaani akukhala ku chigwa, mawa mubwerere ndipo mupite ku chipululu podzera ku Nyanja Yofiira.”
26 Gospod je spregovoril Mojzesu in Aronu, rekoč:
Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti,
27 »Doklej bom še prenašal to zlo skupnost, ki godrnja zoper mene? Slišal sem mrmranja Izraelovih otrok, ki mrmrajo zoper mene.
“Kodi anthu oyipawa adzangʼungʼudza ndi kutsutsana nane mpaka liti? Ndamva madandawulo a Aisraeli ongʼungʼudzawa.
28 Reci jim: › Kakor resnično jaz živim, ‹ govori Gospod, ›kakor ste govorili v moja ušesa, tako bom jaz storil vam.
Tsono awuze kuti, ‘Ndikulumbira pali Ine,’ akutero Yehova, ‘Ndidzakuchitirani zinthu zonse zimene ndamva inu mukunena:
29 Vaša trupla bodo padla v tej divjini in vsi, kar vas je bilo izmed vas preštetih, glede na vaše celotno število, od dvajset let stari in navzgor, ki ste godrnjali zoper mene.
Mitembo yanu idzakhala ili ngundangunda mʼchipululu muno; mtembo wa munthu aliyense pakati panu amene ali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, amene anawerengedwa pa chiwerengero chija ndipo anangʼungʼudza motsutsana nane.
30 Zagotovo ne boste prišli v deželo, glede katere sem prisegel, da v njej prebivate, razen Jefunéjevega sina Kaléba in Nunovega sina Józueta.
Palibe ndi mmodzi yemwe mwa inu amene adzalowe mʼdziko lomwe ndinalumbira mokweza manja kuti likhale lanu, kupatula Kalebe mwana wa Yefune ndi Yoswa mwana wa Nuni.
31 Toda vaše malčke, za katere ste rekli, da naj bi bili plen, te bom privedel noter in oni bodo spoznali deželo, ki ste jo vi prezirali.
Koma ana anu amene mukunena kuti adzatengedwa ngati katundu wolanda ku nkhondo, Ine ndidzawalowetsa kuti akasangalale mʼdziko limene munalikana.
32 Toda kar se tiče vas, bodo vaša trupla padla v tej divjini.
Koma inu mitembo yanu idzakhala ngundangunda mʼchipululu muno.
33 Vaši otroci se bodo štirideset let potikali po divjini in nosili vaša vlačugarstva, dokler ne bodo vaša trupla propadla v divjini.
Ana anu adzakhala abusa mʼchipululu muno zaka makumi anayi, kuvutika chifukwa cha kusakhulupirika kwanu, mpaka munthu womaliza mwa inu atafa mʼchipululu muno.
34 Po številu dni, v katerih ste preiskovali deželo, torej štirideset dni, vsak dan za leto, boste nosili svoje krivičnosti, celó štirideset let in spoznali boste moj odmik od obljube.‹
Mudzavutika chifukwa cha machimo anu kwa zaka makumi anayi Chaka chimodzi chikuyimira tsiku limodzi la masiku makumi anayi amene munakazonda dziko lija ndipo mudzadziwa kuyipa kwake kwa kukangana ndi Ine.’
35 Jaz, Gospod, sem rekel: ›Zagotovo bom tako storil vsej tej zli skupnosti, ki je skupaj zbrana zoper mene. V tej divjini bodo použiti in tam bodo umrli.‹«
Ine Yehova, ndanena, ndidzachitadi zimenezi kwa anthu onse oyipawa, amene agwirizana kunditsutsa. Adzathera mʼchipululu momwe muno, adzafera muno basi.”
36 Možje, ki jih je Mojzes poslal, da preiščejo deželo, ki so se vrnili in vso skupnost pripravili, da je mrmrala zoper njega s prinašanjem obrekovanja nad deželo,
Ndipo anthu amene Mose anawatuma kukazonda dziko aja anachoka pamaso pake nachititsa gulu lonse la anthu kuwukira Moseyo chifukwa chofalitsa mbiri yoyipa ya dzikolo.
37 celo ti možje, ki so nad deželo prinesli zlo poročilo, so zaradi kuge umrli pred Gospodom.
Anthu amene ankafalitsa mbiri yoyipa ya dzikolo anakanthidwa ndi mliri ndipo anafa pamaso pa Yehova.
38 Toda Nunov sin Józue in Jefunéjev sin Kaléb, ki sta bila izmed mož, ki so odšli, da preiščejo deželo, sta še vedno živela.
Mwa anthu amene anakaona dzikolo, Yoswa mwana wa Nuni ndi Kalebe mwana wa Yefune ndi okhawo amene anapulumuka.
39 Mojzes je te stvari povedal vsem Izraelovim otrokom in ljudstvo je silno žalovalo.
Mose atafotokoza izi kwa Aisraeli onse, anthuwo analira kwambiri.
40 Vstali so zgodaj zjutraj in se povzpeli na vrh gore, rekoč: »Glej! Mi smo tukaj in šli bomo gor, na kraj, ki nam ga je Gospod obljubil, kajti grešili smo.«
Mmamawa tsiku linalo anapita mbali ya ku dziko la mapiri. Iwo anati, “Tachimwa, tipita ku dziko limene Yehova anatilonjeza.”
41 Mojzes je rekel: »Zakaj sedaj prestopate Gospodovo zapoved? Toda to ne bo uspelo.
Koma Mose anati, “Chifukwa chiyani simukumvera lamulo la Yehova? Zimenezi sizitheka!
42 Ne pojdite gor, kajti Gospoda ni med vami, da ne boste udarjeni pred svojimi sovražniki.
Musapite chifukwa Yehova sali pakati panu. Mudzagonjetsedwa ndi adani anu
43 Kajti Amalečani in Kánaanci so tam pred vami in vi boste padli pod mečem, ker ste obrnjeni proč od Gospoda, zato Gospod ne bo z vami.«
chifukwa kumeneko mukakumana ndi Aamaleki ndi Akanaani. Popeza mwaleka kutsata Yehova, Iyeyo sadzakhala nanu ndipo mudzaphedwa ndi lupanga.”
44 Vendar pa so si predrznili, da gredo na vrh hriba. Vendar skrinja Gospodove zaveze in Mojzes nista odšla iz tabora.
Komabe mwa maganizo awo anapita molunjika dziko la mapiri ngakhale kuti Mose sanachoke ndi Bokosi la Chipangano la Yehova pa msasa.
45 Potem so prišli dol Amálečani in Kánaanci, ki so prebivali na tem hribu in jih udarili ter porazili, celó do Horme.
Koma Aamaleki ndi Akanaani amene ankakhala ku dziko lamapirilo anatsika ndi kumenyana nawo ndipo anawakantha mʼnjira yonse mpaka ku Horima.

< 4 Mojzes 14 >