< 3 Mojzes 16 >
1 Gospod je spregovoril Mojzesu po smrti Aronovih dveh sinov, ko sta darovala pred Gospodom in umrla,
Atafa ana awiri a Aaroni amene anaphedwa atapita pamaso pa Yehova mosayenera, Yehova anayankhula ndi Mose.
2 in Gospod je rekel Mojzesu: »Govori svojemu bratu Aronu, da ne pride ob vseh časih v sveti prostor znotraj zagrinjala, pred sedež milosti, ki je na skrinji, da ne umre, kajti jaz se bom v oblaku prikazal nad sedežem milosti.
Yehova anawuza Mose kuti, “Uza mchimwene wako Aaroni kuti asamalowe ku Malo Wopatulika, kuseri kwa katani, pamaso pa chivundikiro cha Bokosi la Chipangano nthawi iliyonse imene akufuna kuopa kuti angadzafe, pakuti Ine ndimaoneka mu mtambo umene uli pamwamba pa chivundikiro cha Bokosi la Chipangano.
3 Tako bo Aron prišel na sveti kraj: z mladim bikcem za daritev za greh in ovnom za žgalno daritev.
“Aaroni azilowa Malo Wopatulika Kwambiri motere: azitenga mwana wangʼombe wamwamuna kuti akhale nsembe yopepesera machimo ndi nkhosa yayimuna kuti ikhale nsembe yopsereza.
4 Nadel si bo svet lanen plašč, na svojem mesu bo imel kratke platnene hlače, opasan bo z lanenim pasom in okrašen z lanenim turbanom. To so sveta oblačila, zato bo svoje meso umil v vodi in si jih tako nadel.
Azivala mwinjiro wopatulika wa nsalu yosalala, azivalanso kabudula wa mʼkati wa nsalu yosalala, azimanga lamba wa nsalu yosalala, ndipo avalenso nduwira ya nsalu yosalala kumutu. Zimenezi ndi nsalu zopatulika ndipo atasamba thupi lonse azivala zimenezi.
5 Od zbora Izraelovih otrok bo vzel dva kozlička od koz za daritev za greh in enega ovna za žgalno daritev.
Kuchokera pa gulu la Aisraeli, Aaroni azitenga mbuzi zazimuna ziwiri kuti zikhale nsembe yopepesera machimo ndi nkhosa yayimuna kuti ikhale nsembe yopsereza.
6 Aron bo daroval svojega bikca daritve za greh, ki je zanj ter opravil spravo zase in za svojo hišo.
“Aaroni apereke ngʼombe yayimuna kuti ikhale yopepesera machimo a iye mwini kuti achite mwambo wopepesera machimo ake pamodzi ndi a banja lake.
7 Vzel bo dva kozla in ju postavil pred Gospoda, pri vratih šotorskega svetišča skupnosti.
Kenaka atenge mbuzi ziwiri zija ndipo aziyimike pamaso pa Yehova pa khomo la tenti ya msonkhano.
8 Aron bo metal žrebe med dvema kozloma. En žreb za Gospoda, drugi žreb pa za ubežnega kozla.
Aaroni ndiye achite maere pa mbuzi ziwirizo kuti imodzi ikhale ya Yehova, ndipo inayo ikhale ya Azazele.
9 Aron bo privedel kozla, na katerega je padel Gospodov žreb in ga daroval za daritev za greh.
Aaroni abwere ndi mbuzi imene maere aonetsa kuti ndi ya Yehova, ndipo apereke kuti ikhale nsembe yopereka chifukwa cha tchimo.
10 Toda kozel, na katerega pade žreb, da bo ubežen kozel, bo živ postavljen pred Gospoda, da z njim opravi spravo in da ga za ubežnega kozla spusti v divjino.
Koma mbuzi imene maere aonetsa kuti ndi yosenza machimo, apereke ya moyo pamaso pa Yehova, kuti achite mwambo wopepesera machimo pa mbuziyo poyitumiza ku chipululu kuti ikhale ya Azazele.
11 Aron bo privedel bikca daritve za greh, ki je zanj in opravil spravo zase in za svojo hišo in zaklal bo bikca daritve za greh, ki je zanj,
“Aaroni apereke ngʼombe yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo ake. Ndiye achite mwambo wopepesera machimo a iye mwini wake pamodzi ndi banja lake. Pambuyo pake aphe ngʼombe yopepesera machimo ake aja.
12 in izpred oltarja, pred Gospodom, bo vzel kadilnico, polno gorečega ognjenega oglja in svoji roki polni drobno zdrobljenega dišečega kadila in to bo prinesel znotraj zagrinjala.
Kenaka iye atenge chofukizira chodzaza ndi makala a moto ochokera pa guwa lansembe pamaso pa Yehova. Atengenso lubani wonunkhira ndi woperapera wokwanira manja awiri, ndipo alowe naye kuseri kwa katani.
13 Kadilo bo položil na ogenj pred Gospodom, da oblak kadila lahko pokrije sedež milosti, ki je nad pričevanjem, da ne umre.
Athire lubani pa moto pamaso pa Yehova kuti utsi wa lubaniyo uphimbe chivundikiro chimene chili pamwamba pa Bokosi la Chipangano, kuti Aaroniyo asafe.
14 Vzel bo od krvi bikca in jo s svojim prstom poškropil nad sedežem milosti proti vzhodu. Pred sedežem milosti bo s svojim prstom sedemkrat poškropil kri.
Ndipo atenge magazi ena a ngʼombeyo, awawaze ndi chala chake pa chivundikiro cha kummawa; kenaka awaze magaziwo ndi chala chake kasanu ndi kawiri patsogolo pa chivundikirocho.
15 Potem bo zaklal kozla daritve za greh, ki je za ljudstvo in njegovo kri prinesel znotraj zagrinjala in s to krvjo storil, kakor je storil s krvjo bikca in jo poškropil nad sedežem milosti in pred sedežem milosti.
“Kenaka Aaroni aphe mbuzi ya nsembe yopepesera machimo a anthu, ndipo magazi ake alowe nawo kuseri kwa katani ndi kuchita chimodzimodzi monga anachitira ndi magazi a ngʼombe aja: Aaroni awaze magaziwo pa chivundikiro chija ndi patsogolo pa chivundikirocho.
16 Zaradi nečistosti Izraelovih otrok in zaradi njihovih prestopkov v vseh njihovih grehih bo opravil spravo za svet kraj in tako bo storil za šotorsko svetišče skupnosti, ki ostaja med njimi v sredi njihove nečistosti.
Pamenepo ndiye kuti wansembeyo wachita mwambo wopepesera ku Malo Wopatulika chifukwa cha kudetsedwa ndi kuwukira kwa Aisraeli pa machimo ena aliwonse amene achita. Achite chimodzimodzi ndi tenti ya msonkhano imenenso ili yodetsedwa chifukwa cha machimo awo.
17 Tam ne bo nobenega moža v šotorskem svetišču skupnosti, ko gre vanj, da opravi spravo na svetem kraju, dokler ne pride ven in je opravil spravo zase, za svojo družino in za vso Izraelovo skupnost.
Mu tenti ya msonkhano musakhale munthu ndi mmodzi yemwe nthawi imene Aaroni akupita kukachita mwambo wopepesera ku Malo Wopatulika mpaka atatulukako. Musakhale munthu mu tenti ya msonkhano mpaka atachita mwambo wopepesera machimo a iye mwini wake, banja lake ndi gulu lonse la Aisraeli.
18 Odšel bo ven, k oltarju, ki je pred Gospodom in opravil spravo zanj. Vzel bo od krvi bikca in od krvi kozla in to položil naokoli, na oltarne rogove.
“Kenaka, Aaroniyo akatuluka apite ku guwa limene lili pamaso pa Yehova ndi kulichitira mwambo wolipepesera. Atengeko magazi a ngʼombe yayimuna ndiponso magazi a mbuzi ndi kuwapaka pa nyanga zonse za guwa lansembe.
19 S svojim prstom bo nanj sedemkrat poškropil od krvi, ga očistil in ga posvetil pred nečistostjo Izraelovih otrok.
Magazi ena awawaze pa guwalo ndi chala chake kasanu ndi kawiri kuliyeretsa ndi kulipatula kuchotsa zodetsa za Aisraeli.
20 Ko zaključi očiščenje svetega kraja, šotorskega svetišča skupnosti in oltarja, bo privedel živega kozla,
“Aaroni akatsiriza mwambo wopepesera Malo Wopatulika, tenti ya msonkhano ndi guwa, azibwera ndi mbuzi yamoyo kudzayipereka nsembe.
21 in Aron bo obe svoji roki položil na glavo živega kozla in nad njim priznal vse krivičnosti Izraelovih otrok in vse njihove prestopke v vseh njihovih grehih, s tem, da jih položi na glavo kozla in ga po roki primernega moža pošlje proč, v divjino.
Aaroni asanjike manja ake pa mutu wa mbuziyo ndipo awulule pa mbuziyo zoyipa zonse ndi zowukira zonse za Aisraeli, kutanthauza machimo awo onse. Machimowo awayike pa mutu wa mbuziyo. Kenaka munthu amene anasankhidwa athamangitsire mbuziyo ku chipululu.
22 Kozel bo na sebi nosil vse njihove krivičnosti v nenaseljeno deželo in kozla bo spustil v divjino.
Mbuziyo isenze machimo awo onse ndi kupita nawo kutali ndipo munthuyo aleke mbuziyo kuti ipite ku chipululuko.
23 Aron bo prišel v šotorsko svetišče skupnosti in odložil lanene obleke, ki jih je oblekel, ko je odšel v sveti kraj in jih bo pustil tam.
“Pambuyo pake Aaroni alowe mu tenti ya msonkhano ndi kuvula zovala zosalala zija zimene anavala polowa ku Malo Wopatulika ndi kuzisiya komweko.
24 Svoje meso bo z vodo umil na svetem kraju in si nadel svoje obleke in prišel naprej ter daroval svojo žgalno daritev, žgalno daritev za ljudstvo in opravil spravo zase in za ljudstvo.
Asambe thupi lonse ku Malo Wopatulika ndi kuvala zovala zake za nthawi zonse. Kenaka atuluke ndi kukapereka nsembe yopsereza ya iye mwini, ndiponso nsembe yopsereza yoperekera anthu. Akatero ndiye kuti wachita mwambo wopepesera machimo a iye mwini wake ndi a anthu.
25 Tolščo daritve za greh bo sežgal na oltarju.
Mafuta a nyama yopepesera machimo awatenthe pa guwa lansembe.
26 Tisti, ki je spustil kozla za ubežnega kozla, bo opral svoja oblačila in svoje meso umil v vodi in potem pride v tabor.
“Tsono munthu amene anaperekeza mbuzi yosenza machimo ija achape zovala zake ndi kusamba. Pambuyo pake alowe ku msasa.
27 Bikca daritve za greh in kozla daritve za greh, čigar kri je bila prinesena, da opravi spravo na svetem kraju, bo nekdo odnesel zunaj tabora, v ognju pa bodo sežgali njihove kože, njihovo meso in njihov iztrebek.
Ngʼombe ndi mbuzi zoperekera nsembe yopepesera machimo zimene magazi ake anabwera nawo kuti achitire mwambo wopepesera Malo Wopatulika, azitulutsire kunja kwa msasa. Koma zikopa zake, nyama yake ndi matumbo ake azitenthe.
28 Kdor jih zažiga bo opral svoja oblačila in svoje telo umil v vodi in potem bo prišel v tabor.
Munthu amene azitenthe achape zovala zake ndi kusamba. Pambuyo pake alowe mu msasa.
29 To bo med vami zakon na veke, da boste v sedmem mesecu, na deseti dan meseca, ponižali svoje duše in sploh ne boste počeli nobenega dela; naj bo to nekdo iz vaše lastne dežele ali tujec, ki začasno prebiva med vami,
“Ili likhale lamulo lanu lamuyaya: Mwezi wachisanu ndi chiwiri, pa tsiku la khumi la mwezi, mugonje pamaso pa Yehova. Musamagwire ntchito iliyonse, kaya ndinu mbadwa kapena mlendo amene akukhala pakati panu,
30 kajti na ta dan bo duhovnik opravil spravo za vas, da vas očisti, da boste pred Gospodom lahko čisti pred vsemi svojimi grehi.
chifukwa tsiku limeneli kudzachitika mwambo wopepesera machimo anu, kukuyeretsani kuti mukhale oyeretsedwa ku machimo anu pamaso pa Yehova.
31 To vam bo šabatni počitek in svoje duše boste strli, po zakonu na veke.
Limeneli ndi tsiku lanu la Sabata lopumula, ndipo muzigonja pamaso pa Yehova. Limeneli ndi lamulo lanu la muyaya.
32 Duhovnik, ki ga bo mazilil in ki ga bo uméstil, da služi v duhovniški službi na mestu njegovega očeta, bo opravil spravo in si nadel lanena oblačila, torej sveta oblačila,
Wansembe amene wadzozedwa ndi kupatulidwa kuti akhale wansembe kulowa mʼmalo mwa abambo ake ndiye azichita mwambo wopepesera machimo atavala zovala zake zosalala ndi zopatulika.
33 in ta bo opravil spravo za sveto svetišče in ta bo opravil spravo za šotorsko svetišče skupnosti in za oltar in ta bo opravil spravo za duhovnike in za vse ljudstvo skupnosti.
Adzachite mwambo wopepesera machimo Malo Wopatulika, tenti ya msonkhano ndi guwa lansembe. Adzachitenso mwambo wopepesera anzake ndi gulu lonse la anthu.
34 To vam bodi večen zakon, da enkrat letno opravite spravo za Izraelove otroke, za vse njihove grehe.« In storil je, kakor je Gospod zapovedal Mojzesu.
“Ili likhale lamulo lanu lamuyaya. Mwambo wopepesera machimo uzichitika kamodzi pa chaka chifukwa cha machimo a anthu onse.” Ndipo Mose anachita monga momwe Yehova analamulira.